< 出埃及記 4 >

1 梅瑟回答說:「他們必然不肯相信我,也不肯聽我的話,而對我說:上主沒有顯示給你。」
Mose anayankha, “Aisraeliwo sakandikhulupirira ndipo sakandimvera. Iwowo adzati, ‘Yehova sanakuonekere iwe.’”
2 上主問他說:「你手裏拿的是什麼﹖」他回答說:「一根棍杖。」
Ndipo Yehova anamufunsa nati, “Nʼchiyani chili mʼdzanja lakolo?” Mose anayankha kuti, “Ndodo.”
3 上主說:「將棍杖扔在地上! 」他便將棍杖扔在地上,棍杖即刻變成了一條蛇;梅瑟一見,就逃避了。
Yehova anati, “Tayiponya pansi.” Mose anayiponya pansi ndipo inasanduka njoka ndipo anayithawa.
4 上主向梅瑟說:「伸手捉著蛇的尾巴! ─他便伸手捉住,那條蛇在他手裏又變成一根棍杖。─
Kenaka Yehova anati kwa iye, “Igwire mtchira.” Ndipo Mose anayigwira mchira njokayo ndipo inasandukanso ndodo mʼdzanja lake.
5 好叫他們相信上主,他們主先的天主,亞巴郎的天主,依撒格的天主和雅各伯的天主曾顯示給你。」
Yehova anati, “Ukachite zimenezi ndipo akakukhulupirira kuti Yehova, Mulungu wa makolo awo, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo, wakuonekera iwe.”
6 上主又對他說:「將你的手插在懷裏! 」他就將手插在懷裏;及至抽出手來,見手上患了癩瘡,向雪那樣白。
Yehova anatinso, “Pisa dzanja lako mʼmalaya akowo.” Choncho Mose anapisa dzanja lake mʼmalaya ake ndipo pamene analitulutsa, linali la khate kuchita kuti mbuu ngati ufa.
7 天主又說:「將你的手再插進懷裏! ─他就把手再插進懷裏;及至從懷裏抽出時,見手已經恢復原狀,像別的肌肉一樣。─
Yehova anati, “Tsopano pisanso dzanja lako mʼmalaya.” Mose anapisanso dzanja lakelo mʼmalaya ake ndipo atalitulutsa, linali labwinobwino, ngati thupi lake lonse.
8 如果他們不肯信你,也不信服第一個奇蹟,必定信服第二個奇蹟。
Tsono Yehova anati “Akakapanda kukukhulupirira, osalabadira chozizwitsa choyambacho, akakhulupirira ndithu chifukwa cha chozizwitsa chachiwiricho.
9 如果連這兩個奇蹟也不信,也不聽你的話,你就從尼羅河裏取些水,倒在旱地上;你從河裏取的水必在旱地上變成血。」
Koma ngati sakakhulupirira zizindikiro ziwiri izi kapena kukumvera, ukatunge madzi a mu mtsinje wa Nailo ndi kuwathira pa mtunda powuma ndipo madziwo adzasanduka magazi.”
10 梅瑟對上主說:「吾主,請原諒! 我不是個有口才的人,以前不是,你向你的僕人說話以後,也不是;我原是笨口結舌的人。」
Mose anati kwa Yehova, “Chonde Ambuye, chikhalire ine ndakhala munthu wosatha kuyankhula bwino. Ngakhale tsopano pamene mukundiyankhula, lilime langa ndi lolemera. Ndine wachibwibwi.”
11 上主回答他說:「是誰給人一個嘴﹖是誰給人口啞耳聾,眼明眼瞎呢﹖不是我上主嗎﹖
Yehova anati kwa iye, “Kodi anapatsa munthu pakamwa ndani? Ndani amasandutsa munthu kuti akhale wosayankhula kapena wosamva? Ndani amapanga munthu kukhala wopenya kapena wosaona? Kodi si Ine Yehova?
12 現在你去,我要幫助你說話,指教你該說什麼。」
Tsopano pita, Ine ndidzakuthandiza kuyankhula ndipo ndidzakulangiza zoti ukanene.”
13 梅瑟回答說:「吾主,請原諒! 你要打發誰,就打發誰去吧! 」
Koma Mose anati, “Chonde Ambuye, pepani, tumani wina kuti akachite zimenezi.”
14 上主向梅瑟發怒說:「不是有你的哥哥肋末人亞郎嗎﹖我知道他是有口才的,他現在正前來迎接你;他見了你,心中必要快樂。
Kenaka Yehova anamupsera mtima Mose ndipo anati, “Kodi suli ndi mʼbale wako Aaroni wa fuko la Levi? Ine ndikudziwa kuti iye amayankhula bwino. Iye wanyamuka kale kudzakumana nawe ndipo adzasangalala akadzakuona.
15 你可向他說話,將你應該說的話放在他口中。我要幫助你,也幫助他說話,指教你們應做什麼。
Iwe udzayankhula naye ndi kumuwuza mawu oti akanene. Ine ndidzakuthandizani kuyankhula nonse awirinu ndi kukulangizani zoti mukachite.
