< 歷代志下 28 >

1 [阿哈次的惡行]阿哈次登極時年二十歲,在耶路撒冷作王凡十六年。他沒有像他的祖先達味一樣,行上主視為正義的事,
Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
2 卻走了以色列列王的路,為巴耳諸神鑄了像,
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
3 在本希農山谷焚香,仿效上主從以色列子民面前所趕走的異民所行的醜惡之事,令自己的兒女經火獻神,
Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
4 又在高處、丘陵和綠樹下焚香獻祭。[猶大受懲罰]
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
5 因此,上主他的天主將他交於阿蘭王手中,阿蘭打敗了他,擄去了他一大批人民,帶到大馬士革。上主又將他交於以色列王手中,大加殺戮。
Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
6 勒瑪里雅的兒子培卡黑在猶大一日殺了十二萬人,都是戰士,因為他們離棄了上主,他們祖先的天主。
Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
7 厄弗辣因一個名叫齊革黎的勇士,殺了王子瑪阿色雅、王宮總管阿次黎岡和君王的輔相厄耳卡納。
Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
8 以色列子民由他們的弟兄中擄去了婦女和他們的子女,共二十萬人,並掠去了許多財物,都帶到撒瑪黎雅。[先知力勸釋放俘虜]
Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
9 在那裏有一位上主的先知,名叫敖德得,出來迎接回撒瑪黎雅的軍隊,向他們說:「看,上主,你們祖先的天主,由於向猶大發怒,纔將他們交在你們手中,你們卻怒氣沖天,大加殺戮;
Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
10 現在你們又想強迫猶大和耶路撒冷的子民作你們的奴婢;難道你們自己就沒有干犯上主,你們天主的罪惡嗎﹖
Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
11 現在,你們聽我的話,將由你們弟兄中擄來的俘虜放回去,因為上主的震怒已臨到你們身上。」
Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
12 那時厄弗辣因子民的首領中有幾個人,即約哈南的兒子阿匝黎雅,默史肋摩特的兒子貝勒革雅,沙隆的兒子希則克雅和哈德來的兒子阿瑪撒,就起來反對歸來的軍隊,
Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
13 對他們說:「不可將俘虜帶到這裏來,因為你們想使我們得罪上主,來增加我們的罪惡和過犯! 我們的過犯已經夠重了,上主的震怒已臨於以色列。」
Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
14 軍隊立即將擄來的人和搶來的財物,留在首領和全會眾面前。
Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
15 以上題名的那幾個人便起來,領去被擄的人,其中有赤身的,便從所掠取的財物中,取出衣服來給他們穿,給他們鞋穿,又給他們吃喝,且給他們擦油;又將所有軟弱的人,放在驢上,送到稷櫚城耶里哥,他們的弟兄那裏;以後,便回了撒瑪黎雅。[阿哈次四面受敵]
Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
16 那時,阿哈次派人去亞述王那裏求救,
Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
17 因為厄東人又來攻打猶大,擄去了許多人民;
Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
18 培肋舍特人也侵入平原的城市和猶大的南方,佔領了貝特舍默士、阿雅隆、革德洛特、索苛及其四郊村鎮、提默納及其四郊村鎮、基默左及其四郊村鎮,並住在那裏。
Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
19 由於猶大王阿哈次在猶大肆無忌憚,背叛了上主,因此,上主壓伏了猶大。
Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
20 亞述王提革拉特丕肋色爾到了他那裏,不但沒有協助,反而壓迫了他。
Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
21 阿哈次強奪了上主殿內、王宮以及群臣家中的財寶,奉送給亞述王,但無濟於事。[阿哈次惡上加惡]
Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
22 阿哈次王這個人越在困難之時,越發背叛上主,
Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
23 他竟祭祀打敗了他的大馬士革的神說:「阿蘭王的神,既協助了阿蘭人,我也向他們獻祭,好使他們也協助我。」但是那些神卻使他與以色列民眾陷於滅亡。
Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
24 阿哈次又將上主殿內的器皿收集起來,將上主殿內的器皿予以粉碎,將上主殿宇的門封鎖,在耶路撒冷每個角落設立祭壇,
Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
25 在猶大各城建立丘壇,向外邦的神焚香,這樣激起了上主,他祖先的天主的震怒。[阿哈次逝世]
Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
26 阿哈次其餘的事蹟和他行的一切,前前後後,都記載在猶大和以色列列王實錄上。
Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
27 阿哈次與祖先同眠,葬在耶路撒冷城內,但沒有將他葬在以色列王陵內。他的兒子希則克雅繼位為王。
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 歷代志下 28 >