< 耶利米書 3 >
1 試問:若男人離棄了自己的妻子,她離開他而另嫁了別人,前夫豈能再回到她那裏去﹖像這樣的女人,豈不是已全被玷污了嗎﹖你已與許多愛人行淫,你還想回到我這裏來嗎﹖──上主的斷語──
“Ngati munthu asudzula mkazi wake ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina, kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo? Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri? Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri. Komabe bwerera kwa ine,” akutero Yehova.
2 你舉目環顧高丘.看看在什麼地方你沒有受過玷污﹖你坐在路旁等候他們,像個在阿刺伯人,以你淫亂和邪惡玷污了這土地。
“Tayangʼana ku zitunda zowuma. Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama? Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu. Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu ndi ntchito zanu zoyipa.
3 秋雨不降,春雨不來。你具有娼妓的面孔,仍然不知羞恥。
Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula, ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe. Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere; ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.
4 從此以後,你要向我喊說:「我父! 你是我青年時的良友!」
Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,
5 心想:「衪豈能永遠發怒,懷恨到底﹖」看,你雖如此說,卻仍盡力作惡。
kodi mudzandikwiyira nthawi zonse? Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’ Umu ndimo mmene umayankhulira, koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”
6 在若史雅為王的時日裏,上主對我說:「失節的以色列所做的,你看見了沒有﹖她上到一切高處上,走到所有的綠樹下,在那裏行淫。
Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko.
7 我以為她作了這一切以後,會回到我這裏來;但是她沒有回來。她失信的姊妹猶大也看見了此事:
Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi.
8 雖然看見了我為了失節的以色列所犯的種種姦淫,而命她離去,給了她休書,她這失信的姊妹猶大卻不害怕,竟然也去行淫。
Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo.
9 由於她輕易行淫,與石碣和木偶淫亂,玷污了這土土也。
Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo.
10 儘管這樣,她失信的姊妹猶大回到我這裏來,仍不是全心,只是假意──上主的斷語。」
Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.
11 上主於是對我說:「失節的以色列比失信的猶大 ,更顯得正義。
Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda.
12 你去向北方宣布這些話說:失節的以色列! 請你歸來──上主的斷語──我不會對你怒容相向,因為我是仁慈的──我不會永遠發怒,
Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti, “‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale, pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.
13 只要你承認你的罪過,承認背叛上主你的天主,在一切綠樹下,與異邦神祗恣意相愛,沒有聽我的聲音,上主的斷語。
Ungovomera kulakwa kwako kuti unawukira Yehova Mulungu wako. Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo pansi pa mtengo uliwonse wogudira, ndiponso kuti sunandimvere,’” akutero Yehova.
14 失節的女子,妳們歸來──上主的斷語──因為我是你們的主人,我要選取妳們,每城選一人,每族選二人,領妳們進入熙雍;
“Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse.
15 在那裏給妳們一些隨我心意的牧者,以智慧和明智牧養妳們。
Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha.
16 你們在這地上繁衍增值的時日裏──上主的斷語──人不再提「上主的約櫃」,也不再思念,不再追憶,不再關懷,不再製造。
Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,” akutero Yehova.
17 那時,人要稱耶路撒冷為「上主的御座」,萬民要奉上主的名,匯集在耶路撒冷,不再隨從自己邪惡而頑固的人行事。
Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa.
18 在那些時日內,猶大家與以色列家同行,從北方起回到我賜給了你們祖先作基業的地內。
Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.
19 我曾想過:多麼願意你像一個兒子,賜給你賞心悅目的土地,列國中最美好的領土,我以為你會以「我父」稱呼我,不會轉身遠離我;
“Ine mwini ndinati, “‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga ndikukupatsani dziko labwino kwambiri, cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’ Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’ ndi kuti simudzaleka kunditsata.
20 但是,你們,以色列家對待我,正如對自己良友不忠的婦女──上主的斷語。
Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake, momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,” akutero Yehova.
21 在荒丘上可聽到一片喧嚷:那是以色列子民的哀號哭泣,因為他們走入了邪途,忘卻了自己的天主。
Mawu akumveka pa magomo, Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo chifukwa anatsata njira zoyipa ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.
22 歸來! 失節的子民,讓我療愈你們的失節。」「看,我回到你這裏,的確,你是上主,我們的天主。
Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika; ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.” “Inde, tidzabwerera kwa Inu pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.
23 誠然丘嶺和山卜的狂歡盡是虛幻;唯在上主,我們的天主那裏,有以色列的救援。
Ndithu kupembedza pa magomo komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu. Zoonadi chipulumutso cha Israeli chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.
24 可恥的神祗,自我們幼年就吞噬了我們祖先的收入,他們的羊群、牛群和子女。
Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu la ntchito za makolo athu, nkhosa ndi ngʼombe zawo, ana awo aamuna ndi aakazi.
25 讓我們躺臥在我們恥辱中,讓我們以羞慚遮蓋我們,因為我們和我們的祖先,自我們幼年直到今日,得罪了上主我們的天主,從來沒有聽從上主我們的天主的聲音。」
Tilekeni tigone pansi mwa manyazi, ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe. Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu, ife pamodzi ndi makolo athu kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”