< Mark 6 >

1 Hote hmuen koehoi a tâco teh a hnukkâbangnaw ni a hnuk a kâbang awh teh, a ma onae kho dawk a pha awh.
Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
2 Sabbath hnin vah Sinakok dawk a cangkhai navah tami pueng ni a thai awh teh kângairu awh. Hete hno hah bangtelah hoi maw a hmu vaw. Ahni ni a tawn e lungangnae teh bang patet e na maw, hettelah totouh thaonae hah bangtelah hoi maw a kamnue sak vaw.
Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
3 Ahni teh lettama nahoehmaw, Meri e a capa nahoehmaw, Jem, Jawhan, Joseph, Judah hoi Simon ahnimae a hmau nahoehmaw. A tawncanunaw hai maimae tengpam bo ao ei aw, ti teh a lungpout awh.
Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
4 Jisuh ni Profet teh ama kho aonae koe amae im hloilah barinae awm hoeh telah atipouh.
Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
5 Ka dam hoeh e tami youn touh van vah a kut a toung teh, a dam sak hloilah, hote hmuen koe thaonae kamnuek sak thai mahoeh.
Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
6 Ahnimanaw ni a yuem awh hoeh e a hmu navah, kângai a ru. Hahoi kho touh hoi kho touh a cei teh a cangkhai.
Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
7 A hnukkâbangnaw hlaikahni touh a kaw teh kahni kahni touh hoi a patoun. Kakhine muithanaw pâlei thainae kâ a poe teh,
Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
8 Kahlong na cei awh nah sonron hloilah yawngya, rawca hoi tangkabom dawk tangka na sin awh mahoeh.
Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
9 Khokkhawm khawm awh. Angki a cawi sin awh hanh telah atipouh.
Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
10 A im na ka luen sak e im dawkvah kho louk lah na cei hoehnahlan pueng cam pouh awh.
Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
11 Na phanae kho buet touh ni a im na luen sak hoeh, na dei e lawk tarawi awh hoehpawiteh hote hmuen koehoi na tâco nah na khok dawk e vaiphu kâkai e hah lawkpanuesaknae ao nahanlah takhawng sin awh.
Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
12 A hnukkâbangnaw a tâco awh teh, pankângainae lawk a pâpho awh.
Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
13 Kahraituilinaw a pâlei awh. Kapatawnaw satui a hluk awh teh, a dam sak awh.
Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
14 Jisuh e kamthang teh kho tangkuem vah a kamthang dawkvah, Herod siangpahrang ni hai hote kamthang a thai van. Tami tangawn ni baptisma kapoekung Jawhan teh duenae koehoi bout a thaw. Hatdawkvah, het patet e kângairu hnosakthainae bahu hah a tawn, telah a dei awh.
Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
15 Tangawn ni ahni teh Elijah doeh ati awh. Tami alouknaw ni ayan e profetnaw patetlah e profet buetbuet touh doeh ati awh.
Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
16 Hote lawk Herod ni a thai navah, tui baptisma kapoekung Jawhan doeh. Kai ni a lahuen yo ka tâtueng sak eiteh duenae koehoi bout a thaw telah a ti.
Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
17 Herod ni a nawngha Filip e a yu Herodias hah a yu lah a la teh, hote napui kecu dawk Jawhan hah thongim a paung.
Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
18 Bangkongtetpawiteh, Jawhan ni nang ni na hmau e a yu na yu lah na la e heh hawihoeh telah atipouh dawk doeh.
Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
19 Hatdawkvah Herodias ni Jawhan hah a pahluem teh thei han a ngai ei thet thai hoeh.
Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
20 Bangkongtetpawiteh Herod ni Jawhan teh tamikalan, tami kathoung tie a panue dawkvah a taki teh a bari, a kabawp. A lawk hai a thai pouh dawkvah hote napui ni thei nahane a lam hmawt thai hoeh.
chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
21 Herod khenae hnin nah kum tangkuem pawi ouk a sak awh e patetlah, ukkung bawinaw, ransabawinaw, Galilee ram e bawinaw teh pawi koe a tho awh.
Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
22 Hote pawi koevah Herodias e canu a kâen teh a lam navah, Herod hoi a coun e naw teh a lung a nawm poung awh. Hatdawkvah, Herod siangpahrang ni tangla hanelah, bangmaw na ngai, na hei e pueng na poe han atipouh.
Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
23 Ka uknaeram tangawn totouh na poe han telah lawk a kam pouh.
Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
24 Tangla ni a manu koe a cei teh bangmaw ka hei han atipouh navah, a manu ni baptisma kapoekung Jawhan e a lû hah het atipouh.
Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
25 Tangla ni Herod koevah a cei teh, atu roeroe baptisma kapoekung Jawhan e a lû teh tongben dawk hoi na poe telah atipouh.
Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
26 Ahnie lawk a thai nah, Herod teh a lungmathoe. Hatei, a coun e bawinaw hoi kacuenaw hmalah lawk a kam dawkvah, kangek thai hoeh toe.
Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
27 Hatdawkvah, ransa buet touh thongim thung a patoun teh, Jawhan e lû tho khai hanelah kâ a poe. Hahoi ahni ni hnie lû a tâtueng pouh.
Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
28 Jawhan e a lû teh tongben dawk hoi a thokhai teh tangla hah a poe teh ahni ni a manu koe patuen bout a poe.
nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
29 Hote kamthang teh a hnukkâbangnaw ni a thai nah a ro a la awh teh a pakawp awh.
Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
30 Gunceinaw ni Jisuh koe a kamkhueng awh teh a tawk a sak e naw pueng a dei pouh awh.
Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
31 Jisuh ni, kahrawngum vah tho awh, dawngdeng kâhat awh ei, atipouh. Telah a deingainae teh, kâhlumkâhlai e apap dawkvah, rawca ca nahane tueng boehai a hmu awh hoeh dawk doeh.
Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
32 Hatdawkvah long a kâcui awh teh, kahrawum vah a cei awh.
Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
33 Hateiteh, a cei awh e hah taminaw ni a hmu awh teh, Jisuh doeh tie a panue awh toteh, khoram tangkuem e taminaw teh mon lam lahoi a yawng awh teh, a hnukkâbangnaw a pha awh hoehnahlan hmaloe a pha awh teh, Jisuh koe a la kamkhueng awh.
Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
34 Jisuh ni long dawk hoi a kum teh, tamihupui a hmu navah, tukhoumkung kaawm hoeh e tuhunaw patetlah a hmu dawkvah, a lungpataw teh, moikapap a cangkhai.
Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
35 Kho a hmo navah, a hnukkâbangnaw ni a hnai awh teh, hete hmuen teh thingyeiyawn doeh. Kho hai a hmo toe.
Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
36 Taminaw teh tengpam e khonaw koe amamouh hane rawca ran sak hanelah patoun ei, atipouh awh.
Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
37 Hatnavah, Jisuh ni ahnimouh canei hanelah nangmouh ni poe awh, atipouh. A hnukkâbangnaw ni ngun tangka cumhni touh phu rawca ran vaiteh ka poe awh han maw atipouh awh.
Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
38 Jisuh ni nangmouh koe vaiyei na na yit touh maw kaawm, cet nateh khenhaw! atipouh navah, vaiyei panga touh hoi tanga kahni touh ao atipouh.
Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
39 Hatnavah taminaw pueng teh marangpho van vah hlouphloup lahoi tahung sak hanelah kâ a poe.
Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
40 Ahnimouh teh cum touh, ruipanga touh telah hoi hlouphloup lahoi a tahung sak awh.
Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
41 Jisuh ni vaiyei panga touh hoi tanga kahni touh a la teh kalvan lah a moung teh lunghawinae lawk a dei hnukkhu vaiyei a raen teh taminaw pueng rei hanelah a hnukkâbangnaw koe a poe. Tanga kahni touh e hai a la teh taminaw pueng a rei sak.
Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
42 Taminaw pueng ni koung ka boum lah a ca awh.
Onse anadya ndipo anakhuta,
43 Hathnukkhu hoi kacawie vaiyei hoi tanga a pâkhueng awh navah, tangthung hlaikahni touh akawi.
ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
44 Vaiyei kacate tongpa 5,000 touh hane a pha.
Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
45 Hathnukkhu hoi Jisuh ni a hnukkâbangnaw long dawk a luen sak teh tuipui namran lah Bethsaida kho dawk hmalah a ceisak teh tamihupui teh bout a ban sak.
Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
46 Taminaw a ban sak hnukkhu Jisuh teh ratoum hanlah mon vah a luen.
Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
47 Karum a pha navah long teh, tuipui lungui vah ao. Jisuh teh ama dueng namran lah ao.
Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
48 Kahlî ni a pâban dawkvah, long a mawng awh e nget a tawn awh e hah, Jisuh ni a hmu. Amom khodai hoehnahlan tui van a cei teh a hnukkâbangnaw ceihlawi hane patetlah a cei pouh.
Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
49 A hnukkâbangnaw ni Jisuh tuipui van a cei e a hmu awh navah, kahraituili lah a pouk awh dawkvah a hramki awh.
koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
50 Hatnavah a hnukkâbangnaw teh a tâsue poung awh. Jisuh ni taket awh hanh, Kai doeh telah tang atipouh.
pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
51 Hahoi long thung ahnimouh koe a kâen teh kahlî teh a roum. A hnukkâbangnaw teh kângai hroung a ru awh.
Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
52 Bangkongtetpawiteh, vaiyei dawk kângairu a sak e hah a lungpata a dawk banglahai ngai awh hoeh.
popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
53 Hathnukkhu hoi tui namran lah a raka awh teh Kennesaret kho dawk a pha awh navah, long a kâhat sak awh.
Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
54 Long dawk hoi a kum navah taminaw ni Jisuh a hmu awh teh tang a nout awh dawkvah,
Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
55 Atengpam e kho pueng koe a yawng awh teh, hote hmuen koe Jisuh ao tie a thai awh navah, kapatawnaw hah a kâkayawt awh teh a thokhai awh.
Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
56 Jisuh a ceinae khopui hoi khote dawk hai thoseh, taminaw ni ka dam hoeh e naw hah lam teng a ta awh teh, Jisuh e hni pawi tek sak hanelah ama koe a kâhei awh. Ka tek e naw pueng ni a dam awh.
Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.

< Mark 6 >