< 歷代志上 4 >

1 [猶大的後代]猶大的子孫: 培勒茲、赫茲龍、加爾米、胡爾和芍巴耳。
Ana a Yuda anali awa: Perezi, Hezironi, Karimi, Huri ndi Sobali.
2 芍巴耳的兒子勒阿雅生雅哈特,雅哈特生阿胡買和拉哈得:以上屬祚辣家族。
Reaya mwana wa Sobala anabereka Yahati, ndipo Yahati anabereka Ahumai ndi Lahadi. Awa anali mabanja a Azorati.
3 以下是厄坦的父親胡爾的子孫:依次勒耳、依市瑪和依德巴士;他們的姊妹名叫哈茲肋耳頗尼。
Ana a Etamu anali awa: Yezireeli, Isima ndi Idibasi. Dzina la mlongo wawo linali Hazeleliponi.
4 還有革多爾的父親培奴耳,胡沙的父親厄則爾:以上是白冷的父親,厄弗辣大的長子,胡爾的子孫。
Penueli anabereka Gedori, ndipo Ezeri anabereka Husa. Awa anali ana a Huri, mwana wachisamba wa Efurata ndi abambo a Betelehemu.
5 特科亞的父親阿市胡爾有兩個妻子:赫拉和納阿辣。
Asihuri abambo a Tekowa anali ndi akazi awiri, Hela ndi Naara.
6 納阿辣給他生了阿胡倉、赫斐爾、特曼人和阿哈市塔黎人:以上是納阿辣的兒子。
Naara anamuberekera Ahuzamu, Heferi, Temani ndi Haahasitari. Awa ndiwo anali ana a Naara.
7 赫拉的兒子:責勒特、祚哈爾、厄特難和科茲;
Ana a Hela: Zereti, Zohari, Etinani,
8 科茲生阿奴布;祚貝巴、雅貝茲和哈戎的兒子阿哈勒爾的家族。
ndi Kozi, amene anali abambo ake a Anubi ndi Hazo-Beba ndi mabanja a Ahariheli mwana wa Harumi.
9 雅貝茲在自己的兄弟中最受尊重;他母親給他起名叫雅貝茲說:「我在痛苦中生了他。」
Yabesi anali munthu wolemekezeka kwambiri kuposa abale ake. Amayi ake anamutcha Yabesi kutanthauza kuti, “Chifukwa ndinamubala ndi ululu wambiri.”
10 雅貝茲呼求了以色列的天主說:「若你真祝福我,求你擴展我的疆域,求你常伸手扶助我,脫免災難,不受痛苦。」天主就賞賜了他所求的。
Yabesi analira kwa Mulungu wa Israeli kuti, “Mundidalitse ndipo mukulitse dziko langa! Dzanja lanu likhale pa ine ndipo mundisunge kuti choyipa chisandigwere ndi kundisautsa.” Ndipo Mulungu anamupatsa chopempha chakecho.
11 叔哈的兄弟革路布生厄舍東的父親默希爾。
Kelubi, mʼbale wa Suha, anabereka Mehiri, amene anabereka Esitoni.
12 厄舍東生貝特辣法、帕色亞和依爾納哈士的父親特興納,他是刻尼次人厄色隆的兄弟:以上是勒加布人。
Esitoni anabereka Beti-Rafa, Paseya ndi Tehina amene anabereka Iri Nahasi. Amenewa ndiwo anthu a ku Reka.
13 刻納次的兒子:敖特尼耳和色辣雅;敖特尼耳的兒子:哈塔特和毛諾泰。
Ana a Kenazi anali awa: Otanieli ndi Seraya. Ana a Otanieli anali awa: Hatati ndi Meonotai.
14 毛諾泰生敖弗辣;色辣雅生革哈辣史的父親約阿布;他們原是工匠。
Meonotai anabereka Ofura. Seraya anabereka Yowabu, amene anabereka Ge-Harasimu. Anawatcha dzina ili chifukwa anthu ake anali amisiri.
