< 但以理書 2 >

1 拿步高在位第十二年,拿步高一連做了幾個夢,遂心神不寧,不能入睡。
Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
2 於是君王下令召巫師、術士、方士和占星者前來給君王詳夢;他們前來了,站在君王前,
Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
3 君王對他們說:「我做了一個夢,心神不寧,急於要知道這夢的究竟。」
mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
4 占星者用【阿剌美語】回答君王說:「大王萬歲! 請大王給你的僕人們說出夢來,我們好給大王解釋那夢的意義。」
Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
5 君王答覆占星者說:「我是言出必行的,如果你們不告訴我那夢和夢的意義,你們必被萬刮凌遲,你們的家必成為廢墟。
Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
6 但若你們告知我那夢和夢的意義,你們必獲得我的禮物、賞報和崇高的尊榮;為此你們告訴我那夢和夢的意義罷! 」
Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
7 他們又回答說:「請大王給你的僕人們說出夢來,好讓我們給大王解釋。」
Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
8 君王回答說:「我明知你們是在想爭取時間,因為你們明知我是言出必行的;
Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
9 如果你們不告訴我那夢,為你們只有一個判決。那麼,你們是想在我面前說謊欺騙,專待時機的轉變。現在你們要告訴我那夢,好使我知道你們能為我解釋那夢的意義。」
Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
10 占星者在君王面前回答說:「世上沒有一個人能說出大王所問的事,從來也沒有一位君王,不論他如何偉大,有勢力,向任何巫師、術士和占星者詢問過這樣的事。
Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
11 大王詢問的,確是件難事,沒有誰能告訴大王,除非那不與血肉之軀同居的神祇。」
Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
12 君王因此生氣,大發雷霆,下令消滅巴比倫所有的智者。
Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
13 要殺智者的諭令發出之後,人們就搜索達尼爾和他的同伴,要將他們殺死。
Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
14 君王的衛隊長阿黎約客出發,要殺巴比倫的智者之時,達尼爾機警明智地應付了他。
Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
15 達尼爾問君王的全權大臣阿黎約客說:「君王發出的諭令,為什麼這樣迫切」﹖阿黎約客遂將事情告訴了達尼爾。
Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
16 達尼爾進去要求君王給他延長限期,好為君王詳解夢兆。
Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
17 然後回到家裏,把事情告訴了自己的同伴阿納尼雅、米沙耳和阿匝黎雅,
Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
18 要他們為這秘密事,懇求上天的大主施恩,挽救達尼爾和他的同伴與巴比倫其餘的智者,免被殺害。
Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
19 於是在夜間的神視中,這個秘密就啟示給達尼爾了;達尼爾遂讚美上天的大主,
Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
20 說:「願天主的名,從永遠直到永遠受讚美,因為智慧和能力都屬於他。
ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
21 是他變更四時季節,是他廢黜君王,也興立君主,賜智者以智慧,賜識者以聰敏;
Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
22 是他啟示隱秘深奧之事,洞悉暗中的事,因為光明居於他內。
Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
23 我祖先的天主,我稱謝讚頌你,因為你賜給了我智慧和能力。我們祈求你的事,現在你已曉諭了我們,使我們知道了君王的秘密。」
Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
24 達尼爾遂去見君王委派殺戮巴比倫智者的阿黎約客,對他這樣說:「請暫且先不要殺害巴比倫的智者,帶我去見君王,我要給君王解夢。」
Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
25 於是阿黎約客立刻引達尼爾去見君王,對君王說:「我從猶大被擄的子民中找得一人,他會給大王解夢。」
Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
26 君王對名叫貝耳特沙匝的達尼爾說道:「你能告訴我,我所見的夢和夢的意義嗎﹖」
Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
27 達尼爾回答君王說:「大王所問的奧秘,不是智者、術士、巫師和占卜者所能告訴大王的;
Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
28 但是,在天上有一位啟示奧秘的大主! 他已將那日後要發生的事曉諭給大王。大王! 你在床上腦中所得的夢,所見的神視是這樣:
koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
29 大王你睡在床上忽然想到日後所要發生的事,啟示奧秘的那位,把要發生的事已曉諭給你。
“Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
30 這奧秘已啟示給我,並非因為我比任何活人更有智慧,而只是為把夢兆告訴大王,叫你知道你心心中的思念。」「
Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
31 大王! 你夢見一尊巨大的立像。這尊立像異常高大,非常光輝燦爛,立在君王面前,相貌可怕。
“Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
32 這尊立像,頭是純金的,胸和臂是銀的,腹和股是銅的。
Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
33 脛是鐵的,腳一部份是鐵,一部份是泥的。
Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
34 大王,你在觀望,忽有一塊石頭,未經手鑿即滾下,擊中了立像,把鐵泥的腳,打得粉碎;
Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
35 同時鐵、泥、銅、銀和金立即完全粉碎,有如夏天禾場上的糠秕,被風吹去,無蹤無影;那塊擊碎立像的石頭卻變成了一座大山,佔據了全地。」「
Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
36 夢是這樣的,現在我們要給大王解釋夢兆。
“Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
37 大王! 你是王中之王,上天大主賜給了你領土、勢力、權威和尊榮,
Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
38 凡有人居住的地方,田野的走獸,天空的飛鳥,都交在你手中,由你統治這一切,你便是那屬金的頭。
Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
39 在你以後,將興起另一個比你稍弱的國家,以後興起第三個國家,屬銅,她要統轄大地;
“Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
40 相繼而來的是第四個,堅強如鐵的國家,就如鐵能粉碎擊破一切,這個國家也要如鐵粉碎擊破一切,
Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
41 至於你見腳和趾,一部分是泥,一部分是鐵,表示這個國家必要分裂,然而國內仍有鐵的堅強,正如你見鐵與泥相混一樣。
Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
42 腳趾一部分是鐵,一部份是泥,表示這個國家一部分強,一部分弱。
Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
43 你見鐵與泥混合,是說他們要與其他人種相混合,但是彼此不能相合,就如鐵不能與泥相混合一樣。
Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
44 在這些君王時代,上天的大主必要興起一個永不滅亡的國家,她的王權也決不歸於其他民族,她要粉碎和毀滅這一切邦國,惟獨她永存弗替,
“Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
45 就如你所見那塊未經手鑿,即從山上滾下的石頭,把鐵、銅、泥、銀和金打得粉碎一樣。偉大的天主已曉諭了大王,今後將要發生的事。這夢是真實的,夢的解釋也是正確的。」
Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
46 拿步高於是俯首至地,叩拜達尼爾,下令給他奉上禮物和香品,
Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
47 然後開口對達尼爾說:「的確,你們的天主是萬神的天主,萬王的主宰,奧秘的啟示者,因為你能啟示這個奧秘。」
Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
48 王遂擢升達尼爾,賞賜他很多珍貴的禮品,派他治理巴比倫全省,做巴比倫所有智者的首領。
Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
49 達尼爾要求君王委任沙得辣客、默沙客和阿貝得乃哥掌管巴比倫省的政務;達尼爾自己卻留在朝廷內。
Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.

< 但以理書 2 >