< Jeremiah 26 >
1 Judah siangpahrang Josiah capa Jehoiakim a bawinae kamtawng nah hete lawk BAWIPA koe hoi a tho.
Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 BAWIPA ni hettelah a dei, BAWIPA e im thongma dawk kangdout haw, Judah khopuinaw pueng ni Cathut bawk hanlah BAWIPA e im dawk kathonaw pueng koe dei hanlah na poe e lawknaw hah buet touh hai pâhma laipalah dei pouh.
“Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
3 Yonnae a sak awh dawkvah ahnimae lathueng thoenae sak hanlah ka kâcai e let ka kâhno thai nahanlah tamipueng ni a yonae hah kamlang takhai teh, thai hanlah a ngai thai yawkaw han doeh.
Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
4 Nang ni ahnimouh koevah, BAWIPA ni hettelah a dei, kaie lawk na thai ngai awh hoeh teh, nangmae hmalah ka ta e kâlawknaw tarawi ngai hoeh dawkvah,
Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
5 amom ka thaw teh ka patoun e ka thaw ka tawk e profetnaw e lawk hah banglahai noutna awh hoeh pawiteh,
ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
6 hete im heh Shiloh patetlah ka o sak vaiteh talai van e miphunnaw pueng ni thoebo e khopui lah ka coung sak han, telah na ti han, telah ati.
ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
7 Vaihmanaw hoi profetnaw hoi tamimaya ni BAWIPA im dawk Jeremiah ni a dei e lawk hah a thai awh.
Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
8 Hahoi hettelah o, tamimaya koe dei hanelah BAWIPA ni a poe e lawknaw pueng he a dei hnukkhu vaihma, profet hoi tamimaya ni, a man awh teh na due roeroe han!
Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
9 Bangkongmaw BAWIPA e min lahoi, hete im heh Shiloh patetlah ao vaiteh hete khopui dawk tami awm laipalah kingdi han telah na dei, telah ati awh. Hattoteh BAWIPA e im dawk taminaw pueng ni Jeremiah teh a cusin awh.
Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
10 Judah kahrawikungnaw ni hete kong a thai awh toteh siangpahrang im dawk e BAWIPA e im longkha katha koe a tahung awh.
Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
11 Vaihma hoi profetnaw ni kahrawikungnaw hoi tamihu koe, hete tami he due hanlah a kamcu. Bangkongtetpawiteh, hnâ hoi na thai e patetlah hete khopui taranlahoi a pâpho toe, telah ati awh.
Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
12 Kahrawikungnaw pueng hoi taminaw pueng koe Jeremiah ni, lawknaw pueng na thai awh e patetlah, hete im hoi khopui raphoe hane kong dei hanelah BAWIPA ni na patoun.
Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
13 Hatdawkvah, atu na hringnuen hoi na khosaknae hah pathoup awh nateh BAWIPA Cathut e lawk hah yuem awh, telah pawiteh, BAWIPA ni nangmae lathueng hawihoehnae pha sak hanlah a pâpho tangcoung e hah bout a kâhno han.
Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
14 Kai hah teh, atu nangmae kut dawk ka o, a lan, ahawi na ti awh e patetlah, kaie lathueng vah sak awh.
Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
15 Kai na thet payon awh pawiteh namamouh hoi hete khopui hoi athung kaawmnaw pueng koe yonnae kaawm hoeh e thipaling na pha sak awh tie hah panuek awh. Atangcalah hete lawknaw heh na hnâthai awhnae koe dei hanelah BAWIPA ni na patoun e doeh, telah ati.
Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
16 Hat toteh, kahrawikungnaw hoi tamimaya ni, vaihma hoi profetnaw koevah, hete tami heh due hanelah kamcu hoeh, bangkongtetpawiteh, BAWIPA maimae Cathut min lahoi maimouh koe lawk a dei toe, telah ati awh.
Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
17 Hote ram dawk e kacuenaw a kangdue awh teh, tamimaya koevah,
Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
18 Mikah Morashtite tami ni Judah siangpahrang Hezekiah a bawi navah lawk a pâpho, hahoi Judah taminaw pueng koe, ransahu BAWIPA ni hettelah a dei. Zion teh laikawk patetlah thawn e lah ao han, Jerusalem teh songnawng lah o vaiteh, bawkim mon teh ratu hmuenrasang patetlah ao han, telah ati.
“Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
19 Judah siangpahrang Hezekiah hoi Judah taminaw pueng ni ahni hah a thei awh maw. BAWIPA taki lahoi BAWIPA ni ngaikhainae doeh a pacei awh teh, BAWIPA ni ahnimae lathueng hawihoehnae pha sak hane hah bout a kâhno nahoehmaw. Hatei, maimouh teh kalenpounge hawihoehnae hah mamouh taranlahoi sak awh.
Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
20 Hahoi alouke tami BAWIPA e min lahoi lawk ka dei e Kiriath tami Shemaiah capa Uriah hah bout ao. Jeremiah ni a dei e naw patetlah hete ram hoi khopui raphoe hane kong hah a dei.
(Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
21 Siangpahrang Jehoiakim hoi athakaawme taminaw hoi kahrawikungnaw pueng ni a thai awh toteh, siangpahrang ni thei hanelah a kâcai. Hatei, Uriah ni a thai toteh a taki teh Izip ram lah a yawng.
Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
22 Hahoi siangpahrang Jehoiakim ni Izip ram lah Akbor capa Elnathan hoi alouke taminaw hoi a patoun.
Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
23 Izip ram dawk hoi Uriah a tâcokhai awh teh siangpahrang Jehoiakim koevah a thokhai awh, ama ni tahloi hoi a thei teh a ro hah lam teng mathoenaw e phuen dawk a tâkhawng, telah ati awh.
Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
24 Hatei, Shaphan capa Ahikam ni Jeremiah a kampangkhai dawkvah, thei hanelah tamimaya e kut dawk poe hoeh.
Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.