< 列王紀上 9 >

1 [上主再次顯現]撒羅滿建造完了上主的殿、王宮和他所喜歡建造的一切建築物以後,
Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene ankafuna,
2 上主第二次顯現給撒羅滿,像在基貝紅顯現給他一樣。
Yehova anamuonekera kachiwiri, monga momwe anamuonekera ku Gibiyoni.
3 上主對他說:「我已應允了你在我面前所行的祈禱和哀求,我也祝聖了你所建築的這殿,將我的名永遠安放在那裏,我的眼和我的心,也將時常留在那裏。
Yehova ananena kwa iye kuti: “Ndamva pemphero ndi pembedzero lako pa zimene wapempha pamaso panga. Ndayipatula Nyumba iyi, imene wamanga, poyikamo Dzina langa mpaka muyaya. Maso anga ndi mtima wanga zidzakhala pamenepo nthawi zonse.
4 至於你,如果你在我面前行走,像你父親達味那樣行走,心地純樸,公正無私,遵守我所吩咐你的一切,恪守我的法律和點章,
“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika, mwangwiro ndi moona mtima monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
5 我必永遠鞏固你在以色列中的王位,照我應許你父親達味所說:你的子孫中,決不缺人坐上以色列的寶座。
Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu pa Israeli mpaka muyaya, monga ndinalonjezera abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu pa mpando waufumu wa Israeli.’
6 但是,如果你們或你們的子孫遠離我,不遵守我給你們頒賜的誡命和律例,而去服侍敬拜別的神,
“Koma ngati iwe kapena ana ako mudzapatuka ndi kuleka kusunga malamulo ndi mawu anga amene ndakupatsani ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
7 我必要將以色列從我賜給他們的地面上除掉,而我為我的名所祝聖的這殿,我也必要棄之不顧,使以色列成為萬民中的話柄和笑談,
pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko limene ndinawapatsa ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndayipatula chifukwa cha Dzina langa. Pamenepo Aisraeli adzasanduka mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
8 這殿要成為廢墟,凡從這裏經過的人,都要驚愕嗟歎說:上主為什麼這樣對待了這地和這殿﹖
Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzatsonya ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
9 人必回答說:是因為他們離棄了領他們祖先出離埃及的上主,他們的天主,而歸依、崇拜、服侍了別的神,為此,上主使這一切災禍臨到他們的身上。」撒羅滿與希蘭的交易
Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova Mulungu wawo amene anatulutsa makolo awo mʼdziko la Igupto, ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”
10 撒羅滿費時二十年,纔完成了那兩大殿宇:即上主的殿宇和君王的宮殿。
Patatha zaka makumi awiri, ndiye nthawi imene Solomoni anamanga nyumba ziwirizi: Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu,
11 其間提洛王希蘭曾依照撒羅滿的要求,供給了他香柏木、柏木和黃金。此時撒羅滿王便將加里肋亞境內二十座城,送給了希蘭。
Mfumu Solomoni anapereka mizinda makumi awiri ya ku Galileya kwa Hiramu mfumu ya ku Turo chifukwa Hiramu nʼkuti atapereka mitengo yonse ya mkungudza ndi ya payini ndiponso golide yense zimene Solomoni ankazifuna.
12 希蘭從提洛前來,觀看撒羅滿送給他的城,一見就不滿意,
Koma Hiramu atabwera kuchokera ku Turo kudzaona mizinda imene Solomoni anamupatsa, sanasangalatsidwe nayo mizindayo.
13 說「吾兄,你送給我的這些城,是什麼城﹖」因此直到今日,這些城仍稱為加步耳地。
Iye anafunsa kuti, “Mʼbale wanga, kodi iyi nʼkukhala mizinda yondipatsa?” Ndipo iye anayitcha mizindayo Dziko la Kabuli, dzina lomwe amatchedwa mpaka lero lino.
14 希蘭原送給了撒羅滿王一百二十「塔冷通」黃金。建城造船
Koma Hiramu anali atatumiza kwa mfumu golide oposa makilogalamu 4,000.
15 此段記載撒羅滿徵夫服役,建造上主的殿、王宮、米羅、耶路撒冷的城牆、哈祚爾、默基多、革則爾、【
Izi ndi zimene anachita Mfumu Solomoni: Analamula anthu kuti agwire ntchito yathangata pomanga Nyumba ya Yehova, nyumba yake, malo achitetezo a Milo, mpanda wa Yerusalemu, Hazori, Megido ndi Gezeri.
