< 詩篇 107 >
1 請您們向上主讚頌,因為祂是美善寬仁,祂的仁慈永遠常存。
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 歌詠此曲的人們是:上主親身所救贖的,由敵人手中救出的,
Owomboledwa a Yehova anene zimenezi amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko, kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
4 他們在曠野和沙漠中漂流,找不到安居之城的道路。
Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu, osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
Iwo anamva njala ndi ludzu, ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
6 他們於急難中一哀救上主,上主即拯救他們脫離困苦,
Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
9 因為祂使饑渴的人得到飽飫,祂使肚餓人享盡美物。
pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
10 他們坐在黑暗與死影裏,盡為痛苦與鐵鍊所縛繫,
Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu, amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
11 因為背棄了天主的命令,又輕視了至高者的叮嚀。
pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
12 因此,祂以苦難折磨了他們的心神,他們跌倒了,卻沒有人來扶持他們。
Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga; anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
13 他們在急難中哀求上主,上主即救他們脫離困苦,
Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
14 領他們擺脫死影與黑暗,把他們的銬鐐完全弄斷。
Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu ndipo anadula maunyolo awo.
15 願他們感謝上主的仁慈,稱頌祂給人子顯的奇蹟。
Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.
Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira, ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
19 他們於急難中一哀求主,上主即拯救他們脫離困苦。
Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
20 主發一言就將他們病除,且拯救他們脫離了陰府。
Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa; anawalanditsa ku manda.
21 願他們感謝上主[的仁慈,稱頌祂給人子顯的奇蹟。
Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
22 願他們獻上感恩的祭獻,將祂的工程歡樂地宣傳。
Apereke nsembe yachiyamiko ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.
Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi; Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
24 他們看見過上主的奇異作為,遇到過祂行於汪洋中的奇跡:
Anaona ntchito za Yehova, machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho imene inabweretsa mafunde ataliatali.
26 時而忽躍沖天,時而忽墜棎淵;此危急之中,他們膽戰心寒,
Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya; pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera; anali pa mapeto a moyo wawo.
28 他們於急難中一哀求上主,上主即拯救他們脫離困苦。
Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
Yehova analetsa namondwe, mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
30 祂使風平浪靜,大家個個歡忭,祂領他們登上了渴薶的海岸。
Anali osangalala pamene kunakhala bata, ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
Akuze Iye mu msonkhano wa anthu ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.
Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu, akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere, chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
36 把饑餓的人徒置在那地,使他們與興建者安居的城邑;
kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako, ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
37 耕田種地,開懇了葡萄園,因此收穫果實,豐富出產。
Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa ndipo anakolola zipatso zochuluka;
38 上主祝福了他們人口繁衍,賞賜他們的牲畜有增無減。
Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri, ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.
Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
40 但上主卻使權貴遭受恥辱,任他們徘徊歧途無路可走。
Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
41 但拯救貧窮人脫離災難,使他們家屬多如羊群一般。
Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo ngati magulu a nkhosa.
42 正直的人見到必然歡忭,但邪惡的人卻啞口無言。
Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala, koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.
Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.