< 2 Kawrin 7 >
1 Ka pahren e naw, maimouh koe het patetlah lawkkamnae ao dawkvah, takthai hoi lungthin dawk khinnae pueng teh mahoima kâcai sak vaiteh, Cathut taki laihoi thoungnae hoi kawi a sei.
Abwenzi okondedwa, popeza tili ndi malonjezo amenewa, tiyeni tidziyeretse, kusiyana nazo zilizonse zimene zikhoza kudetsa thupi ndi mzimu, ndipo tiyesetse kukhala oyera mtima poopa Mulungu.
2 Kaimanaw na dâw a loe. Kaimouh ni api koehai ka payon awh hoeh. Apipatethai ka rawk sak awh hoeh. Api koehai huenghai hoi ka cat awh hoeh.
Mutipatse malo mʼmitima mwanu. Ife sitinalakwire munthu aliyense, kapena kuyipitsa munthu aliyense, kapena kumuchenjerera munthu aliyense.
3 Nangmanaw yon na pen ngai dawk hettelah ka dei e nahoeh. Bangkongtetpawiteh ka dei tangcoung patetlah nangmouh hoi rei hring hane hoi due hanelah ngainae totouh kaimouh ni nangmouh lung na pataw awh.
Sindikunena izi kuti mupezeke olakwa. Ndinanena kale kuti ife timakuganizirani kwambiri kotero kuti tili pamodzi, ngakhale tikhale moyo kapena timwalire.
4 Kai ni nangmanaw hah na yuem awh dawkvah nangmouh kecu dawk ka kâoup. Kai teh lungpahawinae ka coe dawkvah kaimouh ni ka khangnae rucatnae pueng dawk lunghawinae hoi ka kawi.
Ndimakukhulupirirani kwambiri ndipo ndimakunyadirani kwambiri. Ndikulimbikitsidwa kwambiri; mʼmasautso athu onse, chimwemwe changa chilibe malire.
5 Masidonia ram ka pha navah kâhat nahan tueng kahmawt laipalah alawilah kâtuknae, a thung lah takinae ao teh a voivang hoi rektapnae ka khang awh.
Pakuti titafika ku Makedoniya, sitinapume nʼkomwe, koma tinavutitsidwa mbali zonse. Kunja kunali mikangano, ndipo mʼmitima mwathu munali mantha.
6 Hatei, a thakayounnaw lung ka pahawikung, Cathut ni Titu a tho e lahoi kaimanaw lung na pahawi awh.
Koma Mulungu, amene amatonthoza mtima wopsinjika, anatitonthoza mtima ndi kufika kwa Tito,
7 Titu a tho e dawk hoi dueng lungpahawi e nahoeh. Titu ni nangmouh koehoi a coe e lungpahawinae lahoi lung na pahawi awh. Alouke lahoi dei pawiteh, nangmouh ni na rabui awh e, na lungmathoe awh e, hoi kai koe pahrennae na tawn awh e naw hah Titu ni na dei pouh dawkvah ka ko a nawm.
sikubwera kwake kokhako, komanso mawu achilimbikitso amene analandira kuchokera kwa inu. Iye anatiwuza kuti mukufuna kundiona, zachisoni chanu chachikulu, ndi kudzipereka kwanu kwa ine, motero chimwemwe changa chinachuluka kuposa kale.
8 Ka thut e ca ni nangmouh, lungmathoenae na kapoekung lah kaawm nakunghai thoseh ka lung mathout hoeh. Hote ca teh, nangmouh koe dongdeng lung ka mathout sak nakunghai atuteh lunghawinae bout ka tawn toe.
Ngakhale kalata yanga ija inakupwetekani mtima, sindikudandaula kuti ndinalemberanji. Ngakhale zinandikhudza, ndikudziwa kuti kalata yanga inakupwetekani, koma kwa kanthawi kochepa.
9 Kai ni na patawn e ca ni nangmouh lung na mathoe sak eiteh lunghawihoehnae ka tawn hoeh. Hote ca ni nangmouh dongdeng lung na mathoe sak awh e hah ka hmu navah ka lunghawi hoeh. Hatei nakunghai, atu ka lung ahawi. Hottelah ka ti navah nangmouh na lungmathoe sak dawkvah ka lunghawi e nahoeh. Nangmae lungmathoenae ni nangmouh pan na ka ngai sak dawk doeh. Atangcalah nangmouh teh Cathut ngainae patetlah na lungmathoe awh dawkvah, kaimouh kecu dawk bangcahai na sung awh hoeh.
