< Sam 78 >
1 Kathutkung: Asaph Oe, ka taminaw ka kâlawk hah tarawi awh nateh, ka dei e lawk hah na hnâpakeng awh.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 Bangnuenae lahoi ka pahni ka ang vaiteh, ayan e lawkkaru hah ka pâpho han.
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 Hothateh, ka thai teh, ka panue tangcoung e mintoenaw ni a dei awh e doeh.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 A canaw koehoi kâhrawk mahoeh. Ka tho hane senaw koevah, BAWIPA pholennae, a thaonae, hoi hno kângairu a sak e hah ka dei han.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 Bangtelah tetpawiteh, mintoenaw hah kâ a poe teh, a ca catounnaw koe a panue sak awh nahanlah, Jakop koe lawkpanuesaknae hah acak sak teh, Isarel koe kâlawk hah a poe.
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 Kaawm han rae se hoi ka tâcawt han rae camonaw ni, a catounnaw koe a dei awh vaiteh, a panue awh nahanlah,
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 Cathut dawk a ngaihawi awh nahan hoi Cathut hnosak hah pahnim laipalah kâpoelawknaw a pahnim awh hoeh nahanlah,
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 Mintoenaw patetlah lungpatanae, taranthawnae, kalan e hno dawk a lung kaawm hoeh e, Cathut hanelah yuemkamcu hoeh e muitha lah ao awh hoeh nahane doeh.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Ephraim catoun teh tarantuknae a khohna teh licung a patuep ei, tarantuk hnin navah a yawng.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 Cathut lawkkam tarawi awh hoeh. Kâlawk tarawi e ngai awh hoeh.
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 A sak e hoi hno kângairu a sak e hah, a pahnim awh.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 A na mintoenaw e mithmu vah, kângairu hno hah Izip ram Zoan tanghling dawk a sak.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 Talîpui hah a kapek teh ahnimanaw hah a cei sak. Tui hah hnopai patetlah a pâhlawp.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 Kanîthun hai tâmai hoi a hrawi teh, tangmin karoitawi hmaiang hoi a hrawi.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 Kahrawngum vah, lungsong a bawng teh, talîpui tui patetlah moikapap e tui a pânei.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 Lungsong thung hoi tui a tâco sak teh, palangpui patetlah a lawng sak.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Hatei, ama taranlahoi hoehoe a yon awh teh, kahrawngum vah Lathueng Poung taranlahoi taran a thaw awh.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 Ca han a ngai poung awh e hah a hei awh teh, a lungthin hoi Cathut hah a tanouk awh.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 Bokheiyah, Cathut taranlahoi a dei awh e teh, kahrawngum vah Cathut ni rawca na poe thai awh han na maw, telah ati awh.
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Khenhaw! tui a tâco teh, tuiko muen ka kawi lah a lawng nahan lah lungsongpui hah a hem. Rawca hai a poe thai namaw. A taminaw hah moi a poe thai han na ou, telah ati awh.
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Hatdawkvah, BAWIPA ni hote lawk hah a thai teh a lungkhuek. Hat toteh, Jakop taranlahoi hmaito a tâco teh, Isarel taranlahoi a lungkhuek.
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 Bangkongtetpawiteh, Cathut hah yuem awh hoeh. A rungngangnae hai kâuep awh hoeh.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Hottelah nahlangva, lathueng lae tâmai hah kâ a poe teh, kalvan longkha hah a paawng pouh.
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 Ca hane mana hah ahnimouh lathueng a rak sak teh, kalvanlae rawca hah a poe.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Taminaw ni thaonae rawca hah a ca awh teh, kaboumlah ca hane a patawn.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Kanîtholae kahlî hah kalvan a tho sak teh, a hnotithainae lahoi a cum lae kahlî hah a tho sak.
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 Vaiphu patetlah moi hah a rak sak teh, rathei ka tawn e tavanaw hah tuirai e sadi yit touh apap awh.
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 A roenae tengpam petkâkalup lah a bo pouh.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 Hateh, a ca awh teh king a boum awh. Bangkongtetpawiteh, a ngai awh e patetlah a poe.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 Hatei, a ngai awh e rawca a hmawt awh hoehnahlan, a ca awh lahun navah,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 Cathut lungkhueknae teh ahnimouh koe a pha. A tami tha kaawmnaw hah a thei teh, Isarel thoundounnaw hah koung a rawp sak.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 Hottelah nahlangva, hoehoe a yon awh teh, hno kalen a sak awh e hai bout yuem awh hoeh.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Hatdawkvah, hringyung hnin hah ayawmyin lah a coung sak awh teh, lungpuennae hoi a kum teh a baw sak awh.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Ahnimanaw hah a thei awh teh, a ma tawng hanelah a ban awh teh, atangcalah Cathut heh a tawng awh.
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 Cathut teh amamae lungsongpui doeh tie a panue awh teh, Lathueng Poung Cathut teh na karatangkung doeh tie a panue awh.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 Hateiteh, ama teh a pahni hoi a pholen teh, lai hoi laithoe a dei awh.
