< 申命記 28 >

1 你若實在聽從上主你的天主的話,謹守遵行我今天吩咐你的這一切誡命,上主你的天主必使你遠超過地上所有的民族。
Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
2 如果你聽從上主你的天主的話,下面這些祝福必臨於你,來到你身上。
Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
3 你在城內必蒙受祝福,在鄉下也必蒙受祝福。
Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
4 你身所生的,田地所產的,牲畜所出的,牛所生殖的,羊所產下的,都要蒙受祝福。
Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
5 你的筐籃,你的揉麵盆,都要蒙受祝福。
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
6 你進來,蒙受祝福;你出去,也蒙受祝福。
Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
7 起來攻擊你的仇敵,上主必使他們在你面前崩潰;他們由一路來攻擊你,卻分七路由你面前逃去。
Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
8 上主決定對你的倉廩和在你著手進行的事上祝福你。
Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
9 只要你謹守上主你的天主的誡命,遵行他的道路,上主必要照他誓許於你的,立你為他自己的聖民;
Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
10 普世萬民一見你屬於上主的名下,必都怕你。
Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
11 在上主你的天主向你祖先起誓要賜給你的土地上,上主必使你滿享幸福:兒女眾多,牲畜繁殖,地產豐富。
Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
12 上主必為你大開天上的寶庫,給你的田地降下時雨,祝福你手所做的一切;你要借給許多民族,而你卻無須向人借貸。
Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
13 上主必立你為首,而不做尾巴,你常是高高在上,而總不屈居在下,只要你聽從我今天吩咐你的上主你天主的誡命,並謹守遵行,
Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
14 不左右偏離我今天吩咐你們的一切話,去跟隨事奉其他的神。
Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
15 但是,如果你不聽從上主你天主的話,不謹守遵行我今天吩咐你的上主的一切誡命和法令,下面這些咒罵必要臨於你,來到你身上。
Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
16 你在城內必遭受咒罵,在鄉下也必遭受咒罵。
Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
17 你的筐籃,你的揉麵盆,都要遭受咒罵。
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
18 你身所生的,田地所產的,牛所生殖的,羊所產下的,都要遭受咒罵。
Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
19 你進來,必遭受咒罵;
Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
20 你出去也必遭受咒罵。上主在你著手進行的一切事上,必使你遭受災難、困擾和恐嚇,直到你完全毀滅,迅速滅亡,因為你作惡,離棄了我。
Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
21 上主必使你瘟疫纏身,直到將你由你要去佔領的地上完全消滅。
Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
22 上主必用癆病、熱病、瘧疾、炎熱、乾旱、熱風和霉爛打擊你;這些災殃必追擊你,直到你滅亡。
Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
23 你頭上的天將變為銅,你下面的地將變為鐵。
Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
24 上主必使雨變成灰沙降在你的田地裏,由天上降在你身上,直到你完全毀滅。
Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
25 上主必使你在仇敵面前崩潰;你由一路出擊他們,卻分七路由他們前逃去;你要成為普世萬國驚駭的對象。
Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
26 你的屍首必成為天空飛鳥,和地上走獸的食物;無人來將牠們嚇走。
Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
27 上主必用埃及的膿瘡、痔漏、癬疥紅疹打擊你,使你無法醫治。
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
28 上主必用癲狂、眼瞎和心亂打擊你;
Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
29 在正午時,你要摸索有如在黑暗中摸索的瞎子;你的所作所為決不會順利;你必日日受人壓迫剝削,而無人援助。
Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
30 你與一女子訂婚,別人卻來與她同寢;你建築一座房屋,卻不得住在裏面;你栽植葡萄園,卻得不到享用。
Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
31 你的牛在你眼前被殺,你卻不能吃牠的肉;你的驢由你眼前被人搶去,再不歸還給你;你的羊群被交給你的敵人,卻無人來援助你。
Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
32 你的兒女被交給外方民族,你只有雙眼張望,日日為他們焦慮,但你卻無能為力。
Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
33 你田地的出產和你勞力之所得,卻為你不認識的一個民族吃盡;你只有時時被人壓迫蹂躪;
Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
34 你必要因你親眼所見的事而變為瘋狂。
Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
35 上主必用惡瘡打擊你的膝和腿,由腫至頂,使你無法醫治。
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
