< Sam 139 >
1 Kathutkung: Devit Oe BAWIPA, nang ni na pâphue teh na panue toe.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
2 Kai ka tahungnae, ka thawnae pueng hah na panue. Kaie ka pouknae pueng hai ahlanae koehoi na panue.
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
3 Ka ceinae lamthung hai thoseh, ka inae hai thoseh, na pâphue teh, ka coungnae puenghai na panue.
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
4 Kai ni lawk kam touh boehai ka dei hoeh nakunghai Oe BAWIPA, nang ni koung na panue.
Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
5 Nang ni kai pet na kalup teh, kaie van vah na kut hah na toung toe.
Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
6 Hot patet e panuenae teh kângairu, arasang, kai ni ka phat thai hoeh.
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
7 Nange Muitha hoi hlout nahanelah nâmouh ka cei thai han va. Na hmalah hoi ka hlout nahanelah nâmouh ka cei thai han va.
Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
8 Kalvan ka luen pawiteh hawvah nang teh na o. Phuen koe yannae ka phai nakunghai hawvah nang teh na o. (Sheol )
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol )
9 Amom ratheinaw ka lat niteh, tuipui avanglae rai koe kaawm nakunghai,
Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
10 hote hmuen koehai Bawipa e kut ni na thak teh, aranglae kut ni na kuet han.
kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
11 Hmonae ni ka ramuk nakunghai, karum hai kaie tengpam vah angnae lah ao han.
Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
12 Bawipa hmalah hmonae ni banghai ramuk thai mahoeh. Karum teh khodai patetlah a ang. Hmonae hoi angnae teh reikâvan.
komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
13 Bawipa ni kaie kuen hah a sak teh, anu von thungvah kai hah na ramuk toe.
Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
14 Kai ni na pholen han. Bangkongtetpawiteh, takikatho lah, kângailah a ru. Ka hringnae ni kacaicalah a panue.
Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
15 Kai hah arulahoi na sak teh, talai thung vah na pahlawm navah, ka tak teh na hmalah hro lah awm hoeh.
Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
16 Nange mit niteh, kamnuek hoeh rae ka tak hai na hmu toe. Kai hanelah na hmoun e hninthanaw hnin touh boehai ao hoehnahlan hoiyah nama e cauk dawk ngit na thut e lah ao toe.
Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
17 Oe Cathut, kai dawkvah nange pouknae teh aphu o poung. Banghloi apap tangngak.
Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
18 Hote pouknae teh parei han pawiteh, sadi hlak hai apap han doeh. Ka kâhlaw toteh nang hoi pou ka o.
Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
19 Oe Cathut, tamikaponaw hah na thet pawiteh ahawi han doeh. Tami thei hanlah thi ka phuen e naw, kai koehoi tâcawt awh.
Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
20 Ahnimouh teh, ponae lahoi Bawipa tarannae lawk a dei awh. Nange tarannaw ni na min hah ayawmyin lah a hno awh.
Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
21 Oe BAWIPA, nang ni na hmuhma e naw hai kai ni hai ka hmuhma nahoehmaw. Nang ka tarannaw hai kai ni ka panuet nahoehmaw.
Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
22 Kai ni ahnimouh hah puenghoi ka hmuhma. Ka taran lah doeh ka pouk.
Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
23 Oe Cathut, kai hah na pâphue teh, kaie ka lungthin hah hmawt haw. Kai hah na noumcai nateh ka pouknae pueng panuek haw.
Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
24 Kai ni lamthung kathout dawk ka dawn ou, ka dawn hoeh ou tie na khen nateh, a yungyoe e lamthung dawk na hrawi haw.
Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.