< 約書亞記 13 >
1 若蘇厄年紀已老,上主對他說:「你年紀已老,但還有廣大的地區應當佔領。
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 還應佔領的地區:是培肋舍特人的整個地區,和革叔爾人的全境;
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 由埃及東方的史革爾人的全境,到北方的厄刻龍的邊界,這是屬客納罕人的區;那五個培肋舍特酋長所管轄的迦薩人、阿市多得人、阿市刻隆人、加特人和厄刻龍人地區,以南方的阿威人地區;
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 遇客納罕人的全境,即由漆東人的阿辣,直到阿費克,而直到阿摩黎人的邊界地區;
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 還有革巴耳人的地區,及東方的整個黎巴嫩區,由赫爾孟山麓巴耳加得,直到哈瑪特關口。
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 從黎巴嫩直到西方的米斯勒佛特瑪殷,所有住在山地的居民,所有的漆東人,我必從以色列民子面前,把他們趕走。你只管照我指示,將這地區抽籤分給以色列人作為產業。
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 現在你要這九地區分九支派和默納協半支派作為產業。」
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 默納協另半支派和勒烏本並加得二支派,已經得了梅瑟在約旦河東岸分給他們的產業;按上主的僕人梅瑟分給他們的產業,
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 是從阿爾農谷旁的阿洛厄爾起,包括谷中的城邑,全默爾巴高原,直到狄朋;
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 還有在赫市朋為王的阿摩黎人王息紅所有的城市,直到阿孟子民的邊疆;
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 還有基肋阿得和革叔爾人與阿加人的領土,以及全赫爾孟山,全巴商,一直到撒耳加;
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 又巴商王敖格的全國領土,他原是勒法因人最後的遺族,在阿市塔洛特和厄德勒為王。這些地方的人,都被梅瑟擊敗趕走了。
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 以色列子民郤沒有趕走革叔爾人和瑪阿加人,因此革叔爾和瑪阿加人直到? 直到現在仍住在以色列人中間。
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 惟有肋未沒有分得產業,因為上主以色列的天主自己是他們的產業,有如上主對他們所說的。
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 梅瑟給勒烏本支派,按照他們的家族,分了一份產業。
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 他們的地區,是從阿爾農谷旁的阿洛厄爾,包括中谷的城邑,直到默德巴整個高原。
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 赫市朋和在這高原所有的城市:狄朋、巴摩特巴爾、貝特巴爾默紅、
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 刻黎雅塔因、息貝瑪、山中盆地的責勒特沙哈爾、
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 高原上各城市,和在赫市朋為王的阿摩黎人王息紅的整個國土。梅瑟曾殺了 息紅和住在那個上的息紅藩屬,米德揚的酋長:厄威、勒狄、族爾、胡爾和勒巴。
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 以色列子民殺這些人時,也用刀殺了貝敖爾的兒子巴郎術士。
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 勒烏本子孫的地區以約旦河為界:以上是勒烏本子孫按照家族,分得作為產業的城市和所屬的村鎮。
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 梅瑟按照他們的家族,給加得支派,給加得子孫,分得了一份產業。
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 他們的地區是雅則爾,基肋阿得所有的城邑和阿孟人的一半土地,直到勒巴對面的阿洛厄爾;
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 又從赫市朋直到勒瑪特米茲帕和貝特尼,從瑪哈納殷到羅德巴爾的邊境;
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 還有谷中盆地的貝特哈蘭、貝特尼默辣、穌苛特、匝豐、赫市朋王息紅國中的其餘土地;以約旦河為界,沿約旦河東岸直到基乃勒特海的頂端:
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 以上是加得子孫按照家族,得作為產業的城市和所屬的村鎮。
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 梅瑟也給默納協半支派,給默納協半支派子孫,按照他們的家族,分了一份產業。
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 他們的地區是起自哈瑪納殷,包括全部巴商,即巴商王敖格的全部國土,巴商境內屬雅依爾的各村莊,共計六十村莊;
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 還有基肋阿得的一半和家族和敖格在巴商的都城阿市塔洛特和厄德勒:以上地區按照家族,分給了默納協的兒子瑪基爾的子孫,即瑪基爾的一半子孫。
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 以上是梅瑟在約旦河東岸,耶利哥面對摩阿布曠野裏,所劃分的產業。
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 至於肋未支派,梅瑟沒有給他們分配產業,因為上主以色列的天主自己是他們的產業,有如上主對他們所說的。
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.