< 2 Kawrin 11 >
1 Kaie pathunae hah dongdeng na panguep awh nahanlah na ngaikhai awh. Dongdeng na panguep awh haw.
Ndikukhulupirira kuti mupirira nako pangʼono kupusa kwanga. Chonde tandipirirani!
2 Cathutlae dipmasin e patetlah nangmouh hanelah ka dipma. Nangmouh teh kathounge tanglakacuem patetlah Khrih koe poe hanlah, hote buet touh dueng e vâ koe na ham sak toe.
Nsanje imene ndimakuchitirani ndi yofanana ndi ya Mulungu. Ndinakulonjezani mwamuna mmodzi yekha, mwamunayo ndiye Khristu, kuti ndidzakuperekeni inuyo kwa Iyeyo monga namwali wangwiro.
3 Tahrun ni amae huengo e lahoi Evi a dumyen e patetlah Khrih lung na patawnae lungthin yout na kâhat awh langvaih tie ka tâsue.
Koma ndikuopa kuti monga Hava ananyengedwa ndi kuchenjera kwa njoka, mitima yanunso ingasocheretsedwe kuleka nʼkudzipereka moona mtima ndi modzipereka kwenikweni kwa Khristu.
4 Nangmanaw koe ka tho e taminaw ni kaimouh ni ka pâpho awh hoeh e alouke Jisuh kong a dei awh nakunghai thoseh, nangmouh ni na coe awh hoeh rae muitha a coe awh nakunghai thoseh, na thai boi awh hoeh rae kamthang na thai awh nakunghai thoseh, ahni hah panguep hanlah ao.
Pakuti ngati wina abwera kwa inu nalalikira Yesu wina wosiyana ndi Yesu amene tinamulalikira, kapena ngati mulandira mzimu wina wosiyana ndi Mzimu amene munalandira, kapena uthenga wabwino wina wosiyana ndi umene munawuvomereza, inuyo mumangolandira mosavuta.
5 Kai teh kalenpounge gunceinaw hlak bet ka rahnoum hoeh mue ka ti.
Komatu sindikuganiza kuti ndine wotsika kwambiri kwa “atumwi apamwamba.”
6 Lawk deinae koelah kathoumhoeh nakunghai thoumthainae koe lah ka rahnoum hoeh. Nangmouh koe bangpueng dawk kacaipinlah kamnue sak toe.
Mwina ndikhoza kukhala wosaphunzitsidwa kayankhulidwe, koma ndili ndi chidziwitso. Izi tinakufotokozerani momveka bwinobwino.
7 Nangmouh ni na oup awh nahanlah ka ka rahnoum teh, Cathut e kamthang kahawi hah nangmouh koe ayawmlah pâpho e lahoi ka payonpakai e o maw.
Kodi linali tchimo kwa ine kudzichepetsa nʼcholinga chakuti ndikukwezeni pamene ndinkalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu kwa inu mwaulere?
8 Nangmae thaw ka tawk hanelah alouke kawhmounnaw koehoi kutphu hei laihoi nangmouh na lawp a maw.
Ndinkalanda mipingo ina pomalandira thandizo kwa iwo kuti ndikutumikireni.
9 Nangmouh hoi rei o teh buet buet touh ka panki nah apihai ka tarawk hoeh. Bangkongtetpawiteh, Masidonia ram lahoi ka tho e hmaunawnghanaw ni ka panki e naw na poe awh. Nangmouh tarawk laipalah doeh ka o. Hmalah haiyah poe ka kâhruetcuet han.
Ndipo pamene ndinali pakati panu, nditasowa kanthu, sindinalemetse munthu aliyense, pakuti abale ena amene anachokera ku Makedoniya anandipatsa zonse zimene ndinkazisowa. Ndayesetsa kuti ndisakhale cholemetsa kwa inu mʼnjira ina iliyonse, ndipo ndidzapitiriza kutero.
10 Khrih e a lawkkatang kai thung ao e patetlah Akhaia ram dawkvah, hettelah kai ka kâoupkhai e heh apinihai cakâ thai hoeh.
Kunena moona mtima molingana ndi chilungamo cha Khristu chimene chili mwa ine, palibe amene angandiletse kudzitamandira mʼzigawo za ku Akaya.
11 Bangkongtetpawiteh, kai ni nangmouh lung na pataw hoeh dawk maw. Nangmouh kai ni lungpataw e hah Cathut ni a panue.
Nʼchifukwa chiyani ndikutero? Kodi nʼchifukwa choti sindikukondani? Mulungu akudziwa kuti ndimakukondani!
