< 約伯記 23 >

1 約伯回答說:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 直到今天,我還是痛苦的哀訴,他沉重的手掌,使我不得不呻吟。
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 惟願我知道怎樣能尋到天主,能達到他的寶座前,
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 好將我的案情向他陳訴,因為我口中滿了證詞!
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 唯願我知道他答覆我的話,明瞭他向我說什麼!
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 他豈能靠強力同我爭辯﹖決不,他必留神聽我。
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 如此,他會分辨出同他爭論的是個正直人,也許我可永久不再受裁判!
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 可是我往東行,他不在那裏;我往西行,也找不到他;
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 往北找,也看不見他;往南去,也見不到他。
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 他洞悉我所有的行動。他若試驗我,我必如純金出現。
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 我的腳緊隨著他的足跡,謹守他的道,總沒有偏離。
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 他所發的命令,我總沒有違背;他口中的訓言,我常保存在心中。
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 但他所決定的,誰能變更﹖他所樂意的,必要實行。
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 他為我注定的,必要完成;類似的事,還有很多。
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 因此,為了他,我很驚慌,一想起來就害怕。
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 天主使我的心沮喪,全能者使我恐怖。
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 因為我雖面臨黑暗,幽暗雖遮蓋我的面,我仍不喪氣。
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

< 約伯記 23 >