< Milu Pareinae 29 >
1 Thapa yung sari, a hnin apasuek hnin vah, kathounge na kamkhueng awh vaiteh, thaw banghai na tawk awh mahoeh. Nangmouh hanlah mongka uengnae hnin lah ao han.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 BAWIPA hmalah hmuitui thuengnae hah na poe awh han. Maitotanca buet touh, tu buet touh, tuca buet touh, kum touh ka phat e kacueme sari touh.
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Tavai thuengnae dawk tavaikanui satui hoi kanawk e maitotan buet touh dawkvah, ephah pung hra pung thum.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 Tutan buet touh ephah pung hra pung hni, tuca kanaw e sari touh, buet touh dawk buet touh dawk lengkaleng ephah pung hra pung touh.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Yontha nahanelah hmaetan buet touh hoi,
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 thaparei hnin hmaisawi thuengnae hoi hot hoi tavai thuengnae ouk a sak awh e, BAWIPA hanlah hmuitui hmaisawi thuengnae tawk sin laipalah na poe awh han.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 Hahoi thapa yung sari, ahra hnin vah, kathounge kamkhueng pawi na tawn awh han. Rawca na hai vaiteh, bang thaw hai na tawk awh mahoeh.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 BAWIPA koevah, hmuitui thuengnae hah na poe awh han. Maitotan kanaw e buet touh, tutan buet touh, tutan kanaw e a tan kum touh ka phat e sari touh, kacueme roeroe han.
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Tavaithuengnae teh tavaikanui satui hoi kanawk e maitotan buet touh dawkvah, ephah pung hra pung thum touh, tu buet touh dawk pung hra pung hni touh hoi,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 tu ca kanaw e sari touh thung vah, buet touh dawk teh ephah pung hra pung touh rip han.
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Yon thuengnae hanlah hmaetan buet touh hoi yontha nahanelah yon thuengnae hoi hmaisawi thuengnae pou na poe awh e hah tavai thuengnae hoi nei thuengnae touksin laipalah, pou na poe awh han.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 Thapa asari, hnin hlaipanga hnin vah kathounge kamkhuengnae na tawn awh han. Bang thaw hai na tawk awh mahoeh.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 BAWIPA han hmuitui hmaisawi thuengnae na poe awh han. Maitotan kanaw e hlaikathum, tutan kahni, tuca kum touh e hlaipali, kacueme seng han.
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Tavai thuengnae dawk maitotan hlaikathum, maitotan buet touh dawk tavaikanui e satui hoi kanawk e ephah pung hra pung thum, tutan kahni touh, tutan buet touh dawk ephah pung hra pung hni touh han.
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 tuca kanaw e hlaipali, tuca kanaw e buet touh dawk ephah pung hra pung touh han.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Yon thuengnae dawkvah, hmaetan buet touh hoi hmaisawi thuengnae pou na poe awh e, hote tavai thuengnae hoi nei thuengnae touksin laipalah, na poe awh han.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 Hahoi apâhni hnin vah maitotan hlaikahni, tutan kahni, tuca kanaw e a tan kum touh ka phat e kacueme hlaipali touh na poe awh han.
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 Tavaithuengnae hoi nei thuengnae phung patetlah a younpap e patetlah maitotan thoseh, tutan thoseh, tuca thoseh,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 yontha thuengnae hmaetan buet touh hoi hmaisawi thuengnae pou na poe awh e hah, tavaithuengnae hoi nei thuengnae touksin laipalah na poe awh han.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 Hahoi apâthum hnin vah, maitotan hlaibun, tutan kahni, tutan kum touh e kacueme hlaipali,
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 tavai thuengnae hoi nei thuengnae hah aphung patetlah a younpap e lahoi maitotan han e thoseh, tutan hane thoseh, tuca kanaw hane thoseh,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 yontha thueng nahanelah hmaetan buet touh hoi hmaisawi thuengnae dawk pou na poe awh e tavai thuengnae hoi nei thuengnae touksin laipalah na poe awh han.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 Hahoi, apali hnin vah, maitotan kanaw e hra, tutan kahni, tuca kum touh ka phat e kacueme hlaipali,
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 tavai thuengnae hoi nei thuengnae phueng patetlah a younpap e lahoi maitotan thoseh, tutan, tuca kanaw e thoseh,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 yontha thueng nahanelah hmaetan buet touh hmaisawi thuengnae dawk pou poe lah kaawm e tavaithuengnae hoi nei thuengnae touksin laipalah na poe awh han.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 Hahoi, apanga hnin maitotan kanaw e tako, tutan kahni, tutanca kanaw e kum touh ka phat e kacueme hlaipali,
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 tavaithuengnae hoi nei thuengnae phueng patetlah a younpap e lahoi maitotan thoseh, tutan, tuca kanaw e thoseh,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 yontha thueng nahanelah hmaetan buet touh hmaisawi thuengnae dawk pou poe lah kaawm e tavaithuengnae hoi nei thuengnae touksin laipalah na poe awh han.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 Hahoi a taruk hnin vah maitotan taroe, tutan kahni, tutanca kanaw e kum touh ka phat e kacueme hlaipali,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 tavai thuengnae hoi nei thuengnae phueng patetlah a younpap e lahoi maitotan thoseh, tutan, tuca kanaw e thoseh,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 yontha thueng nahanelah hmaetan buet touh hmaisawi thuengnae dawk pou poe lah kaawm e tavaithuengnae hoi nei thuengnae touksin laipalah na poe awh han.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 Hahoi asari hnin vah maitotan kanaw e sari, tutan kahni, tutanca kanaw e kum touh ka phat e kacueme hlaipali,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 tavai thuengnae hoi nei thuengnae phueng patetlah a younpap e lahoi maitotan thoseh, tutan, tuca kanaw e thoseh,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 yontha thueng nahanelah hmaetan buet touh hmaisawi thuengnae dawk pou poe lah kaawm e tavaithuengnae hoi nei thuengnae touksin laipalah na poe awh han.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 Hahoi ataroe hnin vah ka sungrenpoung lah kamkhuengnae pawi na tawn awh han. Bang thaw hai na tawk awh mahoeh.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 BAWIPA hanlah hmaisawi thuengnae na pou awh han. Maitotan kanaw e buet touh, tutan buet touh, tuca kanaw e kum touh ka pha e kacueme sari touh,
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 tavai thuengnae hoi nei thuengnae phueng patetlah a younpap e lahoi maitotan thoseh, tutan, tuca kanaw e thoseh, aphung patetlah a younpap lahoi,
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 yontha thueng nahanelah hmaetan buet touh, hmaisawi thuengnae dawk pou na poe awh e tavaithuengnae hoi nei thuengnae touksin laipalah,
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 lawk na kam awh e thoseh, nama ngai lahoi na poe awh e thoseh, tavaithuengnae hai thoseh, hmaisawi thuengnae thoseh, roum thuengnae thoseh, touksin laipalah, hetnaw heh atueng ka tawn e, pawi patetlah hoiyah BAWIPA koe na poe awh han tet pouh telah a ti.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 BAWIPA ni Mosi koe kâ a poe e naw pueng heh Mosi ni Isarel catounnaw koe a dei pouh.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.