< Matthai 15 >
1 Hatnavah, Jerusalem e Farasinaw hoi cakathutkungnaw teh Jisuh koe a tho awh.
Pamenepo Afarisi ena ndi aphunzitsi amalamulo anabwera kwa Yesu kuchokera ku Yerusalemu ndipo anamufunsa kuti,
2 Ayan e kacuenaw e phung hah bangkongmaw na hnukkâbangnaw ni a tapoe awh. Ahnimouh ni kut kamsin laipalah bu a ca awh, telah atipouh awh navah,
“Chifukwa chiyani ophunzira anu amaphwanya mwambo wa akuluakulu? Iwo sasamba mʼmanja pakudya!”
3 Nangmouh ni ayan e phung hah kâuep laihoi bangkongmaw Cathut e kâpoelawk hah na tapoe van awh.
Yesu anayankha kuti, “Nanga chifukwa chiyani inu mumaphwanya lamulo la Mulungu chifukwa cha mwambo wa makolo anu?
4 Cathut e kâpoelawk teh na manu hoi na pa bari awh. Apihai manu hoi na pa hawihoehnae ka dei e teh due totouh thei lah awmseh telah a ti.
Pakuti Mulungu anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako’ ndipo ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’
5 Hatei, nangmouh ni na cangkhai awh e teh apipatet ni hai a manu na ou, a na pa na ou a poe hane hno hah, het hateh Cathut koe ka poe e doeh toe tet pawiteh,
Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukalirandira kuchokera kwa ine ndi mphatso yoperekedwa kwa Mulungu,’
6 a manu nakunghai, a na pa nakunghai bari ngai hoeh toe na ti awh. Hottelah patuen patuen na tawm awh e phung hoiyah Cathut e kâpoelawk na eknae doeh.
iye sakulemekeza nayo abambo ake ndipo ndi khalidwe lotere inu mumapeputsa nalo Mawu a Mulungu chifukwa cha mwambo wanu.
7 A lai kathout e taminaw, Isaiah ni nangmouh noe lahoi,
Inu anthu achiphamaso, Yesaya ananenera za inu kuti,
8 hete miphunnaw teh apâhni hoi na hnai awh teh apâhni hoi na bari a ei a lungthin teh kai hoi ahla.
“‘Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.
9 Tami e kâpoelawk hoiyah a kâpâtu awh teh, ayawmyin lah na bawk awh toe telah sut a dei e hah a tang tangngak atipouh.
Amandilambira Ine kwachabe ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.’”
10 Hattoteh ka kamkhuengnaw hah ama koe a kaw teh, thai awh nateh panuek awh haw.
Yesu anayitana gulu la anthu nati, “Mverani ndipo zindikirani.
11 Thung lah ka kâen e ni tami heh khin sak hoeh. Thung lahoi ka tâcawt e hno ni doeh na khin sak awh, atipouh.
Chimene chimalowa mʼkamwa mwa munthu sichimuchititsa kukhala woyipa, koma chimene chimatuluka mʼkamwa mwake, icho ndi chimene chimamuchititsa kukhala woyipa.”
12 A hnukkâbangnaw ni a hnai awh teh atu na dei e lawk heh Farasinaw ni a thai awh navah a lung apout awh tie na panue maw atipouh awh.
Pamenepo ophunzira anabwera kwa Iye ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukudziwa kuti Afarisi anakhumudwa pamene anamva mawu aja?”
13 Jisuh ni kalvanlae Apa ni a patûe hoeh e a kung kaawm e pueng hah ka phawk han.
Iye anayankha kuti, “Mbewu iliyonse imene Atate anga akumwamba sanadzale idzazulidwa ndi mizu yomwe.
14 La awm awh nah yawkaw seh. Ahnimouh teh mitdawnnaw kahrawikung mitdawnnaw doeh. A mit ka dawn reira kâhrawi pawiteh kahni touh hoi tangkom dawk ka bawt roi han doeh atipouh.
