< 2 Setouknae 28 >

1 Ahaz teh siangpahrang a bawi na kum 20 touh boung a pha, Jerusalem kum 16 touh a uk. A na pa Devit patetlah BAWIPA mithmu vah hawinae sak hoeh.
Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
2 Isarel siangpahrang naw e lamthung a dawn teh Baal hanelah meikaphawknaw a sak.
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
3 Hinnom capa e thingyei yawn dawk hmuitui hmai a sawi. BAWIPA ni Isarelnaw hmalah a pâlei e miphunnaw ni, panuetthopounge hno ouk a sak awh e patetlah a canaw hmai hoi thuengnae a sak.
Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
4 Hmuenrasang hoi monsomnaw hoi thingkung rahim tangkuem vah, thuengnae a sak teh hmuitui hmai a sawi.
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
5 Hatdawkvah, Cathut ni Siria siangpahrang kut dawk a poe. A tuk awh teh a taminaw moikapap san lah a man awh teh, Damaskas lah a ceikhai awh. Isarel siangpahrang kut dawk hai a poe teh ahni ni moikapap a thei.
Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
6 Hahoi Remaliah capa Pekah ni Judah ram dawk hnin touh dawk 120, 000 a thei, abuemlah hoi tami tarankahawinaw seng doeh. Bangkongtetpawiteh, mintoenaw e BAWIPA Cathut a hnoun awh dawk doeh.
Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
7 Hahoi Ephraim tami athakaawme Zikhri ni siangpahrang capa Maaseiah hoi imthung kahrawikung Azrikam hoi Elkanah, siangpahrang kabawmkungnaw a thei awh.
Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
8 Isarelnaw ni a hmaunawngha 200, 000 touh a manu, a capanaw hoi a canunaw san lah a hrawi awh. Hno moikapap a lawp awh teh Samaria lah a ceikhai awh.
Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
9 Hatei, hote hmuen koe BAWIPA e profet ao teh, a min teh Oded doeh. Samaria lahoi ka tho e ransanaw hmalah a cei teh, ahnimouh koe, khenhaw! na mintoenaw e BAWIPA Cathut teh Judahnaw koe a lungkhuek dawkvah, nangmae kut dawk na poe awh.
Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
10 Hahoi Judah hoi Jerusalem e taminaw sannu sanpa lah coung sak hanelah na noe awh. Hatei, namamouh hai BAWIPA Cathut hmalah yonpen lah letlang na o awh van nahoehmaw.
Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
11 Hatdawkvah, ka lawk tarawi awh nateh, na hmaunawngha san lah na man e naw hah ban sak awh leih. Bangkongtetpawiteh, BAWIPA e lungkhuek kamannae teh nangmae lathueng vah ao telah atipouh.
Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
12 Hahoi, Ephraim kahrawikung, Johanan capa Azriah, Meshillemoth capa Berekhiah, Shallum capa Hezekiah, Hadlai capa Amasa, naw ni tarantuknae koehoi kathonaw hah kangdue laihoi a ngang awh.
Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
13 Ahnimouh koe sannaw na kâen thai awh mahoeh. Bangkongtetpawiteh, BAWIPA lungkhuek sak awh toe. Mamae yonnae hoi yonpennae hah thapsin hanlah bout na noe awh. Yonpennae a len poung toe, Isarelnaw koe lungkhuek kamannae ao telah atipouh awh.
Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
14 Hottelah ransanaw ni kahrawikungnaw hoi tamimayanaw e hmalah san hoi lawphnonaw hah a cei takhai awh.
Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
15 Hahoi min a kaw e naw pueng a thaw awh teh, sannaw hah a ceikhai awh teh, lawphno a la awh e hnicunaw hah, tawngtai lah kaawm e naw hah a khohna sak awh. Khokkhawm a khawm sak awh teh, canei a poe awh teh satui a hluk awh. Tami thakayounnaw hah la dawk a kâcui sak awh teh, a hmaunawnghanaw onae koe Jeriko kho tie samtue khopui dawk a thak awh teh, ahnimouh teh Samaria kho lah a ban awh.
Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
16 Hatnae tueng dawk siangpahrang Ahaz ni Siria siangpahrang koevah, ama kabawp hanelah tami a patoun.
Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
17 Edomnaw ni Judahnaw a tuk awh teh, san lah bout a man awh.
Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
18 Filistinnaw ni hai a rahim lae ram hoi akalae Judah ram, Bethshemesh, Aijalon, Gederoth, Sokoh, hoi khotenaw; Timnah hoi khotenaw; Gimzo hoi khotenaw a la awh teh, hote hmuen dawk ao sin awh.
Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
19 Isarel siangpahrang Ahaz kecu dawk BAWIPA ni Judah hah rahim lah a pabo. Bangkongtetpawiteh, ahni ni Judahnaw e pouknae a raphoe pouh teh, BAWIPA hanelah yuemkamcu hoeh lah ao sak.
Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
20 Siria siangpahrang Tiglathpileser hai ahni koe a tho teh kabawm laipalah lungrei hoe a thai sak.
Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
21 Ahaz ni BAWIPA im, siangpahrang im hoi kahrawikungnaw kho hoi hnopai a la teh, Siria siangpahrang a poe, Hatei kabawm ngai kalawn hoeh.
Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
22 Khopouk a deng nahaiyah siangpahrang Ahaz teh, BAWIPA koe yuemkamcu hoeh lah hoehoe ao. Hethateh, Ahaz siangpahrang e a coungnae doeh.
Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
23 Ama ka tâ e Damaskas e cathut koe thuengnae a sak teh, Siria siangpahrang cathutnaw ni a kabawp awh dawkvah, na kabawp van hanelah ahnimouh koe thuengnae sak hanelah ao telah a ti.
Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
24 Ahaz ni Cathut im dawk hnopai pueng a pâkhueng teh, reprep koung a dei. BAWIPA im thonaw koung a taren teh, Jerusalem takin pueng koe thuengnae khoungroe a sak.
Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
25 Judah ram kho moikapap koe cathut alouknaw hanlah hmuitui sawi nahane hmuenrasang a sak teh, a na mintoenaw e Cathut hah a lungkhuek sak.
Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
26 A tawksaknae thung dawk kaawm rae pueng hoi a khosaknae pueng kamtawng hoi apout totouh, khenhaw! Judah hoi Isarel siangpahrangnaw e lairui thutnae dawk thut lah ao.
Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
27 Ahaz teh a na mintoenaw koe a i teh, Jerusalem khopui dawk a pakawp awh. Hatei, Isarel siangpahrangnaw e phuen dawk nahoeh. Hahoi a capa Hezekiah ni a yueng lah a bawi.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Setouknae 28 >