< 約伯記 8 >
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 這些話你要講到幾時﹖你口中的話像狂風要到何時﹖
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 若你的子女得罪了他,他必將他們交於罪過的權勢下。
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 你若純潔正直,他必親來守護你,恢復你正義的居所。
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 因為我們由昨日纔有,本來一無所知;我們在世上的日月,好似影子。
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 蒲草不在池沼內,怎能長大﹖蘆葦沒有水,怎會長起﹖
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 凡忘記天主的,他的末路也是這樣:惡人的希望必化為泡影。
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 他倚恃自己的家,但它卻站立不住;他要依附自己的住所,住所卻不能久存。
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 若有人從原處把它拔除,那地必否認說:「我未曾見過它。」
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 天主決不棄捨完善的人,也決不支持惡人的勢力。
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 你的口角必再洋溢著喜悅,你的唇邊必再充滿歡笑。
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”