< 約伯記 11 >

1 納阿瑪人左法爾發言說:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
2 難道喋喋不休,就不需要答覆﹖難道多嘴多舌的人,就證明有理﹖
“Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
3 你的空談,豈能叫人緘默﹖你如此謾罵,難道無人使你羞愧﹖
Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
4 你說過:「我的品行是純潔的,我在你眼中是清白的。」
Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
5 但願天主講話,開口答覆你!
Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
6 將智慧的秘密,-即那難以理解的事-啟示給你,那麼你便知道,天主還忽略了你的一些罪過。
ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
7 你豈能探究天主的奧秘,或洞悉全能者的完美﹖
“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
8 完美高於諸天,你能作什麼﹖深於陰府,你能知道什麼﹖ (Sheol h7585)
Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
9 其量長過大地,闊於海洋。
Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
10 天主若經過,誰能扣留他﹖他若下了逮捕令,誰能阻擋他﹖
“Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
11 他洞悉人的虛偽,明察人的罪行,且無不注意。
Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
12 如此,愚蠢者纔可獲得智慧,野性驢駒纔能變為馴良。
Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
13 你若居心正直,向他伸開你的雙手;
“Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
14 你若將手中的罪惡除掉,不容不義留在你的帳幕內;
ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
15 那麼你定能仰首無愧,一定站立穩定,一無所懼;
udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
16 你必能忘卻痛苦,縱然想起,也必似水流去;
Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
17 你的壽命如日中之光華,縱有陰暗,仍如晨曦。
Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
18 因有希望,你纔感覺安全;因有保護,你纔坦然躺臥;
Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
19 你躺臥,無人敢來擾亂你,反而有多人來奉承你。
Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
20 然而惡人的眼必要昏花,他們安身之所必全毀壞,他們的希望只在吐出最後的一口氣。
Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”

< 約伯記 11 >