< 以賽亞書 44 >
1 但是現在,我的僕人雅各伯!我所揀選的以色列!你聽罷!
Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
2 那造成你,從母胎形成你,且協助你的上主這樣說:「我的僕人雅各伯!我所揀選的耶叔戎,你不要害怕!
Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
3 因為我要把水倒在乾地上,使豪雨落在旱陸上;我要把我的神傾住在你的苗裔身上,把我的祝福降在你的子孫身上。
Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
5 這個說:「我是上主的,」那個要起雅各伯的名字,另一個要在手上寫 :「屬於上主,」並要起以色列的名號。
Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
6 上主,以色列的君王,救主,萬軍的上主這樣說:「我是元始,我是終末,在我以外沒有別的神。
“Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
7 誰相似我﹖讓他前來伸述,讓他說明,給我拿出證據來!誰能從永遠預言未來的事,請他告訴我們快要發生的事罷!
Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
8 你們不必驚慌,不用害怕!我不是早已告訴過你,早已宣布了嗎﹖你們是我的證人,在我以外還有別的神嗎﹖決沒有別的磐石!我一個也不認識!」
Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
9 製造偶像的人都是虛無,他們所喜愛的,也毫無用處;他們的見證人一無所見,毫無所知,必將蒙受恥辱。
Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
11 看哪!凡作他夥伴的,都要蒙受恥辱,因為製造偶像的,也只是人而已! 讓他們集合起來一同前來罷!他們必要驚慌羞愧!
Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
12 鐵匠先在炭火上工作,再用鎚子打成偶像,他用大力的手臂工作,當饑餓時,也就沒有力量;沒有水喝,他就疲勞不堪。
Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
13 木匠伸展繩墨,用筆劃線,後拿刨子刨平,再用圓規測量,做成一個人形,具有人的美麗,好供在廟裏。
Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
14 人先去砍伐一塊香柏,或取一塊榆木,或橡木;或在樹林中選一塊堅固的木料,或自己種植一棵月桂樹,讓雨水使之長大。
Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
15 這些木料原是為人作燃料,原可用來取煖,也可燃燒烘烤麵包;人卻用它來作神像去恭敬,或做偶像去叩拜:
Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
16 人把一半木頭投入火中燃燒,在火炭上烤肉吃;待吃飽了烤肉,又取了煖,遂說:「哈哈!我暖和了,也覺得有了火!」
Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
17 遂用剩下的一半作了一個神像,一個偶像,向它叩拜,俯伏懇求說:「求你救我,因為你是我的神!」
Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 他們不瞭解,也不覺悟,因為他們的眼糊住了,什麼也看不見;他們的心也不知覺悟,
Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 也不回心想一下,也不會明智通達地說:「一半木頭我已投入火中燒了,並在火炭上烤了麵包,烤了肉吃;我竟將剩下的一半作了一個怪物,向這塊木頭敬拜。」
Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 他所追求的僅是一把灰;他迷惑的心領他走入歧途,而不能自拔,也不會問說:「我右手所拿的不是虛無嗎﹖」
Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
21 雅各伯啊!你要記住這些事!以色列啊!你也應記住,因為你是我的僕人,我造了你,是叫你作我的僕人。以色列啊!我決不會忘了你!
Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
22 我消除了你的罪過,有如煙消;我消除了你的愆尤,有如雲散;歸依我罷!因為我救贖了你。
Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
23 諸天,歡騰罷!因為上主作了這一切;地下的深淵,歡呼罷!山嶺、森林和其中的樹木,高聲歌唱罷!因為上主拯救了雅各伯,在以色列顯揚了自己。
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
24 你的救主,由母胎形成你的上主這樣說:「我是創造萬有的上主,只有我展開了諸天,佈置了大地,誰與我同在﹖
Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
25 是我破壞了占卜者的預兆,使巫士成為愚妄,使智者退後,使他們的知識變為愚蠢,
Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
26 是我叫我僕人們的話實現,叫我使者們的計謀成功;是我論及耶路撒冷說:「你必要有人居住。」論及猶大各城說:「你們要被重建,我必要重建你們的廢址。」
Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
27 是我對深淵說:「你必涸竭,我要使你的河流乾涸。」
Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
28 是我論及居魯士說:「他是我的牧人,他要履行我的一切計劃,要吩咐重建耶路撒冷,奠基重修聖殿。」
Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”