15 耶孚乃的兒子加肋布的兒子:依爾、厄拉和納罕;厄拉的兒子刻納次。
Ana a Kalebe mwana wa Yefune anali awa: Iru, Ela ndi Naama. Mwana wa Ela anali Kenazi.
16 雅肋肋耳的兒子:齊弗、齊法、提黎雅和阿撒勒耳。
Ana a Yehaleleli anali awa: Zifi, Zifa, Tiriya ndi Asareli.
17 厄次辣的兒子:耶特爾、默勒得、厄斐爾和雅隆。彼提雅生米黎盎、沙買和厄市特摩的父親依市巴。
Ana a Ezara anali awa: Yeteri, Meredi, Eferi ndi Yaloni. Mmodzi mwa akazi a Meredi anabereka Miriamu, Samai ndi Isiba abambo ake a Esitemowa.
18 他的猶大妻子生革多爾的父親耶勒得、索哥的父親赫貝爾和匝諾亞的父親耶谷提耳:以上是默勒得所娶法郎的女兒彼提雅所生的兒子。
(Mkazi wake wa Chiyuda anabereka Yaredi abambo ake a Gedori, Heberi abambo ake a Soko ndi Yekutieli abambo a Zanowa). Awa anali ana a mwana wamkazi wa Farao, Bitia, amene Meredi anakwatira.
19 納罕的姊妹,曷狄雅的妻子生的兒子:加爾米人刻依拉的父親和瑪阿加人厄市特摩。
Ana a mkazi wa Hodiya, mlongo wa Nahamu anali awa: abambo ake a Keila wa ku Garimi ndi Esitemowa wa ku Maaka.
20 史孟的兒子:阿默農、陵納、本哈南和提隆。依史的兒子:左赫特和本左赫特。
Ana a Simeoni anali awa: Amnoni, Rina, Beni-Hanani ndi Tiloni. Ana a Isi anali awa: Zoheti ndi Beni-Zoheti.
21 猶大的兒子舍拉的兒子:肋加的父親厄爾、瑪勒沙的父親拉阿達和在耳特阿市貝亞細麻織工的家族;
Ana a Sela mwana wa Yuda anali awa: Eri amene anabereka Leka, Laada amene anabereka Maresa ndi mabanja a anthu owomba nsalu zofewa ndi zosalala a ku Beti-Asibeya,
22 還有約肯、苛則巴人、約阿士和撒辣弗;他們回白冷之前,去摩阿布娶了妻子。【這都是古代的事。】
Yokimu, anthu a ku Kozeba, ndiponso Yowasi ndi Sarafi, amene ankalamulira Mowabu ndi Yasibu-Lehemu. (Nkhani zimenezi ndi zakalekale).
23 他們都是陶工,定居乃塔因和革德辣,操此手藝,靠君王居住。[西默盎支派]
Iwo anali owumba mbiya amene ankakhala ku Netaimu ndi Gederi. Ankakhala kumeneko ndi kumatumikira mfumu.
24 西默盎的兒子:乃慕耳、雅明、雅黎布、則辣黑和沙烏耳。
Ana a Simeoni anali awa: Nemueli, Yamini, Yaribu, Zera ndi Sauli;
25 沙烏耳的兒子沙隆,沙隆的兒子米貝散,米貝散的兒子米市瑪。
Salumu anali mwana wa Sauli, Mibisamu anali mwana wa Salumu ndipo Misima anali mwana wa Mibisamu.
26 米市瑪的子孫:米市瑪的兒子哈慕耳,哈慕耳的兒子匝雇爾,匝雇爾的兒子史米。
Zidzukulu za Misima zinali izi: Hamueli, Zakuri ndi Simei.
27 史米有十六個兒子,六個女兒;但他的兄弟門子女不多,為此他們的家族不如猶大的子孫旺盛。
Simei anali ndi ana aamuna 16 ndi ana aakazi 6, koma abale ake sanabereke ana ambiri; kotero banja lawo silinakule ngati anthu ena a ku Yuda.
