< 民數記 34 >
Yehova anawuza Mose kuti,
2 你命令以色列子民說:你們幾時進入客納罕地,這地應是你們抽籤分配的產業。客納罕地的邊界是:
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 你們南部的地區,是由親曠野直到厄東邊境。你們南邊的邊界是:由鹽海的極端往東,
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 繞過阿刻辣賓高地的南部,經過親直達卡德士巴爾乃亞南部,再到哈匝爾阿達爾,經過阿茲孟,
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 西部的邊界:大海作你們的邊界,這是你們西方的邊界。
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 這邊界再伸至齊弗龍,直達哈匝爾厄南:這是你們北方的邊界。
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 由舍番邊界下延至阿殷東面的黎貝拉;由此邊界,再下延與基乃勒特海東岸相接。
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 此後,邊界再沿約但河下延,直達鹽海:這是你們疆土四周的邊界。」
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 梅瑟又吩咐以色列子民說:「這就是你們應抽籤分為產業的地方,是上主命令分給九個半支派的,
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 因為勒烏本子孫支派和加得子孫支派,為自己的家族已取得產業;默納協半支派也取得了自己的產業:
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 這兩個半支派,已在耶里哥對面,約但河東岸,向日出之地,取得了產業。」
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
Yehova anawuza Mose kuti,
17 這是給你們分配土地的人名:厄肋阿匝爾大司祭和農的兒子若蘇;
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 這些人的名字就是:猶大支派,是耶孚乃的兒子加肋布;
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 若瑟子孫:默納協子孫支派的首領,是厄缶得的兒子哈尼耳;
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 厄弗辣因子孫支派的首領,是色弗堂的兒子刻慕耳;
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 則步隆子孫支派的首領,是帕爾納客的兒子厄里匝番;
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 依撒加爾子孫支派的首領,是阿倉的兒子帕耳提耳;
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 阿協爾子孫支派的首領,是舍羅米的兒子阿希胡得;
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 納斐塔里子孫支派的首領,是阿米胡得的兒子培達赫耳。」
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 這些人是上主任命,為在客納罕地給以色列子民分配產業的人。」
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.