< Bawknae 16 >
1 Aron e capa roi ni BAWIPA hmalah thuengnae a sak teh a due roi hnukkhu, BAWIPA ni Mosi koe a dei pouh e teh,
Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
2 Na hmau Aron ni a due hoeh nahanelah, hmuen kathoung dawk thingkong van, lungmanae tungkhung hmalah nâtuek hai kâen sak hanh. Kai teh thingkong van, lungmanae tungkhung hmalah tâmai dawk hoi ka kamnue han.
Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
3 Aron ni lukkarei hmuen kathoung thung bangtelah hoi maw a kâen han tetpawiteh, yon thueng nahanelah, a kum kanaw e maitotan buet touh, hmaisawi thueng nahanelah tutan buet touh a thokhai han.
“Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
4 Kathounge lukkarei angki hoi hna a khohna vaiteh lukkarei taisawm a kâyeng han. Lukkarei lupawk hai a pawk han. Hote khohnanaw teh a thoung dawkvah, tui a kamhluk hnukkhu a khohna han.
Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
5 Isarel miphun tamimaya naw koe e, yon thueng nahanelah hmaeca kahni touh, hmaisawi thueng nahanelah tu buet touh a la han.
Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
6 Aron ni amae yon thueng nahanelah maito a thueng vaiteh, ama hoi a imthungkhunaw hanelah yonthanae a sak han.
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
7 Hmae kahni touh hai a thokhai vaiteh, kamkhuengnae lukkareiim takhang koe, Cathut hmalah a poe han.
Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
8 Aron ni hmae kahni touh hane kong dawk cungpam a rayu han. Buet touh e Cathut hanelah a rayu vaiteh, bout touh e teh kahrawngum tha hanelah a rayu han.
Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
9 Cathut e cungpam lah a rayu e hmae teh Aron ni a la vaiteh yon thueng nahanelah a thueng han.
Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
10 Tha hanelah cungpam a rayu e hmae teh a hring lahoi Cathut hmalah a poe vaiteh, a lathueng yonthanae a sak hnukkhu, kahrawngum a nganae koe a tha han.
Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
11 Aron ni amae yon thueng nahanelah maito a thokhai hnukkhu, ama hoi a imthungkhunaw hanelah yonthanae a sak vaiteh, amae yon thuengnae maito a thei han.
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
12 Cathut hmalah khoungroe hmaisaan hoi kakawi e tongben buet touh a la vaiteh, kanui lah phawm e hmuitui kutvang touh hoi, lukkarei yap e athunglah kâenkhai han.
Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
13 Aron ni duenae dawk hoi a hlout nahanelah hmuitui e hmaikhu ni lawkpanuesaknae thingkong khuem hmuitui sak hanelah BAWIPA hmalah hmuitui van a phuen han.
Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
14 Maito thi youn touh a la vaiteh, Kanîtholah thingkong khuem van a kutdawn hoi a kahei han. Thingkong khuem a hmalah hai vai sari touh a kutdawn hoi a kahei han.
Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
15 Hathnukkhu, taminaw hanelah yon thuengnae hmae a thei vaiteh, a thi hah lukkarei yap e athunglah a kâenkhai hnukkhu, maito thi a kahei e patetlah thingkong khuem van thoseh, a hmalah hai thoseh, a kahei han.
“Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
16 Isarel miphunnaw e thounghoehnae yon dawk thoseh, kâtapoenae yon pueng dawk thoseh, hmuen kathoung hanelah yonthanae a sak han. Hottelah, Isarel miphunnaw thounghoehnaw yon thung kaawm e naw kamkhuengnae lukkareiim hanelah a sak han.
Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
17 Hmuen kathoung koe yonthanae sak hanelah, a kâen nah, ama hanelah a imthungnaw hanelah, Isarel miphun abuemlah hanelah, yonthanae a sak teh, a tâco hoehroukrak kamkhuengnae lukkareiim thung apihai awm mahoeh.
Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
18 BAWIPA hmalah khoungroe koe bout a tâco vaiteh, yonthanae a sak hanelah, maito thi, hmae thi, a la vaiteh khoungroe kinaw dawk a hlun han.
“Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
19 Thuengnae khoungroe van hai hote thi hah a kutdawn hoi vai sari touh a kahei vaiteh, Isarel miphunnaw e thounghoehnae a thoung sak han.
Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
20 Hottelah, hmuen kathoung hanelah, kamkhuengnae lukkareiim hanelah, khoungroe hanelah, yonthanae a sak hnukkhu, hmae a hring lah a thokhai han.
“Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
21 Aron ni kahring e hmae lû van a kut kahni touh hoi a toung vaiteh, Isarel miphunnaw e yonnae naw hoi a sakpayonnae pueng yonpâpho vaiteh, hmae lû van a toung pouh hnukkhu, a rawi e tami buet touh ni kahrawngum a ceikhai han.
Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
22 Ahnimae yonnae pueng tami ohoehnae hmuen koe ka cetkhai e hote hmae hah kahrawngum a tha han.
Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
23 Aron ni kamkhuengnae lukkareiim thung bout a kâen vaiteh, hmuen kathoung koe apasuek a kâen navah, a kho e loukloukkaang e khohna a kho e hah a rading vaiteh, hmuen kathoung koe a ta han.
“Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
24 Hmuen kathoung koe tui a kamhluk vaiteh amae khohna a khohna hnukkhu, bout a tâco vaiteh, Ama hoi taminaw hanelah hmaisawi thuengnae sathei hah a thueng vaiteh, Ama hoi ayânaw hanelah yonthanae a sak han.
Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
25 Yon thuengnae sathei thaw teh khoungroe van vah hmai a sawi han.
Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
26 Kahrawngum hmae ka tha e tami hai amae khohna a pâsu vaiteh tui a kamhluk hnukkhu, a onae rim dawk bout a kâen han.
“Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
27 Yon thuengnae maito hoi yon thuengnae hmae thi yonthanae sak hanelah hmuen kathoung koe kâenkhai e hah rim alawilah a ceikhai han. A pho, a moi, hoi a ei hah hmaisawi han.
Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
28 Hmai ka sawi e tami hai amae khohna a pâsu vaiteh, tui a kamhluk han. Hathnukkhu, roenae rim koe a cei han.
Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
29 Nangmouh ni na tarawi awh hane phung teh Isarelnaw thoseh, nangmouh koe kaawm e imyinnaw thoseh, Asari e thapa, hnin hra hnin vah, thaw na tawk awh mahoeh. Na kâhat awh han.
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
30 Bangkongtetpawiteh, BAWIPA hmalah nangmanaw yonnae pueng dawk hoi na thoung awh nahanelah, hote hnin dawk vaihma ni nangmouh na thoung a nahanelah yonthanae a sak han.
chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
31 Hote hnin teh nangmouh na kâhat nahanelah sabbath hnin lah ao dawkvah duem na kâhat awh han.
Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
32 A na pa e yueng lah vaihma thaw ka tawk hanelah, apasueke vaihma kut dawk hoi satui awi lah kaawm e tami ni yonthanae a sak han. Hote vaihma teh kathounge lukkarei khohna a khohna han.
Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
33 Hmuen kathoung hanelah, kamkhuengnae lukkareiim hanelah, khoungroe hanelah, vaihmanaw hanelah, tami pueng hanelah yonthanae a sak han.
Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
34 Hete phung teh Isarel miphunnaw ni a yonnae kaawm pueng dawk, kum touh dawk vai touh, yonthanae sak hanelah, nangmouh ni pou na tarawi a hanelah, kâpoe e lah ao telah Cathut ni Mosi koe lawkthui e patetlah Aron ni a sak.
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.