< 耶利米書 36 >
1 猶大王史約雅內的兒子約雅金第四年,上主有話傳給耶肋米亞說
Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 :「你拿卷冊來,寫上自我由約史雅時日,對你說話那一天以來,直到今日,關於耶路撒冷和猶大及列邦對你所說的一切話,
“Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
3 也許猶大家聽了我有意對他們施行的一切災禍,會各自離棄自己的邳道,叫我好寬恕他們的過犯和罪惡」。
Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
4 於是耶肋米亞叫了乃雅黎的兒子巴路克來;路克來依照耶肋米亞的口授,在卷冊上寫上了上主對先知說的一切話。
Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
5 耶肋米亞吩咐巴路克說:「我被阻止,不能到上主的殿宇去,
Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
6 所以你去,在一個禁食的日子上,誦讀卷冊上依我口授寫的上主的話,給在上主殿裏的全體人民聽,也讀給來自各城的全體猶大人聽,
Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
7 也許他們會向上主哀求,各自會離棄自己的邳道,因為上主對這人民用以恐嚇的憤恨和憤怒,真正厲害! 」
Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
8 乃黎雅的兒子巴路克全按耶肋米亞先知吩咐的做了:在上主殿宇裏,宣讀了卷冊上主的話。
Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
9 猶大王約史雅的兒子約雅金第五年九月,耶路撒冷全體人民以及從猶大城市來到耶路撒冷的全體人民,集合在上主面前宣佈禁食。
Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
10 巴路克就乘機在上主殿宇內,沙番的兒子革馬黎雅書記的房子那裏,即上院靠近上主殿宇新門的進口處,宣讀卷冊上耶肋米亞的話,給全體人民聽。
Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
11 沙番的兒子革馬黎雅的兒子米加雅,聽了卷冊上所有的上主的話,
Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
12 就下到王宮書記的事務所內,看,眾首長都正坐在那裏,有書記厄里沙瑪,舍瑪雅的兒子德拉雅,阿革波爾的兒子厄耳納堂,沙番的兒子革馬黎雅,哈紇尼雅的兒子漆德克雅和其餘的首長。
anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
13 米加雅就把自己在巴路克給人民宣讀卷冊時所聽到的所有話,告訴了他們。
Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
14 眾首長便派乃塔尼雅的兒子猶狄和雇史的兒子舍肋米亞到巴路克那裏說:「請你來,並請你隨手帶上你讀給人民的那軸卷冊」。乃肋米亞的兒子巴路克立即手內拿上那軸卷冊,到他們那裏去了。
Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
15 你們對他說:「請坐,讀給我們聽! 」巴路克讀給他們聽了。
Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
16 他們聽了這一切話,彼此不勝驚慌說:「我們必須將這一切話稟告君王! 」
Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
17 然後問巴路克說:「請你告訴我們:你怎樣由耶肋米亞的口授寫了這一切話﹖」
Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
18 巴路克答覆他們說:「這一切話都是他口授給我的,我只不過用筆記錄在這卷冊上」。
Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
19 於是首長對巴路克說:「你快去和耶肋米亞藏起來,不要讓人知道你們藏在哪裏」。
Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
20 然後他們一同到內殿去拜見君王,那卷冊卻留在書記厄里沙瑪室內,只將這一切話稟告了君王。
Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
21 君王於是打發猶狄去取那軸卷冊;猶狄由書記厄里沙瑪室內取了來,讀給君王和環立在君王旁的眾朝臣聽。
Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
22 那時正是九月,君王住在冬宮裏,面前正燒著一盆火,
Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
23 猶狄只讀了三四行,君王就用書記的刀把它割下,拋在火盆裏,直到那卷冊在火盆內被燒盡。
Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
24 君王與眾臣僕言這一切話,毫不害怕,也不撕裂自己的衣服,
Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
25 雖然厄耳納堂和德拉雅及革瑪黎雅曾苦苦哀求君王不要燒毀那軸卷冊,
Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
26 反命王子耶辣默耳,阿次黎耳的兒子色辣雅和哈德耳的兒子舍肋米雅,去逮捕書記巴路克和先知耶肋米亞;但是上主卻將他們藏起來了。
Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
27 君王焚燒了那軸載有巴路克由耶肋米亞口授記錄的話的卷冊以後,有上主的話傳給耶肋米亞說:
Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
28 「你拿另一卷冊來,寫上猶大王約雅金所燒毀的前一軸卷冊上的一切話。
“Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
29 關於猶大王約雅金你應說:上主這樣說:你燒毀了這軸卷冊說:為什麼你在上面寫道:巴比倫王必來破壞這地方,消滅這地方 的人民和獸﹖
Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
30 為此上主關於猶大王約雅金這樣說:他必沒有人繼坐達味的寶座,死後必棄屍原野,遭受日晒夜露。
Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
31 對他和他的後裔及臣僕,我要懲罰他們的罪惡,給他們和耶路撒冷居民及猶大人,召來我向他們預告,他們卻不理會的一切災禍」。
Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
32 耶肋米亞就拿來另一軸卷冊,交給書記乃黎雅的兒子巴路克。巴路克依照耶肋米亞的口授,在上面筆錄了猶大王約雅金,在火中燒毀了的那卷冊上所有的話;並且還加添了許多相類似的話。
Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.