< Papholawk 2 >

1 Efisa kho e kawhmoun e kalvantami koe hettelah thut haw. Aranglae kut dawk Âsi sari touh a sin teh, sui hmaiimkhok sari touh e lungui kâhlai e ni hettelah a dei.
“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Efeso kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri zija mʼdzanja lake lamanja amene akuyenda pakati pa zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide.
2 Na thaw tawk e naw, na kâyawm e naw, hoi na khang e naw hah ka panue. Nang teh tami kahawihoehnaw hah na dâw thai hoeh e hoi amamouh hoi amamouh guncei telah a kâdei eiteh guncei lah kaawm hoeh e taminaw hah na tanouk awh teh ahnimouh teh tami kadumyennaw lah na hmu awh e hai ka panue.
Ine ndimadziwa zochita zako, ntchito yako yowawa ndi kupirira kwako. Ine ndimadziwa kuti sungalekerere anthu oyipa amene amadzitcha atumwi pamene sichoncho, unawayesa, ndipo unawapeza kuti ndi abodza.
3 Nang teh panguep nalaihoi ka Min kecu dawk, patang na khang teh thayounnae na tawn awh hoeh.
Iwe wapirira ndipo wakumana ndi zovuta chifukwa cha dzina langa, ndipo sunatope.
4 Hatei, kai ni nang yon pen hane ao. Bangkongtetpawiteh, nang ni ahmaloe e lungpatawnae hah na pahnawt toe.
Komabe ndili ndi chotsutsana nawe: Wataya chikondi chako chapoyamba.
5 Hatdawkvah, nang teh nâ e hmuen koehoi maw na bo tie bout pouk nateh, pankângai haw. Hmaloe e thawnaw hah tawk haw. Hottelah pankângainae na tawn hoehpawiteh, nang koe kai ka tho vaiteh, nange hmaiimkhok hah hmuen koehoi ka puen han.
Kumbukirani kuti munagwa kuchokera patali. Lapa ndikuchita zinthu zimene unkachita poyamba. Ngati sulapa ndidzabwera ndikukuchotsera choyikapo nyale chako pamalo pake.
6 Hatei, buet touh teh nang dawk ao, ka hmuhma e Nikolas hnukkâbangnaw e tawksaknae hah nang nihai na hmuhma van tie dei hane kawi lah ao.
Komabe chokomera chako ndi chakuti umadana ndi zochita za Anikolai, zimene Inenso ndimadana nazo.
7 Muitha ni kawhmounnaw koe a dei e lawknaw hah hnâ ka tawn pueng ni thai naseh. Ka tâ e tami teh Cathut e paradis takha thung kaawm e hringnae thingpaw hah ca thainae kâ ka poe han.
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wakudya zipatso za mtengo wopatsa moyo umene uli ku paradizo wa Mulungu.
8 Smirna kho e kawhmoun e kalvantami koe hettelah thut haw. Hmaloe poung hoi hnukteng poung lah kaawm e, a due eiteh bout kahring e ni hettelah a dei.
“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Simurna kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi Woyamba ndi Wotsiriza, amene anafa nʼkukhalanso ndi moyo.
9 Nange rucatnae hoi reithainae teh ka panue. Hatei, nang teh na bawi. Namamouh hoi namamouh hah Judah tami na kâti awh eiteh, Judah tami nahoeh, Setan e tami lah kaawm e naw ni na dudam awh e hai ka panue.
Ine ndimadziwa masautso ako ndi umphawi wako, chonsecho ndiwe wolemera! Ndikudziwa zimene amakusinjirira anthu amene amati ndi Ayuda pamene sizili choncho, koma ndi a mpingo wa Satana.
10 Nang ni na khang hane rucatnae hah taket hanh. Khenhaw! Nang ni tanouknae hah na khang awh hanelah kahraimathout ni nangmouh thung dawk hoi tangawn teh thongim dawkvah a pabo awh han toe. Nangmanaw teh hnin hra touh thung reithai rucat na khang awh han. Due totouh yuemkamcu lah awm awh. Telah na sak pawiteh, hringnae bawilukhung teh na poe han.
