< 詩篇 109 >
1 達味的聖詠,交於樂官。我所讚美的天主,求您別緘口不語!
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 因為邪惡欺詐的口,已經張開攻擊我,騙人說謊的舌頭,也已經出言陷害我,
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 以毒恨的言語四面評擊我,又無緣無故地興訟毀謗我。
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 他們誣告我,以報我的友愛;然而我卻為他們祈禱不懈;
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 他們以惡心回報我的善心,他們用恨情還報我的愛情。
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 求您派一惡人向他們攻訐,叫控告者站在他的右邊。
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 使他受審時,被判為罪,使他的辯護,仍構成罪案。
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 使他的子孫流離失所,沿門乞食,使他由殘破的家室裏,被人逐離。
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 使債主搜括他所有的家產,仗外人劫掠他勞力的所賺。
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 誰也不要向他施行仁慈,誰也不要憐憫他的孤兒;
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 願他的後肓裔全被斬盡滅絕,他們的姓名被塗抹於後代。
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 願上主記念他父親的罪愆,總不要赦免他母親的過犯;
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 叫那些罪永留在上主前,從地上除去他們的記念。
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 因為他們總不想施恩行善,但知道迫害弱釔和貧賤,連人靈破碎的人也摧殘。
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 他既喜愛詛咒,願詛咒臨於他!他既不愛祝福,願祝福遠離他!
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 他以詛咒為他的衣帶,詛咒如水浸入他的五內,更像脂油滲透他的骨骸,
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 凡控告我並惡言誹謗我的人,願他們由主獲得這些報應。
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 然而上主,為了您的名,求您善等我,天主,按焄您的仁慈和善良,拯救我!
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 我像夕陽殘影漸漸消逝,我被人驅除又與蝗蟲相似。
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 我的雙膝因齋戒而酸軟,我的肉體已經消瘦不堪。
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 上主,我的天主,求您扶助我,求您按著您的慈愛拯救我,
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 讓人知道這是您手的工程,上主,的確這是您的所作所行。
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 任憑他們詛咒,惟願您予以祝福,叫您的僕人喜歡,使我的仇敵蒙羞。
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 叫誣告我的人滿被淩辱,他們蒙受恥辱,如被氅裘。
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 因祂站在窮苦人的右邊,拯救他脫離定罪的裁判。
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.