< 以西結書 7 >

1 上主的話傳給我說:「
Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
2 人子,你要說:吾主上主這樣對以色列地域說:結局到了,大地四極的結局到了。
“Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti: “Chimaliziro! Chimaliziro chafika ku ngodya zinayi za dziko.
3 現今你的結局已到:我要向你發洩我的憤怒,按你的行為裁判你,按照你所有的醜行報復你。
Chimaliziro chili pa iwe tsopano. Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe. Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
4 我的眼決不憐視你,一點也不顧惜你;反之,我必按照你的行為報復你,使你的醜惡彰顯在你中間;這樣,你們必承認我是上主。
Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako. Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
5 吾主上主這樣說:「看,災禍,那唯一的災禍來了。
“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo! Taona chikubwera!
6 結局到了,那對付你的結局到了,看,已來到目前。
Chimaliziro chafika! Chimaliziro chafika! Chiwonongeko chakugwera. Taona chafika!
7 當地的居民啊! 惡運已臨於你,時辰已到,恐怖的日子已近,山上再聽不到歡呼的聲音。
Inu anthu okhala mʼdziko, chiwonongeko chakugwerani. Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
8 現今我就快要向你發洩我的憤怒,在你身上盡洩我的怒火,要按照你的行為裁判你,按照你所有的醜行報復你。
Ine ndili pafupi kukukwiyirani, ndipo ukali wanga udzathera pa iwe; Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
9 我的眼決不憐視,一點也不顧惜;反之,我要照你的行為報復你,使你的醜惡彰顯在你中間:這樣你們必承認我是施罰的天主。」 「
Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
10 看,那日子確已來到,惡運已定,暴行開花,傲慢發芽。
“Taona, tsikulo! Taona, lafika! Chiwonongeko chako chabwera. Ndodo yaphuka mphundu za maluwa. Kudzitama kwaphuka.
11 殘暴興起,成為作惡的權杖;他們中將一無所存,他們的財富沒有了,豪華不見了,光榮一無所留。
Chiwawa chasanduka ndodo yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo. Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo. Palibiretu ndipo sipadzapezeka munthu wowalira maliro.
12 時辰到了,日子近了;買主不要歡樂,賣主也不要憂愁,因為怒火要降在一切財富上。
Nthawi yafika! Tsiku layandikira! Munthu wogula asakondwere ndipo wogulitsa asamve chisoni, popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
13 賣主雖還活著,但不得再贖回他所賣的,因為懲罰一降在一切民眾身上,誰也不能再挽回。無人在罪惡中能保全生命。
Wogulitsa sadzazipezanso zinthu zimene anagulitsa kwa wina chinkana onse awiri akanali ndi moyo, pakuti chilango chidzagwera onsewo ndipo sichingasinthike. Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense amene adzapulumutsa moyo wake.
14 你們吹喇叭,將一切準備便當;但無人出征上陣,因為我的怒火要降在所有人民身上。
“Lipenga lalira, ndipo zonse zakonzeka. Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo, pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
15 外有刀兵,內有瘟疫饑荒;凡在鄉間的,要喪身刀下;在城中的,要死於瘟疫饑荒。
Ku bwalo kuli kumenyana ndipo mʼkati muli mliri ndi njala. Anthu okhala ku midzi adzafa ndi nkhondo. Iwo okhala ku mizinda adzafa ndi mliri ndi njala.
16 那些僥倖逃亡的,到了山中,必像谷中哀鳴的鴿子,各人悲泣自己的罪惡。
Onse amene adzapulumuka ndi kumakakhala ku mapiri, azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa. Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
17 人人雙手疲憊無力,雙膝軟弱如水,
Dzanja lililonse lidzalefuka, ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
18 身穿苦衣,都為恐怖所籠罩;每人面帶羞慚,頭頂完全剃光。
Iwo adzavala ziguduli ndipo adzagwidwa ndi mantha. Adzakhala ndi nkhope zamanyazi ndipo mitu yawo adzameta mpala.
19 他們將自己的銀子丟在街頭,金子為他們成了污穢之物;他們的金銀,在上主發怒之日,不能拯救他們;金銀不能使他們充饑,不能填滿他們的肚腹,因為金銀是他們犯罪的絆腳石。
“Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa. Siliva ndi golide wawo sizidzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala, kapena kukhala okhuta, pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20 他們既然把自己華麗的裝飾品作為誇耀的東西,做成醜惡的偶像和怪物;
Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina. Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa kukhala zowanyansa.
21 所以我要使偶像成為他們的不潔之物,我要把它交於外邦人手中作勝利品,給本地匪徒作為掠物,而予以褻瀆。
Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe. Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda ndi kudziyipitsa.
22 我要轉面不看他們,讓外人褻瀆我的寶藏,讓野人侵入而加以褻瀆,
Ine ndidzawalekerera anthuwo ndipo adzayipitsa malo anga apamtima. Adzalowamo ngati mbala ndi kuyipitsamo.
23 並用來製造鎖鏈;因為此地充滿了血債,城中充滿了殘暴。
“Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24 為此,我必叫最兇惡的異民來佔據他們的房舍,消滅他們傲慢的勢力,並使他們的聖所受到褻瀆。
Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa kuti idzalande nyumba zawo. Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25 當恐怖來臨時,他們尋求救援,卻沒有救援。
Nkhawa ikadzawafikira adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26 禍上加禍,噩耗接踵而來;那時人向先知要求異像,卻毫無所得;司祭失去了教言,長老沒有了主意,
Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake, ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake. Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri. Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo, ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27 君王失聲痛哭,王侯驚惶失措,當地居民的手顫動無力。我必按他們的行為向他們報復,照他們的功過裁判他們:這樣,他們必要承認我是天主。」
Mfumu idzalira, kalonga adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha. Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo, ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.

< 以西結書 7 >