< Cingthuilawk 11 >
1 Kânging hoeh e yawcu teh BAWIPA hanelah panuet a tho teh, kânging e bangnuenae teh a ngai e lah ao.
Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
2 Kâoup navah yeiraiponae ao teh, kârahnoum navah lungangnae ao.
Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
3 Tamikalan teh yuemkamcunae ni a hrawi han, hatei, yuemkamcu hoeh e khopouknae niteh amamouh a raphoe han.
Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
4 Lungkhueknae tueng navah hnopai teh cungkeihoeh, hatei lannae ni teh duenae koehoi a rungngang han.
Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
5 Lannae ni teh toun kaawm hoeh e naw hah lam kalan a pâtue han, hatei, tamikathoutnaw teh thoenae dawk letlang a rawp awh han.
Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
6 Tamikalannaw teh lannae ni a rungngang awh han, hatei, yuemkamcu hoeh e naw teh amamae ngainae dawk a kâman awh han.
Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
7 Tamikathoutnaw a due awh toteh a ngaihawi awh e puenghai a kahma vaiteh, tamikalanhoehnaw e ngaihawinae puenghai a kahma han.
Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
8 Tamikalan teh runae thung hoi a hlout vaiteh, hote runae teh tamikathoutnaw ni a pang awh han.
Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
9 Cathut ka taket hoeh e niteh, a pahni hoi a imri ouk a raphoe, hatei, tamikalan teh thoumthainae lahoi rungngang lah ao han.
Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
10 Tamikalan ni hawinae a coe navah khobuem a konawm awh, hatei, tamikathout a due toteh a lunghawi awh.
Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
11 Tamikalan ni yawhawi a coe navah khopui hai tawmrasang lah a o, hatei, tamikathoutnaw e pahni ni teh ouk a raphoe.
Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
12 Lungangnae ka vout e tami ni teh a imri hah ouk a dudam, hatei, thaipanueknae ka tawn e teh duem ao.
Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
13 Yuengyoe ka pai ni teh lawk kapap e tami ni hrolawk hah ouk a pâpho, hatei, yuemkamcu e ni teh ouk a hro.
Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
14 Pouknae kahawi poenae a ohoehnae koe khocanaw ouk a kahma teh, pouknae kahawi poenae apapnae koe teh khocanaw roumnae a coe awh.
Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
15 Panue hoeh e tami panuesaknae teh a khang han, hatei, lawkpanuesaknae dawk kut tambeinae ka ngai hoeh e teh a hlout han.
Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
16 Pahrennae ka tawn e napui ni barinae a coe, hatei, a thakasai e tongpa ni teh tawntanae a coe.
Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
17 Pahrennae ka tawn e tami ni a hringnae han lah hnokahawi a sak, hatei, tamikathout teh a takthai hanelah runae kapoekung doeh.
Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
18 Tamikathout ni dumnae phu ouk a hmu awh, hatei, lannae cati katukkungnaw ni tawkphu katang teh a coe awh han.
Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
19 Lannae ni hringnae lamthung dawk tami a hrawi e patetlah, thoenae ka sak e ni ouk a duekhai.
Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
20 Lungthin ka longkawi e teh BAWIPA hanelah panuet a tho, hatei, tamikalan kakuepcingnaw e hringnae teh amamouh letlang lunghawinae doeh.
Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
21 Lungkânging lah ao awh nakunghai, tamikathout teh rek laipalah awm mahoeh. Hatei, tamikalannaw e canaw teh hloutsak lah ao han.
Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
22 A meihawi eiteh pouknae ka tawn hoeh e napui teh, vok hnawng dawk suikuthrawt bang pouh e patetlah doeh ao.
Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
23 Tamikalan ni ngainae teh hawinae dueng doeh, hatei, tamikathout ni a ring e teh lungkhueknae dueng doeh.
Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
24 Thouk ka poe e teh, thouk a tawnta, hatei moikapap a pâkhueng eiteh, ka mathoe e tami hai ao.
Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
25 Hring ka pasoung e teh tawnta sak lah ao han. Ayâ tui ka awi e teh ama hai tui awi lah ao han.
Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
26 Cakang ka haw e tami teh ayâ ni thoe a bo han. hatei, kayawtkung koe teh yawhawinae ao han.
Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
27 Hawinae ka tawng katang e ni barinae a coe han. hatei, thoenae ka tawng koe teh runae a pha han.
Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
28 Hnopai kâuep e teh a rawp han, hatei tamikalan teh phokung patetlah dikhring han.
Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
29 Ma e imthung runae ka poe e ni a coe e râw teh kahlî lah ao vaiteh, tamipathu teh a lungkaangnaw koe san lah ao han.
Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
30 Tamikalannaw e a paw teh hringnae thing paw lah ao teh, muitha ka man e teh tami a lungkaang e doeh.
Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
31 Tamikalan patenghai talai van reknae khang pawiteh, cathutlaipa e hoi tamikayon teh banghloimaw hoe a khang han vai.
Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!