Alekeni, ndi atsogoleri osaona. Ngati munthu wosaona atsogolera wosaona mnzake, onse awiri adzagwera mʼdzenje.”
15 Piter ni Cathut e bangnuenae hah kaimouh koevah pâpho haw atipouh navah,
Petro anati, “Timasulireni fanizoli.”
16 Jisuh ni nangmouh teh atu sittouh lungang laipalah maw na o a rah.
Yesu anawafunsa kuti, “Kani ngakhale inunso simumvetsa?
17 Thung lah kâen e pueng teh von dawk ka cet ni teh alawilah a tâcawt tie heh na panuek awh hoeh rah maw.
Kodi inu simudziwa kuti chilichonse cholowa mʼkamwa chimapita mʼmimba ndipo kenaka chimatuluka kunja kwa thupi?
18 Thung lahoi ka tâcawt e hno teh lung dawk hoi ka tâcawt e a tho dawkvah tami hah kakhin sak e hno doeh.
Koma zinthu zimene zituluka mʼkamwa zimachokera mu mtima ndipo zimenezi zimamuchititsa munthu kukhala woyipa.
19 Kahawi hoeh e pouknae, tami theinae, kamsoumhoehe napui tongpa yonnae, napui kahlout hoi yonnae, ayâ e hno parunae, kamsoumhoehe kapanuekkhaikung lah kangduenae, ayâ minhmai mathoe saknae teh lungthung hoi a tâco dawkvah,
Pakuti mu mtima mumatuluka maganizo oyipa, zakupha, zachigololo, zadama, zakuba, zaumboni wonama ndi zachipongwe.
20 Tami kakhin sak e hnonaw doeh. Kamsin laipalah rawca canae ni tami khinsak hoeh atipouh.
Izi ndi zimene zimachititsa munthu kukhala woyipa; koma kudya ndi mʼmanja mosasamba sikumuchititsa munthu kukhala woyipa.”
21 Hathnukkhu Jisuh teh hote hmuen koehoi a kamthaw teh, Taire hoi Sidon kholah a cei.
Yesu atachoka kumalo amenewo anapita kudera la ku Turo ndi ku Sidoni.
22 Kanaan napui buet touh teh a tâco teh, Devit Capa kai hah na pahren haw. Ka canu teh kahrai ni puenghoi a rek atipouh eiteh kam touh hai pathung hoeh.
Mayi wa Chikanaani wochokera dera la komweko anabwera kwa Iye akulira, nati, “Ambuye, Mwana wa Davide, ndichitireni chifundo! Mwana wanga wamkazi akuzunzika kwambiri ndi chiwanda.”
23 A hnukkâbangnaw ni a hrawi awh teh, hote napui bout ban sak leih. Maimouh hnuk a kâbang teh a hram atipouh awh.
Yesu sanayankhe kanthu. Ndipo ophunzira ake anabwera namupempha Iye kuti, “Muwuzeni achoke chifukwa akulira mofuwula pambuyo pathu.”
24 Jisuh ni Isarel miphun kahmat e tunaw hloilah alouke miphunnaw onae koe kai hah na patoun hoeh atipouh.
Iye anayankha kuti, “Ine ndinatumidwa kwa nkhosa zotayika za Israeli zokha.”
25 Hote napui ni tabo laihoi Bawipa na rungngang ei bout atipouh.
Mayiyo anabwera ndi kugwada pamaso pake, nati, “Ambuye ndithandizeni!”
26 Hat toteh, Bawipa ni capa e rawca hah ui poe phung nahoeh bout atipouh.
Iye anayankha kuti, “Sibwino kutenga chakudya cha ana ndi kuponyera agalu.”
27 Napui ni hai oe, Bawipa, uinaw tie teh kabawt e burameinaw hah ouk a luep phung nahoehmaw bout atipouh toteh,
Mayiyo anati, “Inde Ambuye. Komatu ngakhale agalu amadya nyenyeswa zimene zimagwa kuchokera pa tebulo la mbuye wawo.”