12 Kâoup han kangainaw ni a kâoup awh hoeh nahanelah, kâoupnaw ni hai kai patetlah hmantang a sak awh nahanelah, ka sak tangcoung e patetlah pou ka sak han rah.
Ndipo ndipitiriza kuchita zomwe ndikuchitazi nʼcholinga chakuti ndisapereke mpata kwa amene akufuna kupezera mwayi woti afanane nafe pa zinthu zimene iwowo amadzitamandira.
13 Bangkongtetpawiteh, ahnimanaw teh guncei kaphawknaw doeh. Khrih e guncei patetlah a kâsak awh teh, dumyennae thaw katawknaw lah ao awh.
Pakuti anthu oterewa ndi atumwi onama, antchito achinyengo, odzizimbayitsa ngati atumwi a Khristu.
14 Hetheh kângairukhai hane na hoeh, Setan patenghai ka ang e kalvantami boiboe lah a kâsak.
Sizododometsa zimenezi, pakuti Satana mwini amadzizimbayitsa kuoneka ngati mngelo wowunikira anthu.
15 Hat pawiteh, ahnimae sayanaw hai lannae kamthang ka pâpho e lah kâsak pawiteh, bangmouh dei han kaawm. Ahnimouh teh amamouh ni a tawk awh e patetlah a hnukteng e hnin navah a tawk e patetlah a khang awh han doeh.
Nʼzosadabwitsa tsono ngati atumiki ake akudzizimbayitsa ngati otumikira chilungamo. Matsiriziro awo adzalandira zoyenerana ndi ntchito zawo.
16 Kai ni bout ka dei e teh, apinihai tamipathu tet hanh naseh. Kai kâoupnae younca ao thai nahan, tamipathu patetlah na pouk awh nateh panguep awh.
Ndibwereze kunena kuti, wina aliyense asandiyese chitsiru. Koma ngati mutero, mundilandire monga mmene mukhoza kulandirira chitsiru, kuti ndinyadirepo pangʼono.
17 Hettelah kai ni ka dei e lawk heh Bawipa ni a dei e patetlah ka dei e nahoeh. Ka pathu e patetlah taranhawi laihoi kâoup teh ka dei e doeh.
Kudzinyadira kwangaku, sindikuyankhula monga mmene Ambuye akufunira koma ngati chitsiru.
18 Tami pueng ni teh talai ngainae dawk kâoupkâpawi dawkvah kai haiyah kâoupkâpawi van e doeh.
Popeza ambiri akudzitama monga dziko lapansi limachitira, inenso ndidzitamanso.
19 Nangmouh teh na lungang awh dawkvah, tamipathunaw hah lunghawicalah na panguep thai awh.
Inu mumalolera kukhala ndi zitsiru mokondwera chifukwa mumati ndinu anzeru!
20 Ayânaw ni nangmanaw pueng san lah na ta awh, na yo awh, hnopai na lawp awh, na yue awh, na tambei awh navah, na panguep awh.
Kunena zoona mumangololera aliyense; amene amakusandutsani akapolo, kapena amene amakudyerani masuku pamutu, kapena amene amakupezererani, kapena amene amadzitukumula, kapena amene amakumenyani khofi.
21 Kai teh hot patetlah ka tawk sak hoeh nahanlah ka tha a youn tangngak. Hatei tami buetbuet touh ni hno buetbuet touh dawk kâoupkhai pawiteh, kai hai kâoupkhai van han telah kapathunaw e patetlah ka dei.
Ndikuvomera mwamanyazi kuti ife sitinali olimba mtima kuti nʼkuchita zinthu zimenezi. Ndikuyankhula ngati chitsiru kuti chimene wina aliyense akhoza kudzitama nacho, Inenso ndikhoza kudzitama nachonso.
22 Ahnimanaw teh Hebru tami namaw. Kai hai doeh. Isarel taminaw maw. Kai hai doeh. Abraham catounnaw maw. Kai hai doeh.
Kodi iwo ndi Ahebri? Inenso ndine Mhebri. Kodi iwo ndi Aisraeli? Inenso ndine Mwisraeli. Kodi iwo ndi zidzukulu za Abrahamu? Inenso ndine mdzukulu wa Abrahamu.