Koma tsopano ndine wokondwa, osati chifukwa chakuti kalatayo inakupwetekani, koma chifukwa chakuti chisoni chanu chinakuthandizani kutembenuka mtima. Pakuti munamva chisoni monga mmene Mulungu amafunira, choncho simunapwetekedwe mwanjira iliyonse.
10 Bangkongtetpawiteh, Cathutlae lahoi khang e lungmathoenae ni teh rawkphai koe lah awm sak laipalah rungngangnae hmu nahan koe lah pan na kângainae lah doeh ao. Talaivan lungmathoenae teh duenae ka tâcawtkhai e lah ao.
Chisoni chimene Mulungu amafuna chimabweretsa kutembenuka mtima komwe kumabweretsa chipulumutso, ndipo sichikhumudwitsa. Koma chisoni cha dziko lapansi chimabweretsa imfa.
11 Khenhaw! Cathutlae lahoi lungmathoenae ni nangmouh thungvah hoe tawknae, caisaknae, khang thaihoehnae, takinae dounnae, lungthawgnae a tâcokhai. Hahoi, kamsoum lah lawkcengnae kong naw dawk hoi yon thoung nahanelah hno puengpa dawk na hringnae kamnue sak awh toe.
Taonani zimene chisoni chimene Mulungu amafuna chatulutsa mwa inu. Chatulutsa khama lalikulu, chakuthandizani kuti mudzikonze nokha, chakukwiyitsani kwambiri, komanso chakupatsani mantha aakulu. Chakuchititsani kuti mufune kundiona ine, mwakhudzidwa kwambiri ndipo mukufuna kuonetsetsa kuti chilungamo chachitikadi. Pa nkhani yonseyi, mwaonetsadi kuti ndinu osalakwa.
12 Hottelah, kai ni nangmouh koe ka thut e ca teh yonnae ka sak e tami hanelah nahoeh, yon ka khang e hai nahoeh, maimae lathueng nangmae lung thahmeinae naw hah Cathut hmalah namamouh ni roeroe na hmu hanelah doeh ka thut.
Choncho ngakhale ndinakulemberani kalata ija, sindinayilembe ndi chifukwa cha amene analakwayo kapena wolakwiridwa, koma ndinayilemba kuti inuyo muone kudzipereka kwanu kwa ife pamaso a Mulungu.
13 Hatdawkvah maimouh teh lungpahawinae coe awh. Maimae lungpahawinae coe e Titu e a lungthin teh nangmouh abuemlah kecu dawk lunghawi hmu e lah ao teh ahnie lunghawinae dawk hoi maimouh teh puenghoi konawm awh.
Zimenezi zatilimbikitsa kwambiri. Kuwonjezera pa zotilimbikitsazo, tinakondwa kwambiri poona chisangalalo cha Tito, chifukwa nonsenu munamuthandiza kukhazikitsa mtima wake pansi.
14 Kai ni nangmae kong hah Titu koevah kâoupkhai e yeirai awmhoeh. Bangkongtetpawiteh nangmouh koe kaimouh ni ka dei awh e naw pueng teh, lawkkatang lah ao dawkvah, Titu kâoupkhai e naw hai atang e lah a onae a kamnue toe.
Ndinamuwuza kuti ndimakunyadirani, ndipo simunandichititse manyazi. Koma monga zonse zimene tinakuwuzani zinali zoona, tsono zomwe ndinawuza Tito zokunyadirani zinali zoona.
15 Titu ni nangmae lawk a ngâi teh nangmouh ni takinae hoi na dawn awh e heh pouk navah nangmanaw hah lung hoe na pataw awh.
Ndipo chikondi chake pa inu nʼchachikulu kwambiri akakumbukira kuti nonse munali omvera, munamulandira ndi mantha ndi kunjenjemera.
16 Kai ni bangpueng dawk nangmanaw na tang awh dawkvah ka konawm.
Ndine wokondwa kuti ndingathe kukukhulupirirani pa zonse.