< Isaiah 14 >

1 Bangkongtetpawiteh, BAWIPA ni Jakop imthung hah a pahren dawkvah, Isarelnaw hah bout a rawi teh, amamae ram dawk ahnimanaw hah a hmuen a poe han. Ramlouknaw ni ahnimouh koe ao awh van han.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 Miphunnaw ni ahnimouh teh, amamae ram dawk a thokhai awh han. Isarelnaw ni miphunnaw e napui tongpanaw hah san lah a tawn awh han. Ahnimouh ni ahnimouh kamankungnaw hah a man awh han. Ahnimouh ka rektap e naw hai a uk awh han.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 BAWIPA ni nange patawnae, temdengnae, ka ru e thaw na tawk saknae koehoi nang hlout sak nahan lah BAWIPA e hnin teh a tho han.
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 Hattoteh, nangmouh ni Babilon siangpahrang hanelah hettelah bangnuenae na dei awh han, talai ka rektap e teh hete tami nahoehmaw, a uknaeram teh a rawp bo toung vaw.
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 BAWIPA teh tamikathoutnaw e sonron, ukkungnaw e tahroe hah a khoe pouh.
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 Hote ni pout laipalah hemnae hoiyah taminaw hah lungkhueknae hoi a hem. Pahrennae awm laipalah, rektap teh lungkhueknae miphunnaw hah a uk
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 Talaivan pueng teh duem a kâhat teh, la sak lawk ni a katin.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 Hmaica thingnaw ni nang koe a lunghawi awh. Lebanon mon kaawm e sidar thingnaw ni, nang na rawp hnukkhu, kaimouh na ka tâtueng hane luen takhang hoeh toe ati awh.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 Nang na tho toteh dawn hanelah, tami kadout kho teh a kâcai. Talai ukkungnaw pueng a hroecoe teh, ram tangkuem e siangpahrangnaw pueng hai amamae bawitungkhung dawk hoi a thaw sak. (Sheol h7585)
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
10 Ahnimouh pueng ni na pathungnae lah a dei awh e teh, nang hai kaimouh patetlah na tha a youn teh, kaimouh hoi rei na kâvan bo vaw
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 Nange raim onae, nange ratoung lawk teh tami kadout kho a cei awh toe. Pârinaw teh na yan nahanelah ao teh, ahrinaw teh na kâkhu e lah ao. (Sheol h7585)
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
12 Oe Khosei capa (Lucifer), amom tempalo, kalvan hoi na bo toe. Ram pueng na kata e, nang teh talai dawk rek na taben toe khe.
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 Nama ni teh na lungthung hoi hettelah na dei. Kalvan vah ka luen han. Cathut e âsinaw lathueng vah, ka tahungnae bawitungkhung ka rasang sak han. Atunglah kaawm e kamkhuengnae mon dawk ka tahung han.
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 Tâmainaw e lathueng ka luen han. Lathueng Poung e Cathut patetlah ka kâsak han.
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Hatei, nang teh tami kadout kho, kadung poung e tangkom thung na bo toe. (Sheol h7585)
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
16 Nang na kahmawt e naw ni nang hah na khet awh teh, talai kâhuen sak e tami, ram pueng kâhuen sak e tami,
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 talaivan heh kahrawngum patetlah ka coung sak niteh, khopuinaw hah ka raphoe e, a man e naw hah ama im bout ban sak hanelah kâ ka poe hoeh e teh hete tami han namaw, na ti pouh awh han.
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 Ram tangkuem e siangpahrangnaw pueng teh, amamae tangkom dawk bawilennae hoi a yan awh.
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 Hatei, nang teh panuettho e thingkang patetlah na tangkom dawk hoi takhoe lah na o toe. Thei lah kaawm e, tahloi hoi thut lah kaawm e, talung tangkom thung ka cet e naw hoi ramuk lah na o teh, khok hoi coungroe e ro patetlah doeh na o toe.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 Nang teh ahnimouh hoi rei pakawp mahoeh. Bangkongtetpawiteh, nang teh, nama e ram hah na raphoe teh, na taminaw hah na thei toe. Hawihoehnae ka sak e a catounnaw teh nâtuek hai a min bout dei mahoeh toe.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Ahnimae a canaw teh, amamae napanaw e yon kecu dawkvah, thei nahane hmuen hah rakueng awh. Ahnimouh thung hoi apihai talai ukkung awm mahoeh toe. Talaivan kho hai kangdout sak awh mahoeh toe.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 Rasahu BAWIPA ni, ahnimouh hoi kâtaran lah ka o han. Babilon kho dawk hoi ahnie min hoi kacawie naw thoseh, a ca catounnaw hai thoseh ka raphoe han telah ati.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 Babilon kho teh sambuem lah ka o sak vaiteh, bukbu onae lah ka ta han. Raphoenae sampho hoi ka pâthoun han telah ransahu BAWIPA ni a pathang.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 Rasahu BAWIPA ni, ka pouk e patetlah ao han. Ka noe e patetlah ka sak han.
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 Assirianaw hah ka ram dawk rek ka hem vaiteh, kama e monnaw dawkvah, rep ka coungroe han. Ahnie yawcu hah ka takhoe pouh vaiteh, a hno hah a loung dawk hoi ka takhoe pouh han telah thoe a kâbo teh a dei.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 Hethateh, talai van puenghoi kâkuen e ka noenae doeh. Hathateh, ram pueng koe ka dâw e kut doeh
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 Bangkongtetpawiteh, ransahu BAWIPA ni a noe toe. Apinimouh a oun thai han. BAWIPA e kut teh a dâw toe. Apinimouh a hno sak thai han.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 Ahaz siangpahrang a duenae kum dawk hete lawk teh a tho.
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 Filistin khocanaw, nangmouh na hemnae bongpai a lawt dawk na lunghawi awh hanh. Bangkongtetpawiteh, tahrun phun dawk hoi hrunthoe a khe awh han. Hote a canaw hai kamleng thai e hmaitahrun lah ao awh han.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Mathoenaw e caminnaw hai kawkhik lah ao han. Mathoemaranaw hai kahawicalah a i awh han. Hatei, nange tangpha teh takang hoi ka thei han. Kacawie naw hai thei lah ao han.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 Oe kho longkha, cingou haw. Oe khopui, khuikap haw. Filistinnaw pueng teh taki hoi a pâyaw awh. Bangkongtetpawiteh, atunglah hoi hmaikhu a tâco. Hote ransahu dawkvah, kampek e awm hoeh.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 Ahnimouh ni, ram tangkuem e patounenaw koe bangtelamaw a dei pouh han vai. BAWIPA ni Zion kho hah a kangdue sak teh, mathoenaw ni hote kho dawk a kângue awh han.
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

< Isaiah 14 >