23 Khrih e a san maw, ahnimanaw hlak vah kai teh ka taluehnawn lah ka o telah ka pathu e patetlah hoi ka dei. Ahnimanaw hlak hoe ka panki teh, avai moikapap thongim na pabo awh, moikapap na hem awh, due han totouh khangnae atuhoitu ka kâhmo.
Kodi iwo ndi atumiki a Khristu? Ndikuyankhula ngati wamisala. Ine ndine woposa iwowo. Ndagwira ntchito kwambiri kupambana iwo, ndakhala ndikuyikidwa mʼndende kawirikawiri, ndakwapulidwapo kwambiri, kawirikawiri ndinali pafupi kufa.
24 Judahnaw kut dawk hoi avai 40 vaitouh vout hemnae vai panga touh ka khang toe.
Andikwapulapo kasanu zikoti zija za Ayuda, makumi anayi kuchotsapo chimodzi.
25 Ruitaboung hoi vai thum touh na hem awh. Talung hoi vai touh na dêi awh. Long vai thum touh a kamko teh tui van hnin touh hoi rum touh ka o.
Katatu anandimenya ndi ndodo. Kamodzi anandigendapo miyala. Katatu sitima yathu ya panyanja inasweka, ndipo ndinakhala usiku ndi usana ndi kuyandama pa nyanja.
26 Kahlong voutsout ka ceinae koe tuipui rakanae koehoi runae, dingcanaw koehoi runae, ka miphunnaw koehoi runae, Jentelnaw koehoi runae, kho thung kâhmo e runae, kahrawngum kâhmo e runae, tuipui dawk kâhmo e runae, hmaunawngha lah ka kâsaknaw koehoi runae, het patetlah e runae naw ka ka hmo.
Ndakhala ndikuyenda maulendo ataliatali. Moyo wanga wakhala ukukumana ndi zoopsa pa mitsinje, zoopsa za achifwamba, zoopsa zochokera kwa abale anga Ayuda, zoopsa zochokera kwa anthu akunja. Ndinakumana ndi zoopsa mʼmizinda, mʼmidzi, pa nyanja, ndi pakati pa abale onyenga.
27 Thapatungnae hoi patangnae, atuhoitu ihmuhnapahlanae, kahaikahlam lah onae, pâding ni karuemnae, caicinae hai ka kâhmo.
Ndakhala ndikugwira ntchito molimbika ndipo kawirikawiri ndakhala ndikuchezera usiku wonse osagona. Ndakhala ndikumva njala ndi ludzu ndipo kawirikawiri ndakhala wopanda chakudya. Ndakhala ndi kuzizidwa ndi wosowa zovala.
28 Hote runae hloilah kawhmounnaw hanelah lungpuennae ni hai hnintangkuem na ratet.
Kuwonjezera pa zonsezi, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa chipsinjo cha nkhawa ya mipingo yonse.
29 Ayânaw a thayoun navah ka thayoun laipalah ka o thai han maw. Ayânaw a payonpakai navah ka lungpuen laipalah ka o thai han namaw.
Ndani ali wofowoka, ine wosakhala naye mʼkufowoka kwakeko? Ndani amene mnzake amuchimwitsa, ine wosavutika mu mtima?
30 Kai ni kâoup pawiteh kama e ka thayounnae dawk ka kâoup han.
Ngati nʼkoyenera kudzitamandira, ndidzadzitamandira pa zinthu zimene zimaonetsa kufowoka kwanga.
31 Kai teh laithoe ka dei hoeh tie teh Bawipa Jisuh Khrih e napa, a yungyoe yawhawinae katawnkung, Cathut ni a panue doeh. (aiōn )
Mulungu, Atate a Ambuye Yesu, amene tiyenera kumutamanda nthawi zonse, akudziwa kuti sindikunama. (aiōn )
32 Damaskas kho kaawm e siangpahrang Aretas kut rahim kaawm e khobawi ni kai na man sak hanlah a kâcai navah, longkha khoup a khan awh.
Ku Damasiko, bwanamkubwa woyimira Mfumu Areta, anayika alonda kuzungulira mzinda wonse kuti andigwire.
33 Khobawi e kut dawk hoi hlout thai nahanlah, a hnukkâbangnaw ni tapawm thung na ta awh teh kho thung hoi rapan alawilah na pabo awh teh, na yawng sak awh.
Koma abale anandiyika mʼdengu nanditsitsira pa chipupa kudzera pa zenera la mpandawo, motero ndinapulumuka mʼmanja mwake.