< 創世記 23 >

1 撒辣一生的壽數是一百二十歲。
Sara anakhala ndi moyo zaka 127.
2 撒辣死在客納罕地的克黎雅特阿爾巴,即赫貝龍。亞巴郎來舉哀哭弔撒辣;
Anamwalirira ku Kiriyati-Araba, kumeneku ndi ku Hebroni, mʼdziko la Kanaani, ndipo Abrahamu anapita kukakhuza maliro a Sara, namulirira.
3 然後從死者面前起來,對赫特人說道:
Kenaka Abrahamu ananyamuka pamene panali mtembo wa mkazi wakepo kupita kukayankhula ndi anthu a ku Hiti. Ndipo anati,
4 「我在你們中是個外鄉僑民,請你們在這裏賣給我一塊墳地,我好將我的死者移去埋葬。」
“Ine ndine mlendo wongoyendayenda kwanu kuno. Bwanji mundigulitse malo woti akhale manda kuti ndiyikepo thupi la mkazi wanga.”
5 赫特人答覆亞巴郎說:「
Anthu a ku Hiti aja anamuyankha Abrahamu kuti,
6 先生,請聽:你在我們中是天主的寵臣,你可在我們最好的墳地埋葬你的死者,我們沒有人會拒絕你,在他的墳地內埋葬你的死者。」
“Tatimverani mbuye wathu, inu ndinu mwana wa mfumu wamkulu pakati pathu. Chonde ikani thupi la mkazi wanu mʼmanda aliwonse amene mungafune. Palibe mmodzi wa ife amene adzakukanizani manda ake kuti musayike mkazi wanu.”
7 亞巴郎遂起來,向當地人民赫特人下拜,
Tsono Abrahamu anayimirira naweramira anthu a dziko la Hiti aja
8 然後對他們說:「如果你們實在願意我將死者移去埋葬,請你們答應我,為我請求祚哈爾的兒子厄斐龍,
nati, “Ngati mwaloladi kuti ndiyike mkazi wanga kuno, ndiye ndimvereni. Mundipemphere kwa Efroni mwana wa Zohari
9 要他賣給我他那塊田地盡頭所有的瑪革培拉山洞;要他按實價在你們面前賣給我,作為私有墳地。」
kuti andigulitse phanga la Makipela, limene lili kumapeto kwa munda wake. Mumupemphe kuti andigulitse pamtengo wake ndithu inu mukuona kuti akhale manda.”
10 當時,厄斐龍也坐在赫特人中間。這赫特人厄斐龍遂在聚於城門口的赫特人面前,高聲答覆亞巴郎說:「
Pamenepo nʼkuti Efroni Mhiti ali pomwepo pakati pa anthuwo amene anabwera ku chipata cha mzindawo. Ndipo onse akumva anamuyankha Abrahamu
11 先生,不要這樣。請聽我說:我送給你這塊田,連其中的山洞,也送給你。我願在我同族的人民眼前送給你,埋葬你的死者。」
nati, “Ayi mbuye wanga tandimverani, ine ndikukupatsani mundawo ndiponso phanga limene lili mʼmenemo. Ndikukupatsani malowa pamaso pa anthu a mtundu wanga. Chonde ikani mtembo wamkazi wanu.”
12 亞巴郎又在當地人民面前下拜,
Apo Abrahamu anaweramanso mwaulemu pamaso pa anthu a mʼdzikolo
13 然後對當地人民高聲向厄斐龍說:「假如你樂意,請你聽我說:我願給你地價,你收下後,我才在那裏埋葬我的死者。」
ndipo anthu onse akumva Abrahamu anati kwa Efroni, “Ngati kungatheke, chonde ndimvereni. Ine ndichita kugula mundawu. Landirani ndalama za mundawu kuti ine ndiyike mkazi wanga mʼmenemo.”
14 厄斐龍答覆亞巴郎說:「
Koma Efroni anamuyankha Abrahamu nati,
15 先生,請聽我說:一塊值四百「協刻耳」銀子的地,在你和我之間,算得什麼! 你儘管去埋葬你的死者罷! 」
“Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.”
16 亞巴郎明白了厄斐龍的意思,便照他在赫特人前大聲提出的價值,按流行的市價稱了四百「協刻耳」銀子給他。
Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito.
17 這樣,厄斐龍在瑪革培拉面對瑪默勒的那塊田地,連田地帶其中的山洞,以及在田地四周所有的樹木,
Choncho munda wa Efroni wa ku Makipela umene unali kufupi ndi Mamre, kuphatikiza munda, phanga linali mʼmenemo pamodzi ndi mitengo yonse ya mʼmundamo, zinaperekedwa
18 當著聚在城門口的赫特人面前,全移交給亞巴郎作產業。
kwa Abrahamu ngati chuma chake pamaso pa anthu onse a ku Hiti amene anabwera ku chipata cha mzindawo.
19 事後,亞巴郎遂將自己的妻子撒辣葬在客納罕地,即葬在那塊面對瑪默勒,(即赫貝龍),瑪革培拉田地的山洞內。
Zitatha izi, Abrahamu anayika mkazi wake Sara mʼphanga la mʼmunda wa ku Makipela, kufupi ndi ku Mamre (kumene ndi ku Hebroni) mʼdziko la Kanaani.
20 這樣,這塊田地和其中的山洞,由赫特人移交了給亞巴郎作為私有墳地。
Choncho Ahiti anapereka munda pamodzi ndi phanga la mʼmenemo kwa Abrahamu kuti akhale manda.

< 創世記 23 >