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 Bangkongtetpawiteh, ahnimae lungthin teh a hmalah lan hoeh, a lawkkam dawk yuemkamcu awh hoeh.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Hatei, ama teh lungmanae hoi akawi teh, a payonnae heh a ngaithoum teh, koung raphoe hoeh. Bokheiyah, avai moikapap lungkhueknae a roum sak teh, a lungphuennae kaman sak ngai hoeh.
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 Bangkongtetpawiteh, takthai lah ao awh teh, bout ban hoeh hanelah, kâha a poe e tie hah pahnim awh hoeh.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 Thingyeiyawn vah vai nâyittouh maw a lungkhuek sak awh teh, ramke vah avai nâyittouh maw a lungmathoe sak awh toe.
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Bokheiyah, atuhoitu Cathut a tanouk awh teh, Isarelnaw e Tami Kathoung hah a taran awh.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 A thaonae pâkuem ngai awh hoeh, a tarannaw koehoi a rungngang ei nakunghai, pâkuem ngai awh hoeh.
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 Izip ram hoi Zoan yawn dawk kângairu hno a sak e hoi.
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 Ahnimae palang hah thipaling lah a coung sak teh, ahnimae tuikhunaw hai nei thai hoeh hanlah thipaling lah koung a coung sak.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Ahnimouh ka kei e bitseinaw hoi, ahnimouh karaphoekung ekkanaw hah a tha pouh.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 Ahnimae a pawhiknaw hah, ahri ni ca hanelah a poe teh, a tawksak awh e a pawhik hah samtongnaw a poe pouh.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 Ahnimae misurnaw teh roun ni koung a raphoe pouh teh, thailahei kungnaw hai tadamtui ni koung a thei pouh.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 Ahnimae saringnaw hai roun ni dêi hanelah a poe pouh teh, saringnaw hah kei ni a ka pouh.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Takitho e a lungkhueknae hah ahnimouh lathueng a rabawk teh, lungkhueknae, lungpoutnae, hoi runae hah ahnimouh koe thoenae kaphawtkung kalvan tami totouh a tha pouh.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 A lungkhueknae hanlah lamthung a sak, a hringnae hah duenae hlak pasai laipalah, lacik mathout hah letlang a poe.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 Izip vah camin pueng hoi Ham e rim a thaonae hmaloe poung e hoi koung a raphoe.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 Hatei, a taminaw teh tu patetlah a hrawi teh, saringnaw patetlah kahrawngum vah a hrawi.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 Karoumcalah a hrawi teh, taki hane banghai awm hoeh. A tarannaw teh talîpui ni koung a ramuk.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 Hahoi, ramri kathoung, aranglae kut hoi a tawn e, mon totouh a hrawi.
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 Ahnimae hmalah, alouke miphunnaw hah a pâlei pouh. A pang awh hane râw hah a bangnue pouh teh, alouklouk lah hmuen a poe.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Hat nahlangva, Lathueng Poung Cathut hah a tanouk awh teh, a lungkhuek sak awh teh, a panuesaknae lawk hah tarawi awh hoeh.
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 A na mintoenaw patetlah a kamlang awh teh, yuemkamcu hoeh lah a kâroe awh. Dumyennae licung patetlah a kâkamei awh.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 Bangkongtetpawiteh, ahnimae hmuerasangnaw ni a lungkhuek sak teh, a sak awh e meikaphawknaw ni dipma sinnae a tâco sak.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Hetheh Cathut ni a thai toteh, puenghoi a lungkhuek teh, Isarel hah puenghoi a panuet.
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 Hatdawkvah, taminaw koe a ta e Shiloh rim koe totouh a ceitakhai.
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 A thaonae teh san lah a coung sak teh, a lentoenae teh a tarannaw kut dawk a poe.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 A taminaw tahloi a kâhmo sak teh, râw lah a coe e naw koe a lungkhuek.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 A thoundounnaw teh hmai ni a kak awh teh, a tanglanaw ni vâ kâhmo awh hoeh.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 A vaihmanaw teh tahloi hoi a thei awh eiteh, lahmainaw ni khui awh hoeh.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 BAWIPA teh ka ip e patetlah a kâhlaw teh, misurtui kecu dawk ka hram e athakaawme tami patetlah a hram.
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 A taran hah a pâlei teh, a yungyoe min mathoenae hah a poe.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Hothloilah Joseph rim hah a pahnawt teh, Ephraim miphun hah rawi ngai hoeh.
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Ama koehoi Judah miphun, Zion mon ka pahren e heh a rawi.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 A hmuen kathoung hah karasang e patetlah a sak teh, talai patetlah a yungyoe acak sak.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 A san Devit hai a rawi teh tutakha thung hoi a la.
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 Tumanu, a canaw ouk a hrawi e patetlah, a tami Jakop hoi a coe e râw Isarelnaw khenyawnkung hanelah a la.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 Hothloilah, a lungthin ahawi e patetlah, a khetyawt teh, a thoumnae kut hoi a hrawi awh.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.