< 彌迦書 2 >

1 禍哉,那些在床上籌劃不義,圖謀行惡的人! 因為你們手中有能力,一到天亮,就去實行。
Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
2 他們想要田地,便去霸佔;朼想要房屋,便去奪取:以暴力對付業主和他的家族,物主和他的產業。
Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
3 為此上主這樣說:「看,我正在為這一家籌劃災禍,致令你們不能縮回你們的頭頸,也不能挺身前行,因為那是一個災禍的時刻。」
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
4 在那一日,人要作詩諷刺你們,唱這悲慘的哀哥說:「我們完全被搶掠了,我人民的基業已被人瓜分了,再無人歸還;我們的土地已分配給搶掠我們的人! 」
Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
5 因此,你們在上主的集會中,再沒有拉繩測量和抽籤的人。
Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
6 你們講說:「你們不要說預言。」「人不該預言這樣的事,恥辱決不會來到我們身上!
Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
7 雅各伯的家豈是可詛咒的﹖上主的氣量豈能變為狹小﹖難道這是衪的作風﹖衪的話豈不是有益於以色列子民﹖」
Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
8 「但是你們正像敵人一樣,起來攻擊我的人民,因為你們向沒有短衣的人索取長袍,向平安走路的人索取戰利品。
Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
9 你們驅逐我人民的婦女離開她們的快樂家庭,從她們的嬰兒身上,永遠奪去我的光榮。
Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
10 你們起來走吧! 因為這不是你們安息之所。為了不懂,這地必要遭受不可挽救的毀滅。」
Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
11 假若有人隨從虛妄而撒謊說:「我要對你預言清酒和醇酒。」這人必可作這民族的先知。
Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
12 我必要聚集雅各伯全民眾,我必要集合以色列的遺民,使他們合併在一處,有如羊欄裏的綿羊,有如牧場上的羊群,不再怕任何人。
“Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
13 開路者走在他們前面開道;他走在前面,眾人隨他穿門而過;他們的君王走在他們們前面,上主親作他們的響導。
Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”

< 彌迦書 2 >