28 Oe! napui nang teh na yuemnae a len tangngak. Na ngainae patetlah nang dawk awmseh atipouh navah, a canu teh hmawi a dam.
Pomwepo Yesu anayankha kuti, “Mayi iwe uli ndi chikhulupiriro chachikulu! Pempho lako lamveka.” Ndipo mwana wake wamkazi anachira nthawi yomweyo.
29 Jisuh ni hote hmuen koehoi a cei teh, Galilee tui koe a pha toteh, monsom a luen teh a tahung.
Yesu anachoka kumeneko napita mʼmbali mwa nyanja ya Galileya. Ndipo anakwera ku phiri nakhala pansi.
30 Tami moikapap ni khokkhem, mitdawn, lawka, kamkhuen e hoi alouke patawnae ka tawn e naw hah a thokhai awh teh a khok koevah a ta awh.
Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye ndi anthu olumala, osaona, ofa ziwalo, osayankhula ndi ena ambiri nawagoneka pa mapazi ake ndipo Iye anawachiritsa.
31 A patawnae pueng hah a dam sak dawkvah, lawkanaw ni lawk a dei thai, kamkhuennaw ni a dam awh, khokkhemnaw ni lam a cei awh, mitdawnnaw ni a hmu awh e hah ka kamkhuengnaw ni a hmu awh navah Isarelnaw e Cathut hah a pholen awh.
Anthu ataona osayankhula akuyankhula, ofa ziwalo akuchira, olumala miyendo akuyenda ndi osaona akuona anadabwa kwambiri. Ndipo analemekeza Mulungu wa Israeli.
32 Hattoteh Jisuh ni a hnukkâbangnaw hah a kaw teh, hete taminaw hah ka pahren poung. Hnin thum touh thung canei tawn laipalah kai koe ao awh toe. Lam vah tawn a langvaih, ka ti dawkvah, rawca cat laipalah ceisak hane ka ngainae awm hoeh atipouh.
Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala kale ndi Ine masiku atatu ndipo alibe chakudya. Ine sindifuna kuti apite kwawo ndi njala chifukwa angakomoke pa njira.”
33 A hnukkâbangnaw ni, het yit touh e tami kapap e naw ni kaboumlah a ca awh hane rawca hah hi kahrawngum vah kaimouh ni bangtelamaw ka hmu thai awh han atipouh awh.
Ophunzira anayankha kuti, “Ndikuti kumene tingakapeze buledi mʼtchire muno okwanira kudyetsa gulu lotere?”
34 Jisuh ni nangmouh koe vaiyei na yit touh maw kaawm atipouh. Ahnimouh ni vaiyei sari touh hoi tanga youn touh ao bout atipouh awh.
Yesu anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri ndi tinsomba pangʼono.”
35 Hattoteh tami kamkhuengnaw hah talai dawk tahung sak hanelah kâ a poe.
Iye anawuza gululo kuti likhale pansi.
36 Vaiyei sari touh hoi tanganaw hah a la teh lunghawinae lawk a dei hnukkhu, vaiyei hoi tanga hah a raen teh a hnukkâbangnaw hah patuen a poe.
Kenaka anatenga malofu asanu ndi awiri aja ndi tinsombato ndipo atayamika anagawa napatsa ophunzira ake ndipo iwo anagawira anthuwo.
37 Rangpui ni a boum awh toteh, ka cawi e hah a racawng awh navah tangthung sari touh akawi.
Onse anadya ndipo anakhuta. Pomaliza ophunzira anatolera zotsalira nadzaza madengu asanu ndi awiri.
38 Ka cat e naw abuemlah napuinaw hoi camonaw e dei laipalah 4,000 touh a pha.
Chiwerengero cha anthu amene anadya chinali 4,000 kupatula amayi ndi ana.
39 Hote taminaw hah a ceisak hnukkhu Magadan kho lah long hoi a cei.
Yesu atatha kuwuza gululo kuti lipite kwawo, analowa mʼbwato ndipo anapita kudera la Magadala.