< Luk 15 >

1 Tamuk kacawngnaw hoi tamikayonnaw ni Bawipa e cangkhainae thai hanelah ama koe a tho awh.
Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake.
2 Farasi hoi cakathutkungnaw niyah hete tami teh tamikayonnaw hoi rei a o, ahnimouh hoi cungtalah bu rei a ca telah yon a pen awh.
Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”
3 Hatnavah bangnuenae lawk a dei e teh nangmouh dawk tami buetbuet touh ni tu cum touh a tawn.
Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili:
4 Hotnaw thung dawk e tu buet touh kahmat pawiteh 99 touh e tunaw hah kahrawngum a ta vaiteh kahmat e tu buet touh a hmu hoeh roukrak a cei teh tawng laipalah ao han maw.
“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza?
5 A hmu torei teh a lunghawi teh a loung dawk a thueng teh,
Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe
6 im a pha torei teh a huikonaw hoi a imrinaw a kaw teh kahmat e tu bout ka hmu toe, cungtalah konawm khai awh haw telah a dei han.
ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’
7 Hot patetlah pankângai han ka tawn hoeh e tami 99 touh hlakvah pankângai e tamikayon buet touh koe kalvan vah a lunghawinae bet ao hnawn telah a ti.
Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”
8 Hottelah napui buet touh ni phoisa phek hra touh a tawn. Phek touh kahmat pawiteh hmai paang vaiteh a hmu hoeh roukrak imthungkhu imka pâthoun vaiteh kahawicalah tawng laipalah ao han maw.
“Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza?
9 A hmu torei teh a huikonaw hoi imrinaw a kaw vaiteh kahmat e phoisa bout ka hmu toe, cungtalah konawm khai awh haw telah ati han.
Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’
10 Hot patetvanlah, Cathut e kalvantaminaw ni pankângai e tamikayon buet touh dawkvah lunghawinae a tawn awh, telah atipouh.
Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”
11 Bout a dei e teh tami buet touh ni ca tongpa kahni touh a tawn,
Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri.
12 A ca cahnoung ni a na pa koe a cei teh apa, ka hmu hane kawi râw na kapek pouh leih telah a kâhei teh a na pa ni hnopainaw pueng a kapek teh a poe.
Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.
13 Hathnukkhu hoi a ca cahnoung ni amae hnopainaw pueng a la teh kahlatpoung e ram dawk a cei teh hote ram dawkvah talai nawmnae dawk a ngai patetlah kho a sak teh hnopainaw pueng koung a kaseikasak.
“Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko.
14 A tawn e hnopai koung a pâbaw hnukkhu hote ram dawk takang puenghoi a tho teh puenghoi roedengnae koe a pha.
Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka.
15 Hatdawkvah hote ram dawk tami buet touh koe o hanelah a cei teh hote tami ni vok ring hanelah a patoun.
Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba.
16 Ahni teh vok rawca patenghai ca hane ngai totouh a vonhlam, hatei apinihai rawca banghai poe awh hoeh.
Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.
17 Hatnavah a lung vuk a ang teh apa im vah aphu hmu hanelah hoi a ta e a sannaw ni boeba hai cat laipalah ca hane a tawn, kai teh hivah vonhlam hoi ka o.
“Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala!
18 Ka thaw vaiteh apa koe ka cei han. Apa, kai ni kalvan hoi na hmaitung vah ka yon toe.
Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu.
19 Na ca ti hanelah ka kamcu hoeh. Na san buet touh lah o hanelah na tat lawih ka ti han a ti.
Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’
20 Hatdawkvah, a na pa koe ban hanelah a kamthaw. Lam ahlapoungnae koe a tho e a na pa ni a hmu navah a pahren dawk a yawng sin teh a takawi teh a paco.
Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake. “Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.
21 A capa ni vah a Pa kalvan koe thoseh, na hmaitung thoseh, ka yon toe. Na ca ti han ka kamcu hoeh toe telah a ti.
“Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’
22 A na pa ni vah aphu kaawm poung e angki lat nateh kho sak awh, a kut dawk kuthrawt buen sak awh.
“Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato.
23 Khokkhawm hai khawm sak awh, hahoi Maito ca kathâwpoung e lat nateh thet awh, kanawm poung lah pawi sak awh sei.
Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera.
24 Bangkongtetpawiteh ka capa teh a due toe, hatei atu bout a hring. A kahma, hateiteh atu bout ka hmu toe ati. Hottelah hoi pawi teh a kamtawng awh.
Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.
25 A capa kacue ni law hoi a ban teh im teng a pha navah ratoung tamawi lawk hoi lamtu e a thai.
“Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina.
26 A san buet touh a kaw teh bangmaw na sak awh, telah a pacei.
Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika.
27 A san ni vah na nawngha ka dam lahoi im bout a tho dawkvah, na pa ni maito ca kathâw e a thei pouh telah atipouh. A capa kacue e teh a lungphuen teh im dawkvah kâen laipalah ao.
Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’
28 A na pa ni capa kacue koe a cei teh kâen leih telah a pasawt.
“Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira.
29 A capa kacue ni hai kai ni atueng moi kasawlah apa, nange san patetlah thaw ka tawk, vai touh boehai nange kâpoelawk ka tapoe hoeh. Hateiteh kai ni ka huinaw hoi cungtalah nawmnae sak hanelah hmae boehai na poe hoeh.
Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga.
30 Ka kâyawt e napuinaw hoi kaawm ni teh na hnopai kaseikasak e na ca cahnoung, im bout a pha torei teh maito ca kathâw kathâw na thei pouh telah a ti.
Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’”
31 A na pa ni, ka ca nang teh ka im vah yungyoe na o teh ka tawn e hnopueng nange hno lah ao.
Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako.
32 Hatei na nawngha teh a due eiteh, atu bout a hring. A kahma eiteh atu bout hmu toe. Hatdawkvah lunghawi khai hane roeroe lah ao telah a na pa ni atipouh.
Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”

< Luk 15 >