< 約伯記 26 >

1 約伯回答說:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 無能為力的人,你怎樣援助了他﹖無力的手臂,你怎樣支持了他﹖
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 你給無知的人出過什麼主義,表現了你豐富的智慧﹖
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 你說這些話是指教誰﹖從你心裏發出的是什麼精神﹖
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 幽魂在地下打顫,海底與居於海底的,驚恐不已。
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 陰府在他前面顯露,死域也沒有遮掩。 (Sheol h7585)
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
7 他將北極伸張到太虛,將大地懸於虛無之上。
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 他將水包裹在濃雲中,托水的雲彩卻不破裂。
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 他遮蔽了滿月的面貌,使雲彩散佈其上。
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 在水面上劃了一圓圈,當作光明與黑暗的分界。
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 支天的柱子震動,因他的呵叱而戰慄。
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 他以威力使海洋動盪,以明智擊傷了海怪。
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 他一噓氣,天氣清朗;他親手戮穿了飛龍。
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 看啊! 這只是他行動的一端,我們所聽到的語句,何其細微! 他轟轟烈烈的作為,有誰能明瞭﹖
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

< 約伯記 26 >