< Rom 3 >
1 Hat pawiteh, Judah tami ni bangmaw meknae kaawm. Vuensomanae ni bangmaw hawinae kaawm.
Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe?
2 Ahawinae aphunphun ao. Hmaloe vah, vuensoma lah kaawm e Judahnaw teh Cathut lawk hah a coe awh.
Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.
3 Hat pawiteh, ahnimouh thungvah ka yuem hoeh e awm pawiteh bangtelane ahnimae yuemhoehnae ni Cathut yuemkamcunae hah a kâ raphoe sak han na maw.
Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu?
4 Kâ raphoe mahoeh. Cathut ni a lawk lahoi lannae lah a coe teh, lawkceng toteh tâ nahanelah, Cakathoung dawk thut e patetlah tami pueng teh laithoe kadeikung lah ao awh ei, Cathut teh kalan e lah awm naseh, telah ati.
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti, “Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi kupambana pamene muweruza.”
5 Hatnavah, maimae lanhoehnae ni Cathut lannae kamnuek sak pawiteh, bangtelamaw dei awh han. Tami koe lahoi dei pawiteh, lungkhueknae ka phat sak e Cathut teh kalan hoeh e Bawipa lah maw ao.
Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira).
6 Hottelah khoeroe awm hoeh. Hottelah awm pawiteh Cathut ni bangtelah hoi maw talaivan lawk a ceng han vaw.
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi?
7 Hatei, kaie laithoenae lahoi Cathut lawkkatang ni a bawilennae hoe pung sak pawiteh, kai heh tamikayon buet touh lah bangkongmaw lawkceng e lah ka o rah vaw.
Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?”
8 Hnokahawi a tâco nahanlah hno kahawihoehe sak awh han, telah tet thai mahoeh maw. Tami tangawn ni hottelah maimouh ni dei awh ati awh teh, maimouh dudam lahoi a dei awh. Ahnimae yonphukhangnae teh a kamcu doeh.
Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.
9 Hottelah pawiteh, bangtelah han maw. Maimouh teh hoe hawi awh maw. Hoe hawi awh hoeh. Bangkongtetpawiteh, Judahnaw hoi Griknaw hai yon rahim vah ao tie yo kamnue sak toe.
Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa.
10 Cakathoung dawk thut e patetlah tamikalan awmhoeh, buet touh boehai awmhoeh.
Monga kwalembedwa kuti, “Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
11 Ka thai panuek e awmhoeh. Cathut ka tawng e awmhoeh.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira, palibe amene amafunafuna Mulungu.
12 Tami pueng lam a phen awh teh, abuemlahoi cungkeihoeh lah ao awh toe. Hnokahawi ka sak e apihai awmhoeh, buet touh boehai awmhoeh.
Onse apatukira kumbali, onse pamodzi asanduka opandapake. Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino, palibe ngakhale mmodzi.”
13 Ahnimae a lawkron teh kamawng e tangkom lah ao. Ahnimouh ni a lai hoi laithoe a dei awh. A pahni dawk hrunthoe sue ao.
“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.” “Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
14 Ahnimae apâhni teh lawkthoeumkha hoi akawi.
“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 Ahnimae khok teh tami thei hane koe lah a hue a rang awh.
“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
16 Ahnimae lamthung dawk kamkonae hoi roedengnae ao teh,
Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
17 Ahnimouh ni roumnae lam panuek awh hoeh.
ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
18 Ahnimae mit dawk Cathut takinae tawn awh hoeh.
“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”
19 Kâlawk ni a dei e pueng teh kâlawk thung kaawmnaw hanelah doeh tie panue awh. Hottelah ao dawkvah, talaivan pueng teh lawk kam touh boehai dei thai laipalah, Cathut hmalah ka yon e lah ao awh.
Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu.
20 Hatdawkvah, kâlawk tarawinae lahoi apihai Cathut hmalah tamikalan lah awm thai hoeh. Bangkongtetpawiteh, kâlawk teh yon ka panueksakkung lah doeh ao.
Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.
21 Atuteh kâlawk hoi profet lawknaw ni a kampangkhai e Cathut lannae teh, kâlawk laipalah a kamnue toe.
Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni.
22 Cathut lannae teh Jisuh Khrih kayuemnaw pueng e lathueng vah a pha. Hatdawkvah, kapeknae khoeroe awmhoeh.
Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina,
23 Bangkongtetpawiteh, tami pueng teh a yon awh dawkvah Cathut bawilennae hoi kâhla awh toe.
pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu
24 Ahnimouh teh Cathut lungmanae dawk Khrih Jisuh thung ratangnae lahoi aphu poe laipalah na lan toe telah khoe e lah o toe.
ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola.
25 Cathut ni ama lannae a kamnue sak nahanelah Khrih hah a rawi teh, yuemnae hanlah Khrih thipaling teh thuengnae lah ao sak. Phunlouk lahoi dei pawiteh, Cathut ni a lungsawnae lahoi kaloum tangcoung e yonnae naw hah pâkuem laipalah ao.
Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale.
26 Hatdawkvah, atuteh amae lannae hah kamnue sak hane hoi Cathut ama roeroe alan teh, Jisuh ka yuem e taminaw hai alansak.
Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.
27 Hat pawiteh, kâoupkhai kawi na mouh ao va. Hot teh pahnawt lah ao toe. Bang phung hoi mouh pahnawt lah ao va. Tawksaknae hoi maw. Na hoeh. Yuemnae lahoi pahnawt lah ao.
Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro.
28 Bangkongtetpawiteh, tami teh kâlawk tarawinae lahoi laipalah yuemnae lahoi tamikalan lah na khoe toe tie lah pouk awh.
Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo.
29 Nahoeh pawiteh, Cathut teh Judahnaw hane Cathut dueng na maw. Jentelnaw e Cathut lahai awmhoeh namaw. A o. Jentelnaw e Cathut lahai ao.
Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso,
30 Yuemnae lahoi vuensom ka a e tami teh na lan toe telah khoe e lah ao teh, vuensom ka a hoeh naw hai yuemnae lahoi na lan toe telah ka khoe e Cathut teh buet touh duengdoeh.
popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho.
31 Hat pawiteh, maimouh ni yuemnae lahoi kâlawk teh pahnawt awh namaw. Khoeroe pahnawt awh hoeh. Kâlawk hah hoe caksak awh.
Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.