< 約書亞記 14 >
1 以下是以色列子孫在客納罕地所得的產業,那是司祭厄肋阿責爾和農的兒子若蘇厄,以及以色列子孫各支派的族長給他們劃分的,
Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
2 按照上主藉梅瑟吩咐的,以抽籤方式將土地分給又個支派,
Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
3 因為梅瑟在約旦河東,已將產業分給了另兩個支派;在他們中只沒有給肋未人分配產業。
Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
4 實際上,若瑟的子孫形成了兩個支派,即默納協和厄弗辣因。雖沒有分配給肋未人產業,卻給了他們一些城市作住所,和城郊草地,為牧放他們的的牲畜和羊群。
Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
5 上主怎樣吩咐梅瑟,以色列子民便怎樣進行劃分土地。
Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 猶大的子孫來到基加耳見若蘇厄時,刻納次族耶孚乃的兒子加肋布對若蘇厄說:「上主在卡德士巴爾乃亞,關於你和我對天主的人梅瑟所說的話,你是知道的。
Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
7 當上主的僕人梅瑟從卡德士巴爾乃亞,派我去偵探這地方時,我正十四歲,我全按我的良心回報了衪。
Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
8 當與一同上去的弟兄們使百姓喪氣時,我紿終服從了上主我的天主。
Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
9 那天梅瑟曾起誓說:你的腳所踏過[的地方,必定永久歸你和你們的子孫作為產業,因為你始終服從了上主我的天主。
Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
10 現在你看,自從上主對梅瑟說了這話,上主便照所應許的,使我又活了四十五歲,經過了以色列人在曠野漂流的時期,現在我已是八十五歲的人了。
“Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
11 但我現在還很強壯,如派我去的那一天一樣;不拘是打仗或是出入行動,我現在的力量和那時完全一樣。
Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
12 現在,請你將上主所許下的那座山地賜給我,因為那天你也曾聽過這話。固然,那裏有有阿納克人,城池又大又堅固,或許上主會與我同在,照上主所應許的,我能將他們趕走。」
Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
13 若蘇厄就祝福了他,將赫貝龍給了耶孚乃的兒子加肋布作為產業。
Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
14 因此赫貝龍直到今日仍為刻納次人耶孚乃的兒子加肋布的產業因為他紿終服從了上主以色列的天主。
Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
15 赫貝龍以前名叫克黎雅特阿爾巴,原是阿納克人中的一個偉人。以後國內昇平,再無戰事。
(Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.