36 上主你將你和你所立的統治你的君王,送到你和你祖先不認識的一個民族那裏去,在那裏你要事奉別的神,即木石所製的神。
Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
37 在上主要送你去的各民族中,你必成為驚駭、嘲笑和諷刺的對象。
Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
38 你在田間撒的種子雖然很多,但收穫的卻很少,因為蝗蟲要來吃盡。
Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
39 你雖然栽種修剪葡萄園,卻沒有酒喝,沒有收成,因為都要為蟲子吃盡。
Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
40 你雖然在全境栽有橄欖樹,卻沒有油抹身,因為橄欖要遂結遂落。
Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
41 你雖然生子養女,但他們卻不屬於你,因為他們要被擄去。
Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
42 害蟲要吃盡你所有的樹木和土地的出產。
Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
43 住在你中間的外方人不斷發達興旺,遠在你以上,你反而日趨卑下。
Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
44 他要借給你,你卻不能借給他;他要為首,你卻要做尾巴。
Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
45 這一切咒罵必臨於你,追擊你,來到你身上,直到你全被消滅,因為你沒有聽從上主你天主的話,沒有遵守他吩咐你的誡命和法令。
Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
46 這些咒罵對你和你的子孫,永遠是一個徽號和徵兆。
Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
47 因為在財物富裕時,你沒有誠心悅意地去事奉上主你的天主,
Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
48 你必在飢渴,赤身露體,一無所有中,服侍上主派來攻擊你的仇敵;他必將鐵軛放在你的頸上,直到將你消滅。
chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
49 上主必由遠方,由地極引來一個民族,像鷹一樣撲擊你;這民族的語言,你不明瞭;
Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
50 這民族又鐵面無情,不敬老,不恤幼;
mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
51 他必吞食你家畜的幼雛,和田地的產物,直到你被消滅;必不給你留下什麼穀、米、酒、油、牛犢或羔羊,直到將你完全毀滅。
Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
52 他必將你圍困在所有的城鎮內,直到你全國內所依恃的高大堅固的城牆都被攻陷;當你被圍困在上主你天主賜給你的全境各城鎮內時,
Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
53 在你被仇敵圍困的窮困中,你要吃你自身所生,即上主你天主賜給你子女的肉。
Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
54 你中間最溫柔嬌嫩的男人,這時對自己的兄弟、懷中的妻子、尚存的子女,也必冷眼相看,
Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
55 不願將他所吃的子女的肉,分給他們任何人,因為在你的仇敵使你在各城鎮受圍困陷於絕境時,已一無所剩。
ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
56 你中間最溫柔嬌嫩的女人,先前嬌嫩溫柔得連腳都不踏在地上,這時對自己懷中的丈夫、自己的子女、也要冷眼相看,
Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
57 暗中將她兩腿間脫出的胞衣,和她所生的子女吃掉,因為在你的仇敵使你在各城鎮中受圍困,陷於窮困時,已一無所有。
zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
58 如果你不謹守遵行這書上所記的法律的一切條文,敬畏這光榮可畏的名號:上主你的天主,
Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
59 上主必使你和你的後裔遭受更奇特的災害,大而且久的災害,毒而且頑的疾病;
Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
60 必使你所怕的各種埃及病災發生在你身上,纏繞著你。
Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
61 此外,在在這法律書上所沒有記載的一切疾病和災害,上主也要引來降在你身上,直到將你完全消滅。
Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
62 你們以前雖然多如天上的繁星,你們所留下的,卻寥寥無幾,因為你沒有聽從上主你天主的話。
Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
63 有如上主先前怎樣喜歡你們獲得幸福,使你們人數眾多,將來也要怎樣喜歡你們衰落,使你們滅亡,使你們由你要去佔領的地上盡被剷除。
Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
64 上主要將你分散在大地兩極間所有人民中,你要在那裏事奉你和你祖先所不認識的外神,即木石之神;
Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
65 而且在這些民族中,你總得不到安寧,也找不到一塊歇腳的地方;上主在那裏必使你心情煩亂,眼目憔悴,精神頹喪。
Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
66 你未來的生活必提心吊膽,日夜驚惶;生命毫無保障。
Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
67 因你心情恐慌,因你眼見的景象,早晨你要說:「巴不得現在是晚上! 」到了晚上你又要說:「巴不得現在是早晨! 」
Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
68 上主要用船將你送回埃及,走我曾告訴你,你不會再見的那條路;在那裏你們雖自願將自己賣給你的仇敵為奴為婢,卻無人肯買。
Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.

< 申命記 28 >