Musachite mantha ndi zimene muti musauke nazo posachedwapa. Ndithu, Satana adzayika ena a inu mʼndende pofuna kukuyesani, ndipo mudzazunzika kwa masiku khumi. Khalani okhulupirika ngakhale zitafika pa imfa, ndipo Ine ndidzakupatsani chipewa cha ulemerero wamoyo.
11 Muitha ni kawhmounnaw koe a dei e lawk hah thainae hnâ ka tawn ni thai seh, ka tâ e tami teh apâhni duenae ni rektap mahoeh.
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana sadzapwetekedwa ndi pangʼono pomwe ndi imfa yachiwiri.
12 Pergamos kho e kawhmoun e kalvantami koe hettelah thun haw. A hâ avoivang kahran e tahloi ka tawn e ni hettelah a dei.
“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Pergamo kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi lupanga lakuthwa konsekonse.
13 Nang teh na e hmuen dawk maw na o tie ka panue. Hote hmuen dawk Setan e bawitungkhung ao. Kai dawk yuemkamcu lah kaawm e, kai na kapanuekkhaikung, Antipas teh Setan onae hmuen lah kaawm e nangmouh koevah a thei awh nah patenghai yah kaie min hah na kuet awh teh, yuemnae na tâkhawng awh hoeh.
Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa kumene mumakhala, kumene kuli mpando waufumu wa Satana. Komabe inu ndinu okhulupirika kwa Ine. Simunataye chikhulupiriro chanu pa Ine, ngakhale mʼmasiku a Antipa, mboni yanga yokhulupirika, amene anaphedwa mu mzinda wanu, kumene amakhala Satana.
14 Hatei, nang koe yon pen hane youn touh ao. Bangkongtetpawiteh, nang koevah Balaam e cangkhainae ka tarawi e ao. Isarelnaw ni meikaphawk bawknae koe a thueng e hnonaw hah a ca awh nahan hoi kamsoumhoehe napui tongpa yonnae ahnimouh hmalah payon sak e hnonaw hah pâtoum pouh hanelah Balaam ni Balak siangpahrang koe a cangkhai.
Komabe, ndili ndi zinthu zingapo zotsutsana nanu. Kumeneko muli ndi anthu ena amene amatsata ziphunzitso za Balaamu, uja amene anaphunzitsa Baraki kukopa Aisraeli kuti azidya nsembe zoperekedwa ku mafano ndi kumachita chigololo.
15 Hot patet lavah nangmouh dawkvah Nikolas hnukkâbangnaw e cangkhainae ka tarawi e tami moi ao awh.
Chimodzimodzinso inuyo muli ndi ena amene amatsatira ziphunzitso za Anikolai.
16 Hatdawkvah pankângai awh haw. Hoehpawiteh kai teh nangmouh koe karanglah ka tho vaiteh, ka kâko e tahloi hoi ahnimanaw teh ka tuk han.
Tsono tembenukani mtima. Mukapanda kutero, ndidzabwera kwanuko posachedwa ndipo ndidzachita nanu nkhondo ndi lupanga lotuluka mʼkamwa mwanga lija.
17 Muitha ni kawhmounnaw koe a dei pouh e lawk hnâ ka tawn e pueng ni thai naseh. Ka tâ e tami teh hro e Mana ka poe han. Talung pangaw hai ka poe han, hote talung van e min ka kâthut e kacoekung hloilah apinihai panue hoeh e min katha teh a thut.
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Kwa amene adzapambane ndidzamupatsa chakudya chobisika cha mana. Ndidzamupatsanso mwala woyera wolembedwapo dzina latsopano, lodziwa iye yekha amene walandirayo.’”
18 Thiatira kho e kawhmoun e kalvantami koe hettelah thun haw. Hmaipalai patetlah e mit hoi laklakkaang e rahum hoi kâvan e khok ka tawn e Cathut e Capa ni hettelah a dei.
“Lembera mngelo wampingo wa ku Tiyatira kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa Mwana wa Mulungu, amene maso ake ali ngati moto woyaka ndi mapazi ake ngati chitsulo chonyezimira.
19 Nange na tawk e naw puenghoi nange lungpatawnae, yuemnae, thawtawknae, hoi lungsawnae hai kai ni ka panue. Nange hnuk lae thaw na tawk e naw teh hmaloe e thaw na tawk e hlak hoe ahawi e hah ka panue.
Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zanu, chikondi chanu ndi chikhulupiriro chanu, kutumikira kwanu ndi kupirira kwanu. Ndikudziwa tsopano kuti ntchito zanu ndi zabwino kuposa zoyamba zija.
20 Hatei, nang teh kai ni yon pen hane ao. Bangdawk tetpawiteh nang teh amahoima profet napui ka kâtet e Jezebel hah sak ngai e pueng sak thainae kâ na poe dawkvah ahni teh kaie ka hnukkâbangnaw koe kamsoumhoehe napui tongpa yonnae hoi meikaphawk bawknae sathei moinaw ca hanelah na cangkhai teh ahnimanaw na dumyen awh.
Komabe ndili ndi chinthu chokudzudzula nacho. Umamulekerera mkazi uja Yezebeli amene amadzitcha yekha kuti ndi mneneri. Iye amaphunzitsa atumiki anga kuti azichita zadama ndi kumadya zansembe zoperekedwa ku mafano.
21 Kai ni ahni koe pankângai hane tueng ka poe eiteh ahni ni kamsoumhoehe napui tongpa yonnae dawk pankângainae lungthin tawn hoeh.
Ndamupatsa nthawi kuti aleke zachigololo zake koma sakufuna.
22 Khenhaw! kai ni ahni teh a ikhun dawk pak ka tha han. Ahni hoi uicuknae dawk pankângai awh hoehpawiteh, takikathopounge runae ka pha sak han.
Tsono ndidzamugwetsa mʼmasautso ndipo amene amachita naye zadama zakezo ndidzawasautsa kwambiri akapanda kulapa ndi kuleka njira za mkaziyo.
23 Ahnie a canaw koehai duenae hoi kai ni lawk ka ceng han. Hahoi kai teh pouknae lungthin hoi ngainae kakhenkung lah ka o tie kawhmounnaw pueng ni a panue awh han. Nangmanaw pueng hai namamouh ni na sak e patetlah tawkphu na poe awh han.
Ana ake ndidzawakantha ndi kuwapheratu. Kotero mipingo yonse idzadziwa kuti Ine ndine uja amene ndimafufuza mʼmitima mwa anthu ndi mʼmaganizo mwawo. Aliyense wa inu ndidzachita naye monga mwa ntchito zake.
24 Hatei, hote napui e cangkhainae na dawn awh hoeh. Setan e hro e hno telah ka panuek hoeh e Thiatira kho kaawm e pueng koe, kai ni ka dei e teh nangmouh lathueng vah alouke hno karinaw hah na thueng pouh mahoeh.
Tsopano ndikunena kwa enanu a ku Tiyatira, kwa inu amene simunatsate chiphunzitso cha mkaziyo ndipo simunaphunzire zimene iwo amati ndi ‘zinsinsi zonama’ za Satana. Kwa inu mawu anga ndi akuti sindikuwunjikirani malamulo ena.
25 Nangmouh dawkvah kaawm e hno hah kai ka tho totouh kacakcalah kuen awh.
Inu mungogwiritsa zimene munaphunzira basi, mpaka Ine ndidzabwere.
26 Ka tâ e tami hoi kaie ka thaw hah a pout totouh ka tawk e tami teh miphunnaw pueng uknae kâ ka poe han.
Amene adzapambana ndi kuchita chifuniro changa mpaka kumapeto, ndidzamupatsa ulamuliro pa mitundu yonse ya anthu.
27 Ahni teh talai hlaamnaw reppasei lah hem e patetlah sum sonron hoi ahnimouh teh a uk han. Hethateh, kama roeroe ni a Pa koehoi ka coe e uknae hoi a kâvan.
Adzayilamulira ndi ndodo yachitsulo ndipo nadzayiphwanyaphwanya ngati mbiya. Ulamuliro umenewu ndi omwe ndinalandira kwa Atate anga.
28 Ahni teh amom tempalo hai ka poe han.
Ine ndidzamupatsanso nthanda, nyenyezi yowala mʼmamawa ija.
29 Muitha ni kawhmounnaw koe a dei e lawk hah hnâ ka tawn pueng ni thai naseh.
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.

< Papholawk 2 >