< 約伯記 37 >

1 為此我心戰慄,跳離它的原位。
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 你們且細聽天主的怒吼聲,聽那從他口中發出的巨響。
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 他令閃電炫耀天下,使之照射地極;
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 接著是雷聲隆隆,那是天主威嚴之聲;他的巨聲一響,沒有什麼能夠阻止。
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
5 天主每以巨響施行奇事,做出我們莫測的事。
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 他命令雪說:「落在大地上! 」對暴雨說:「傾盆而降! 」
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 人人都停止活動,為叫人知道,這是他的作為。
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 野獸逃回洞穴,臥於自己的窩中。
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 暴風來自南極密宮,嚴寒出自極北之地。
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 天主噓氣成冰,使大水凝成一片。
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 他使雲霧滿涵濕氣,使閃光穿過烏雲。
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 雷電照他的指示旋轉,全照他的命令實行於地面,
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 或為懲戒大地,或為施行恩惠。
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 約伯啊! 你且側耳細聽這事,立著沉思天主的奇事!
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 你豈能知道天主怎樣發命,怎樣使雲中電光閃爍﹖
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 雲怎樣浮動,全知者的奇妙化工,你豈能明白﹖
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 當南風吹起,大地鎮靜時,你的衣服豈不是發暖﹖
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 你豈能同他展開蒼天,使它堅固如鑄成的銅鏡﹖
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 我們昏愚,不能講話,請教訓我們怎樣答覆他。
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 我說話時,能給他講述些什麼新事﹖世人說話後,豈算是告訴他一項新聞﹖
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 人現今看不見陽光照耀天空,除非等到風過天晴。
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 金光來自北方,天主的左右有威嚴可怕的異光。
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 全能者是我們不可接近的,他的能力和正義,高超絕倫;他公義正道,決不欺壓。
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 所以人應敬畏他;但那心中自以為聰慧的,他卻不眷顧。
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

< 約伯記 37 >