< 耶利米書 48 >

1 關於摩阿布:萬軍的上主,以色列的天主這樣說:「禍哉,乃波! 因為她遭受了浩劫;克黎雅塔殷蒙受了羞辱,被人攻佔;城堡被人侮辱,飽受驚恐。
Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
2 摩阿布的誇耀不再存在,在赫市朋就有人對她蓄意謀害:「來,我們將她剷除,使她不再是個民族! 」連你瑪德門,也要遭受蹂躪,在你後面緊隨著刀劍。
Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
3 由曷洛納因傳來哀號的聲音:蹂躪! 絕大的蹂躪!
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
4 摩阿布遭受了蹂躪,哀號之聲直達祚阿爾。
Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
5 他們哭泣著攀登路希特山坡;在曷洛納因斜坡上,人們可聽到悽慘的悲號:
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
6 請你們逃跑,拯救你們的性命! 願你們有如曠野中的楊柳!
Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
7 正因你信賴你的工作和財富,你也要被佔領;革摩士與自己的司祭和執事,也要一同充軍。
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
8 正如上主說了:蹂躪者必踏遍所有的城市,無一可以幸免;山谷必遭破壞,平原必摧殘。
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
9 你們給摩阿布立墓碑,因為她已全被消滅,她的城邑全化為無人居住的荒野。──
Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
10 那怠慢執行上主工作的,是可咒罵的;那制止自己的刀劍見血的,也是可咒罵的。──
“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
11 摩阿布自少年就享安逸,安息在自己的糟粕上,從沒有由一缸內,也從沒有被擄充軍,為此她的滋味仍然存在,她的香味還未改變。
“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
12 惟其如此,看,時日將到──上主的斷語──我必給她派傾倒的人來將她倒空,倒乾她的酒缸,打碎她的酒瓶;
Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 那時,摩阿布必因革摩士而受辱,就如以色列家因他們信賴的貝特耳而受辱一樣。
Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
14 你們怎能說:「我們是勇士,善戰的力士﹖」
“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 蹂躪摩阿布者上來進攻她的城市,精銳的少年,下去遭受殺戮─名叫「萬軍上主」的君王的斷語──
Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 摩阿布的災難已逼近前來,她的禍患加速進行。
Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
17 你們四鄰,凡認識她聲名的,都應對她惋惜說:「怎麼,威能的權杖,光榮的柄杖,也被折斷! 」
Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
18 住在狄朋的女兒! 你該由榮耀中下來,坐在乾地上,因為蹂躪摩阿布者已前來攻擊你,摧毀你的要塞。
“Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 阿洛厄爾的居民! 請你站在路旁觀望,向在逃亡出走的男女探問說:「發生了什麼事﹖」
Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
20 摩阿布已羞愧無地,因為已經瓦解;你們應悲哭哀號,在阿爾農宣布:「摩阿布遭受了蹂躪! 」
Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
21 懲罰已來到了平原之地,到了曷隆、雅哈茲和默法阿特;
Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22 到了狄朋、乃波和貝特狄貝拉塔因;
Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23 到了克黎雅塔殷、貝特加慕耳和貝特默紅;
Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24 到了克黎約特、波責辣和摩阿布地遠近的各城市。
Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 摩阿布的角已被砍下,她的手臂已被折斷──上主斷語。
Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
26 請你們灌醉她,因為她自高自大,反抗上主;摩阿布必要在自己的嘔吐中輾轉,連她自己也要成為笑柄。
“Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 以色列為你豈不是一個笑柄﹖難道她是被人發現在盜賊之中,為什麼你一提到她,就只有搖頭﹖
Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 摩阿布的居民! 你們該離棄城市,住在巖石間,彷彿在深谷懸崖邊緣結巢鵓鴿。
Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
29 我們聽說過摩阿布的驕傲,她的確驕傲無比;我們也聽說過她的強橫、矜誇、自大和心中的傲慢。
“Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
30 我知道她狂妄,好事空談,舉動輕率──上主的斷語──
Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 為此,我為摩阿布哀哭,為整個摩阿布悲號,為克爾赫勒斯人嘆息。
Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 息貝瑪葡萄園! 我為雅則爾痛哭,更為你痛哭;你的枝葉曾越過海洋,伸展到雅則爾;現在蹂躪者竟突然來摧殘你夏季的果實和秋季的收穫。
Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 摩阿布的田園已再沒有歡欣喜樂;我已使槽中無酒可榨;榨酒的不再榨酒,再也聽不見歡呼。
Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
34 赫市朋和厄肋阿肋的哀號遠達雅哈茲,由祚阿爾發出的呼聲,直達曷洛納因和厄革拉舍里史雅,因為尼默凌的水業已枯竭。
“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 如此,我要給摩阿布滅絕上高丘向神祇獻香的人──上主的斷語──
Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
36 為此我的心像笛蕭一般為摩阿布鳴咽,我的心像笛簫一般為克爾赫勒斯人鳴咽,因為他們獲得的積蓄,都已喪失。
“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 人人剃光頭髮,人人剪去鬍鬚,手上帶有割傷,腰間繫有苦衣;
Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 摩阿布所有的屋頂和廣場上,處處可聽到哀聲,因為我擊碎了摩阿布,有如擊碎一不中人意的器皿──上主的斷語──
Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
39 摩阿布崩潰得多麼悽慘! 你們真該嚎啕! 她是多麼含羞轉過背來! 摩阿布竟成了她四鄰的笑柄和恐怖。
“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
40 因為上主這樣說:「看,敵人好像老鷹飛翔,向摩阿布展開自已的翅膀,
Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 攻取了城池,佔領了要塞;在那一日,摩阿布的勇士必心志頹喪有如臨產的婦人。
Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 摩阿布必要消滅,不再成為一個民族,因為她自高自大,反抗上主。
Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 摩阿布的居民! 恐怖、陷阱和羅網齊來襲擊你──上主的斷語──
Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
44 逃脫了恐怖的,必落在陷阱裏;爬出了陷阱的,必為羅網纏住;在懲罰她的那年,我要給摩阿布召來這一切──上主的斷語──
“Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
45 逃命的人,筋疲力盡,站在赫市朋的陰影下;但是從赫市朋發出了火,從息紅宮中冒出了火焰,吞滅了摩阿布的首領,和騷動子民的頭目。
“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
46 禍哉,摩阿布! 革摩士的人民! 你算完了,因為你的兒子已被擄去充軍,你的女兒流為囚徒;
Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
47 雖然如此,在末日我仍要轉變摩阿布的命運──上主的斷語。至此是關於摩阿布的判決。
“Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

< 耶利米書 48 >