16 他要代替你向百姓說話,作你的口舌;你對他是代替天主。
Iye akayankhula kwa anthu mʼmalo mwako. Iye adzakhala wokuyankhulira ndipo iweyo udzakhala ngati Mulungu kwa iye.
17 你手中要拿著這根棍杖,用來行奇蹟。」梅瑟回埃及
Koma utenge ndodo imene ili mʼdzanja lakoyo kuti ukachite nayo zizindikiro zozizwitsa.”
18 於是梅瑟起來回到他岳父耶特洛那裏,對他說:「請讓我回到埃及我兄弟那裏,看看他們還健在嗎﹖」耶特洛對梅瑟說:「你平安去罷! 」
Tsono Mose anabwerera kwa Yetero, mpongozi wake ndipo anati kwa Iye, “Chonde ndiloleni kuti ndibwerere ku Igupto kwa anthu anga kuti ndikaone ngati ali moyo.” Yeteri anati, “Pitani mu mtendere.”
19 上主在米德揚對梅瑟說:「起身回埃及去! 因為那些想殺害你的人都死了。」
Nthawiyi Yehova anali atamuwuza kale Mose ku Midiyani kuti, “Bwerera ku Igupto, pakuti anthu onse amene amafuna kukupha aja anamwalira.”
20 梅瑟遂帶著妻子孩子,叫他們騎在驢上,起身回埃及國去了;梅瑟手中拿著天主的棍杖。
Kotero Mose anatenga mkazi wake ndi ana ake aamuna, ndipo anawakweza pa bulu nayamba ulendo wobwerera ku Igupto. Ndipo anatenga ndodo ya Mulungu ija mʼdzanja lake.
21 上主對梅瑟說:「你回到埃及,要將我交於你行的一切奇蹟,行於法朗面前;但我要使他心硬,不肯放百姓走。
Yehova anati kwa Mose, “Ukaonetsetse kuti wachita pamaso pa Farao zodabwitsa zonse zimene ndayika mphamvu mwa iwe kuti ukachite. Koma Ine ndidzawumitsa mtima wake kotero kuti sadzalola anthuwo kuti apite.
22 你要對法朗說:上主這樣說:以色列是我的長子。
Ndipo iwe ukati kwa Farao, ‘Yehova akuti, Israeli ali ngati mwana wanga wachisamba.’
23 我命你,讓我的兒子去崇拜我。你若拒絕放他們走,我必要殺你的長子。」
Choncho ndikuti, ‘Mulole mwana wanga apite kuti akandipembedze. Koma ngati ukana, Ine ndidzapha mwana wako wachisamba.’”
24 梅瑟在路上住宿的時候,上主遇著他,要想殺他。
Pambuyo pake Mose ali mʼnjira, pamalo wogona, Yehova anakumana naye, ndipo anafuna kumupha.
25 漆頗辣急忙拿了一塊石刀,將他兒子的包皮割下,拿包皮接觸他的腳說:「你真是我的血郎。」
Koma Zipora anatenga mwala wakuthwa nachita mdulidwe mwana wake ndipo khungulo analikhudzitsa pa mapazi a Mose. Iye anati “Zoonadi, kwa ine ndiwe mkwati wamagazi.”
26 這樣上主就放了他。當時漆頗辣說:「血郎。」是因了割損的原故。
Choncho Yehova anamuleka Mose wosamupha. Pa nthawiyo, Zipora anati, “Mkwati wa magazi,” ponena za mdulidwe.
27 其時上主向亞郎說:「你往曠野去迎接梅瑟! 」他就去了。在天主的山旁預見了梅瑟,口親了他。
Yehova anati kwa Aaroni, “Pita ku chipululu ukakumane ndi Mose.” Iye anapitadi nakakumana ndi Mose pa phiri la Mulungu namupsompsona.
28 梅瑟把上主打發他所說的一切話和命他行的奇蹟,都告訴了亞郎。
Kenaka Mose anamufotokozera Aaroni chilichonse chimene Yehova anamutuma kuti akanene. Anamufotokozera za zizindikiro zozizwitsa zimene anamulamulira kuti akazichite.
29 梅瑟和亞郎遂去召集了以色列子民所有的長老
Mose ndi Aaroni anapita kukasonkhanitsa pamodzi akuluakulu onse a Aisraeli.
30 亞郎講述了上主向梅瑟所說的一切話,也當著百姓行了那些奇蹟;
Ndipo Aaroni anawafotokozera zonse zimene Yehova ananena kwa Mose. Anachita zizindikirozo pamaso pa anthu onse,
31 百姓就都信了,也都高興,因為上主眷顧了以色列子民,也垂念了他們的痛苦。他們遂都俯伏叩拜。
ndipo anakhulupirira. Iwo atamva kuti Yehova anadzawayendera ndi kuti waona mmene akuzunzikira, anaweramitsa mitu pansi napembedza.

< 出埃及記 4 >