< 士師記 20 >

1 於是以色列全體子民出動,從丹到貝爾舍巴,以及基肋阿得地,全會眾集合起來好像一個人一樣,來到米茲帕上主面前。
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa.
2 全民眾,即以色列各支派的首領,都參與天主百姓的集會;拿刀的步兵,共有四十萬。
Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga.
3 本雅明子孫也聽說以色列子民上到了米茲帕。以色列子民說:「這件惡事是怎樣發生的,請你們述說一遍! 」
Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”
4 那被殺的女子的丈夫肋末人就回答說:「我與我的妾來到屬本雅明的基貝亞,要在那裏過夜,
Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko.
5 基貝亞的公民起來攻擊我,夜間包圍我過夜的住宅,企圖殺害我,並把我的妾強姦致死。
Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa.
6 因為他們在以色列中間行了這窮兇極惡的醜事,我遂將我的妾切成碎塊,遍送以色列基業各地。
Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli.
7 以色列子孫,請你們說出你們的意見和對策。」
Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”
8 那時全體民眾好像一個人一樣都起來說:「我們中誰也不要返回自己的帳幕,誰也不要回自己的家,
Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake.
9 現在我們就要這樣對付基貝亞,抽籤進攻,
Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene.
10 由以色列各支派中,每百人抽十人,每千人抽百人,每萬人抽千人,給民眾運送軍糧;待眾人到達本雅明的基貝亞後,按照那城在以色列中間所行醜事報復它。」
Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.”
11 於是以色列人聯合起來攻擊那城,彼此合作有如一人。本雅明備戰
Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.
12 以色列眾支派差人往本雅明支派的各家說:「你們中間怎樣發生了這樣的惡事﹖
Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani?
13 現在你們把那些人,即基貝亞的無賴之徒,交出來,我們好處死他們,從以色列中鏟除這邪惡。」本雅明子孫卻不肯聽從他兄弟們以色列子民的呼聲;
Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.” Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo.
14 本雅明子孫反而從各城聚集起來,來到基貝亞,要與以色列子民交戰。
Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli.
15 那一天,本雅明人從各城來的共計兩萬六千拿刀的,基貝亞的居民尚未計算在內。
Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa.
16 在這些人中,還有特選的七百精兵,能左右開弓,個個能用機絃拋石,毫釐不爽。
Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.
17 本雅明人除外,以色列人共有四十萬拿刀的,個個都是戰士。兩次進攻失利
Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.
18 以色列子民起身上到貝特耳,求問天主說:「我們中誰該先上去與本雅明子孫作戰﹖」上主答說:「猶大先去。」
Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?” Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”
19 於是以色列子明早晨起來,對著基貝亞安營。
Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya.
20 以色列人出來要與本雅明人交戰,遂在基貝亞前面擺陣等待他們。
Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya.
21 本雅明子孫從基貝亞出來迎戰,那一天殺死了兩萬兩千以色列人。
A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko.
22 以後,眾以色列又鼓起勇氣,又在前一日布陣的地方布陣。
Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja.
23 事前,以色列子民先上到貝特耳,在上主面前哀哭,一直到晚上,然後求問上主說:「我們可否再去與我們的弟兄本雅明交戰﹖」上主答說:「可上去攻打。」
Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?” Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”
24 於是第二天,以色列子民又去攻打本雅明子孫。
Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo.
25 本雅明人第二天也從基貝亞出來與以色列人交戰,又殺死一萬八千以色列子民,都是拿刀的人。
Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.
26 以色列眾子民,即全民眾,又上到貝特耳,坐在上主面前哀哭,整日禁食到晚上;以後,在上主面前獻了全燔祭與和平祭。【
Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
27 那時天主的約櫃正在那裏,同時有亞郎的子孫厄肋阿匝爾的兒子丕乃哈斯在約櫃前供職。】以色列子民又求問上主說:「我們是否應再去與我們的弟兄本雅明人交戰﹖或是休戰﹖」上主答說:「你們應上去,因為我明天必將他們交在你們手中。」
Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko.
28 以色列人就在基貝亞四周設下伏兵。
Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?” Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”
29 第三天以色列子民上去攻打本雅明子孫,在基貝亞對面布陣,像前兩次一樣。
Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya.
30 本雅明子孫出來迎敵,被引出城外,在兩條大路上,─一條通往貝特耳,一條通往基貝紅,─像前兩次一樣,開始殺敵,在田野就殺死了約有三十個以色列人。
Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba.
31 本雅明子孫遂說:「他們像前次一樣,在我們面前打敗了。」但以色列子民卻說:「我們不如後退,引他們遠離城,到大路上來。」
Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.
32 當以色列眾人從他們的地方起來,在巴耳塔瑪爾布陣的時候,以色列的伏兵從革巴西邊埋伏的地方衝出來;
Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”
33 全以色列中所選出的一萬精兵齊來攻打基貝亞,戰爭非常激烈,但是本雅明人還不知道大禍臨頭。
Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba.
34 上主在以色列前打擊本雅明人,那一天以色列子民殺死本雅明人共有二萬五千一百,都是拿刀的人。
Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
35 這樣,本雅明子孫看出自己失敗。原來以色列人依仗在基貝亞所設下的伏兵,先在本雅明人前退怯;
Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo.
36 伏兵急速衝入基貝亞,衝進之後,用刀屠殺了全城的人。
Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa. Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya.
37 原先以色列人與伏兵約定,在城內放火,以煙火上騰為號。
Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga.
38 以色列人在戰場上撤退的時候,本雅明動手殺死以色列人約有三十人,他們想:「的確,他們如前一仗一樣,在我們前殺敗了。」
Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo,
39 當煙柱信號從城中上騰的時候,本雅明人轉過身來,見全城煙火沖天;
ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo. Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.”
40 那時以色列人也轉身回來;本雅明人大為驚慌,因為看見大禍臨頭,
Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba.
41 遂在以色列人面前轉向曠野的路上逃去,但戰士卻追蹤而至,從城裏出來的人也夾擊他們;
Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
42 這樣,以色列人擊潰了本雅明人,追擊他們,從諾哈蹂躪他們,直到革巴對面的東方之地。
Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo.
43 本雅明人陣亡一萬八千,都是勇士。
Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya.
44 其餘的人都轉身向著曠野逃往黎孟岩石,以色列人在路上又掃蕩了他們中五千人;以後,直追到革巴,擊殺了二千人。
Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa.
45 那一日,本雅明中陣亡的,共有二萬五千人,
Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.
46 所剩下的六百人,
Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa.
47 轉身逃往曠野,直到黎孟岩石,在黎孟岩石中住了四個月。
Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi.
48 以色列人又回到本雅明子孫那裏,把各城的人和牲畜,以及所遇見的都用刀殺盡;並將所經過的城池放火燒燬。
Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.

< 士師記 20 >