< 箴言 10 >

1 智慧的兒子使父親喜樂;愚昧的兒子,使母親憂愁。
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 不義之財,毫無益處;惟有正義,救人脫免死亡。
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 上主不忍義人受飢,卻使惡人大失所望。
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 游手好閒,使人貧窮;勤奮工作,使人富有。
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 夏季貯蓄的,是明智的孩童;秋收酣睡的是無恥的兒子。
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 上主的祝福在義人頭上,災禍卻使惡人啞口無言。
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 義人受人懷念祝福,惡人卻必身敗名裂。
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 心靈智慧的人,必接受命令;饒舌的愚的人,必自招喪亡。
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 走正路的,行路穩妥;走邪路的,終必敗露。
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 暗中擠眼的人,必引人煩惱;坦然規勸的人,必促進和平。
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 義人的口,是生命的泉源;惡人的口,是殘暴的淵藪。
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 仇恨引起爭端,愛情遮掩一切過失。
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 有見識的口唇上,可找著智慧;棍杖只是為打缺乏智慧者的脊背。
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 智慧的人,隱諱自己的學問;愚昧人的口,招致逼近的喪亡。
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 富人的財富,是他自己的堅城;窮人的零落,卻是他們的貧乏。
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 義人的薪金,用以維持生活;惡人的收入,卻只用來犯罪。
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 誰遵守勸告,必走向生命之路;誰輕視規勸,必自誤入迷途。
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 撒謊的唇舌,必暗藏仇恨;散播謠言的,必是愚昧人。
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 多言難免無過,明智的人必約束自己的唇舌。
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 義人的舌,貴若純金;惡人的心,賤似草芥。
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 義人的唇舌教育群眾,愚人必因缺乏心智而死亡。
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 使人致富的,是上主的祝福;營營的辛勞,卻無補於事。
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 愚昧人樂於作惡,明哲人樂於求智。
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 惡人畏懼的,反向他侵襲;義人的希望,終獲得應允。
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 暴風雨一過,惡人不復存在;義人卻根深蒂固。
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 懶漢之於派遣他的人,就如醋之於牙,煙之於目。
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 敬畏上主,將延年益壽;惡人的歲月,必要短縮。
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 義人的期待,終歸是喜樂;惡人的希望,終歸是失望。
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 上主的道路,是正人君子的保障;為作惡的人,卻是滅亡。
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 義人永不會動搖,惡人決不會久留地上。
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 義人的口,散播智慧;邪惡的舌,必被剷除。
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 義人的唇,常吐雅言;惡人的口,只說邪惡。
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< 箴言 10 >