< 箴言 11 >

1 上主深惡假秤,卻喜愛法碼準確。
Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
2 傲慢來到,恥辱隨後而至;智慧只與謙遜人相處。
Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
3 正直的人,以正義為領導;背義的人,必為邪惡所毀滅。
Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
4 在上主盛怒之日,財富毫無用途;只有正義,能救人免於死亡。
Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
5 完人的正義,為他修平道路;惡人必因自己的邪惡而顛仆。
Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
6 正直的人,將因自己的正義而獲救;奸詐的人,反為自己的惡計所連累。
Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
7 惡人一死,他的希望盡成泡影;同樣,奸匪的期待也全然消失。
Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
8 義人得免患難,惡人反來頂替。
Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
9 假善人以口舌,傷害自己的近人;義人因有知識,卻得以保全。
Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
10 幾時義人幸運,全城歡騰;幾時惡人滅亡,歡聲四起。
Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
11 義人的祝福,使城市興隆;惡人的口舌,使城市傾覆。
Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
12 嘲弄自己朋友的人,毫無識趣;有見識的人,必沉默寡言。
Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
13 往來傳話的人,必洩露秘密;心地誠樸的人,方能不露實情。
Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
14 人民缺乏領導,勢必衰弱;人民的得救,正在於謀士眾多。
Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
15 為外人作保的,必自討苦吃;厭惡作保的,必自享安全。
Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
16 淑德的婦女,必為丈夫取得光榮;惱恨正義的婦女,正是一恥辱的寶座;懶散的人失落自己的財物,勤謹的人反取得財富。
Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
17 為人慈善,是造福己身;殘酷的人,反自傷己命。
Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
18 惡人所賺得的工資,是空虛的;播種正義者的報酬,纔是真實的。
Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
19 恒行正義,必走向生命;追求邪惡,必自趨喪亡。
Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
20 上主憎惡心邪的人,喜悅舉止無瑕的人。
Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
21 惡人始終不能逃避懲罰,義人的後裔必獲得拯救。
Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
22 女人美麗而不精明,猶如套在豬鼻上的金環。
Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
23 義人的心願必獲善報;惡人的希望終歸破滅。
Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
24 有人慷慨好施,反更富有;有人過於吝嗇,反更貧窮。
Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
25 慈善為懷的人,必得富裕;施惠於人的人,必蒙施惠。
Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
26 屯積糧食的人,必受人民咀咒;祝福卻降在賣糧食者的頭上。
Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
27 慕求美善的,必求得恩寵;追求邪惡的,邪惡必臨其身。
Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
28 信賴自己財富的人,必至衰落;義人卻茂盛有如綠葉。
Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
29 危害自己家庭的,必承受虛幻;愚昧的人,必作心智者的奴隸。
Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
30 義人的果實是生命樹,智慧的人能奪取人心。
Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
31 看義人在地上還遭受報復,惡人和罪人更將如何﹖
Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!

< 箴言 11 >