< 詩篇 104 >

1 【讚美造物的大主】我的靈魂請向上主讚頌!上主我的天主,您偉大無限,您以尊貴威嚴作您的衣冠:身披光明,好像外氅,展開蒼天,相似棚帳,
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 在水上建築您的宮殿,造了雲彩,作您的車輦,駕御著風翼,馳騁直前;
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 發出暴風,作您的使團,您以火燄,作您的隨員。
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 您奠定大地於基礎之上,您使大地永遠不再動盪;
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 以汪洋作氅衣把大地遮蓋,又以大水把群山峻嶺掩埋。
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 您一呵叱,大水即逃避,您一鳴雷,大水即驚退。
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 峻嶺血上突出,山谷向下沉落,各個都停在您指定的處所。
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 您劃定了界限,都不越過,免得大水再把大地淹沒。
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 您使水泉成為溪川,蜿蜒長流於群山間,
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 供給各種走獸水喝,使野驢也得以解渴。
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 天上飛鳥,在水邊宿臥,在枝葉痋叢中不斸鳴叫。
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 您從高樓宮殿上,灌溉山地,以出產的果實,飽飫普世;
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 您使青草和植物生出,餵養牲畜,為給人服務。又使土地產生出五穀,
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 美酒,人飲了舒暢人神,膏油,人用來塗面潤身,麵餅,人吃了增強人神。
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 上主的木喬木飽餐水澤,黎巴嫩香柏,主手所植。
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 鳥類在那裏壘窩築巢,鶴群以樹梢為家安臥。
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 高山崚嶺作羚羊的洞府,絕壁岩石作野兔的居處。
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 您造有月亮以定節季,太陽自知向西沉墜。
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 您造了黑暗,便有了夜晚,林中的野獸遂四出狂竄。
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 少壯的獅子恕吼覓姇,向天主要求食物充饑;
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 太陽升起的時候,牠們各自逃避,回到自己的洞穴,安然臥下休息;
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 於是人們出外謀生,各去勞動,直到黃昏。
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 上主,您的化工,何其浩繁,全是您以智慧所創辦,您的受造物遍地充滿。
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 看,汪洋大海,一望無際,其中水族,不可計數,大小生物,浮游不息。
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 在那裏有舟有船,往來航行,還有您造的鱷魚,遊戲其中。
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 這一切生物都瞻仰著您,希望您按時給它們飲食。
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 您一賜給它們,它們便會收集,您一伸您的手,它們便得飽食。
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 您若隱藏您的面容,它們便要恐懼,您若停止它們的呼吸,它們就要死去,再回
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 到它們由灰土出來的那裏去。
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 您一嚧氣萬物創成,您使地面,更新復興。
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 願上主的光榮,永世無窮;願上主喜樂,自己的化工!
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 祂一垂視大地,大地抖顫;祂一觸摸群山,群山冒煙。
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 只要我活著,我要歌頌上主,只要我存在.我要詠讚上主。
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 願我的頌詞使祂樂意,我要常在上主內歡喜。
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 願罪人由地面上滅跡,惡人不再存留於人世!我的靈魂,頌讚上主!阿肋路亞。
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< 詩篇 104 >