16 以前,埃及王法郎曾上來,攻取了革則爾,放火燒城,屠殺了城裏的客納罕人,將這城賜給了自己的女兒,撒羅滿的妻子,作為妝奩。
(Farao mfumu ya ku Igupto inali itathira nkhondo ndi kulanda Gezeri. Iye anatentha mzindawo. Anapha Akanaani amene ankakhala mʼmenemo ndipo kenaka anawupereka ngati mphatso yaukwati kwa mwana wake wamkazi amene anakwatiwa ndi Solomoni.
17 為此撒羅滿重修了革則爾。】下貝特曷龍、
Ndipo Solomoni anamanganso Gezeri.) Iye anamanga Beti-Horoni Wakumunsi,
18 巴拉特和境內靠近曠野的塔瑪爾、
Baalati ndi Tadimori ku chipululu, mʼdziko lake lomwelo,
19 撒羅滿所有的貯貨城、屯車城和養馬城,以及撒羅滿在耶路撒冷,在黎巴嫩,在他管轄的各地內,喜歡建造的一切建築物。
pamodzinso ndi mizinda yake yosungira chuma ndiponso mizinda yosungiramo magaleta ndi akavalo ake. Anamanganso chilichonse chimene anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.
20 至於不屬於以色列子民的阿摩黎人、赫特人、培黎齊人、希威人和耶步斯人的遺族,
Panali anthu amene anatsala pakati pa mitundu ya Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi (anthu awa sanali Aisraeli).
21 就是以色列人子民未能消滅而留在地方上的外族子孫,撒羅滿都徵來充作苦役,直到今天。
Zimenezi ndiye zinali zidzukulu zawo zotsalira mʼdzikoli, anthu amene Aisraeli sanathe kuwawononga kotheratu. Solomoni anawatenga ndi kukhala akapolo ake ogwira ntchito yathangata, monga zilili mpaka lero lino.
22 至於以色列子民,他不令他們作苦役,只叫他們服兵役,作朝臣、將帥、軍官、戰車長和騎兵長。
Koma Solomoni sanagwiritse ntchito ya ukapolo Mwisraeli aliyense; iwo anali anthu ake ankhondo, nduna zake, atsogoleri a ankhondo, akapitawo ake, olamulira magaleta ndi oyendetsa magaleta ake.
23 管理撒羅滿工程的主任官員,計有五百五十人,他們負責監督作工的人。
Amenewa ndiwo anali akuluakulu oyangʼanira ntchito za Solomoni. Anthu okwana 550 ndiwo ankayangʼanira anthu amene ankagwira ntchitowo.
24 法郎的女兒從達味城,搬進撒羅滿為她建造的宮室之後,撒羅滿纔開始建造米羅。
Mwana wamkazi wa Farao atachoka mu Mzinda wa Davide, kupita ku nyumba ya mfumu imene Solomoni anamumangira, Solomoni anamanga malo achitetezo a Milo.
25 撒羅滿每年三次在他建的祭壇上,向上主奉獻全燔祭與和平祭,在上主面前的香壇上焚香;又常修理聖殿。
Katatu pa chaka Solomoni ankapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe limene anamangira Yehova ndiponso ankafukiza lubani pamaso pa Yehova. Potero ankakwaniritsa zoyenera kuchitika mu Nyumba ya Yehova.
26 此後,撒羅滿王又在厄東城,紅海之濱,靠近厄拉特的厄茲雍革貝爾建造船隻。
Mfumu Solomoni anapanganso sitima zapamadzi ku Ezioni Geberi, malo amene ali pafupi ndi Eloti ku Edomu, mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
27 希蘭派遣自己的臣僕,善於航海的船員,與撒羅滿的僕人同船航行,
Ndipo Hiramu anatumiza anthu ake oyendetsa sitima zapamadzi amene ankadziwa za pa nyanja kuti aziyendetsa pamodzi ndi anthu a Solomoni.
28 去了敖非爾,從那裏裝載了四百二十「塔冷通」黃金,運到撒羅滿王那裏。
Iwo anapita ku Ofiri ndipo anakatenga golide okwana makilogalamu 14,000, amene anamupereka kwa Mfumu Solomoni.

< 列王紀上 9 >