28 他們住在貝爾舍巴、摩拉達、哈匝爾叔阿耳、
Iwo amakhala ku Beeriseba, Molada, Hazari-Suwali,
29 彼耳哈、厄曾、托拉得、
Biliha, Ezemu, Toladi,
30 貝突耳、曷爾瑪、漆刻拉格、
Betueli, Horima, Zikilagi,
31 貝特瑪爾加波特、哈匝爾穌心、貝特彼黎和沙阿辣因,直到達味王時代,都是他們住的城市,
Beti-Marikaboti, Hazari-Susimu, Beti-Biri ndi Saaraimu. Iyi inali mizinda yawo mpaka pa nthawi ya ulamuliro wa Davide.
32 和所屬的村莊。此外,還有厄坦阿殷、黎孟、托庚、阿商五城市,
Midzi yowazungulira inali Etamu, Aini, Rimoni, Tokeni ndi Asani, midzi isanu
33 和這些城市四周直到巴耳所屬的各村莊:以上是他們居住的地方和族譜。
ndi midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baala. Awa anali malo awo okhalapo. Ndipo anasunga mbiri ya makolo awo.
34 默芍巴布、雅默肋客、阿瑪責雅的兒子約沙、
Mesobabu, Yamuleki, Yosa mwana wa Amaziya,
35 約厄耳、耶胡,─耶胡是約史貝雅的兒子,約史貝雅是色辣雅的兒子,色辣雅是阿息耳的兒子;
Yoweli, Yehu mwana wa Yosibiya, mwana wa Seraya, mwana wa Asieli,
36 還有厄里約乃、雅科巴、耶芍哈雅、阿撒雅、阿狄耳、耶息米耳、貝納雅、
komanso Eliyoenai, Yaakoba, Yesohaya, Asaya, Adieli, Yesimieli, Benaya,
37 齊匝,─齊匝是史非的兒子,史非是阿隆的兒子,阿隆是耶達雅的兒子,耶達雅是史默黎的兒子,史默黎是舍瑪雅的兒子:
ndiponso Ziza mwana wa Sifi, mwana wa Aloni, mwana wa Yedaya, mwana wa Simiri, mwana wa Semaya.
38 以上諸人,都是宗族的首領,他們的家族也很興旺。
Anthu amene atchulidwawa anali atsogoleri a mabanja awo. Mabanja awo anakula kwambiri
39 他們遷往革辣爾關口,直到山谷東面,為羊群找尋牧場。
ndipo anakafika ku malire a Gedori ku chigwa cha kummawa kufuna msipu wodyetsa ziweto zawo.
40 他們找了一片很肥沃良好的牧場,廣闊、清靜、安寧的地方。古時含的後代住在那裏。
Anapeza msipu wobiriwira ndi wabwino ndipo dziko linali lalikulu, la mtendere ndi bata. Kumeneko kunkakhala fuko la Hamu poyamba.
41 猶大王希則克雅時代,上述的這些人出征,破壞了當地民族的帳幕,擊殺了當地所有的瑪紅人,將他們消滅直到今日;他們遂居住在他們的地方,因為那裏有放羊的牧場。
Anthu amene mayina awowa alembedwa, anabwera pa nthawi ya Hezekiya mfumu ya Yuda. Iwo anathira nkhondo fuko la Hamu mʼmalo awo amene amakhala komanso Ameuni amene anali kumeneko ndipo anawononga onsewo kotero kuti mbiri yawo simvekanso mpaka lero lino. Kotero iwo anakhala mʼmalo awo chifukwa kunali msipu wa ziweto zawo.
42 西默盎的子孫中,另有五百人出征色依爾山區;依史的兒子培拉提雅、乃阿黎雅、勒法雅和烏齊耳為統率,
Ndipo anthu 500 a fuko la Simeoni, motsogozedwa ndi Pelatiya, Neariya, Refaya ndi Uzieli, ana a Isi, analanda dziko lamapiri la Seiri.
43 擊殺了其餘未逃脫的阿瑪肋克人;以後他們住在那裏,直到今日。
Iwo anapha Aamaleki otsala amene anali atapulumuka ndipo akukhala kumeneko mpaka lero lino.

< 歷代志上 4 >