< 箴言 4 >

1 孩子,你們要聽父親的教訓,專心學習明智,
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 因為我把好教訓授給你們,你們不要拋棄我的規勸。
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 我也曾在父親面前作過孝子,在我母親膝下是唯一的嬌兒。
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 我父曾訓誨我說:你應留心牢記我的話,遵守我的命令,好使你生存;
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 你應緊握智慧,握住明智,不要忘記,也不要離棄我口中的教訓:
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 你若不捨棄她,她必護佑你;你若喜愛她,她必看顧你。
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 首先應爭取的是智慧,因此你應尋求智慧,應犧牲一切去爭取明智。
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 你若顯揚智慧,智慧也必顯揚你;你若懷抱她,她也必光榮你:
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 將華冠加在你的頭上,將榮冕賜給你。
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 我兒,你若聽取我的訓言,你必延年益壽。
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 我要教給你智慧的道路,引你走上正直的途徑:
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 這樣,你若行走,你的腳決不會受阻礙;即便你奔馳,也決不致顛仆。
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 你要堅持教訓,切勿把她拋棄;你應保存她,因為她是你的生命。
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 惡人的道路,你不要進去;壞人的途徑,你不要踏入;
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 反應躲避,不經其上;遠遠離去,繞道他往。
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 因為他們不作惡,不能入睡;不使人跌倒,就要失眠。
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 他們吃的是邪惡的餅,飲的是暴虐的酒。
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 但是,義人的途徑,像黎明的曙光,越來越明亮,直至成日中;
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 惡人的道路,卻宛如幽暗,他們不知道,要跌在何處。
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 我兒,你要注意我的訓言,側耳傾聽我的教導;
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 不要讓她離開你的視線,卻要牢記在心中。
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 因為,凡找著她的,必獲得生命;他整個身軀,必獲得健康。
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 在一切之上,你要謹守你的心,因為生命是由此而生。
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 你應摒絕口舌的欺詐,遠避唇舌的乖謬。
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 你的眼睛應向前直視,你的視線應向前集中。
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 你要修平你腳下的行徑,要鞏固你一切的路途。
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 你斷不可左傾右依,務使你的腳遠離邪惡。
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< 箴言 4 >