< 1 Jawhan 3 >

1 Cathut e canaw telah kaw e lah o awh nahanelah, Cathut ni maimouh banghloimaw lungpataw awh, tie hah pouk a haw! Talai taminaw ni Cathut hah a panue awh hoeh dawkvah, maimouh hai na panuek awh hoeh.
Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye.
2 Ka lungpataw e naw: atuvah maimouh teh Cathut e ca lah o awh. Ato hmalah teh bangtelamaw o awh han tie hah kamnuek hoeh rah. Hatei Bawipa Jisuh ama a kamnue toteh, ama hoi kâvan awh han. Bangkongtetpawiteh, Bawipa ama a coung e patetlah hmu awh han.
Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili.
3 Hottelah, ka ngaihawi e tami teh Bawipa a thoung e patetlah amahoima a kamthoung.
Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.
4 Yonnae ka sak e tami teh kâlawk a ek. Sak payonnae teh kâlawk eknae doeh.
Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo.
5 Bawipa ni maimae yonnae pueng ceikhai hanelah a tho toe tie hah na panue awh. Bawipa dawk yonnae awm hoeh.
Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo.
6 Bawipa dawk kahring e tami teh, yonnae pou sak hoeh. Yonnae pou ka sak e tami teh, Bawipa hah hmawt hoeh rah.
Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.
7 Ka canaw: apihai kâdum sak awh hanh. Apihai lannae nuen ka tarawi e teh Bawipa a lan e patetlah a lan.
Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama.
8 Kahraimathout teh ahmaloe hoi yonnae ka sak e lah ao dawkvah, apipatet hai yonnae ka sak e teh kahraimathout hoi a kâkuet. Cathut Capa a tho ngainae teh kahraimathout thaw tawk raphoe pouh hane doeh.
Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi.
9 Cathut ni a khe e tami teh, yonnae pou sak hoeh. Bangkongtetpawiteh, ahni dawk Cathut e cati a o. Ahni teh, Cathut ni a khe e lah ao dawkvah, yonnae pou sak thai hoeh.
Aliyense amene ndi mwana wa Mulungu, sachimwirachimwira, popeza mbewu ya Mulungu ili mwa iye, sangathe kuchimwa, chifukwa ndi mwana wa Mulungu.
10 Hot patetlah e noutnae lahoi yah, Cathut e a canaw hoi kahraimathout e a canaw teh a kamnue awh. Lannae ka tarawi hoeh e, mae hmaunawngha lungpataw hoeh e teh, Cathut hoi kâkuen hoeh.
Mmenemu ndi mmene timadziwira ana a Mulungu ndi amene ali ana a mdierekezi. Aliyense amene sachita chilungamo si mwana wa Mulungu; ngakhalenso amene sakonda mʼbale wake.
11 Nangmouh ni hmaloe hoi na thai a tangcoung e kamthang kahawi hateh, buet touh hoi buet touh lungkâpataw awh han tie hah doeh.
Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake.
12 Kahrai hoi kâkuen niteh a nawngha ka thet e Kain patetlah awm hanh awh. Kain ni bangkongmaw a nawngha a thei tetpawiteh, amae tawksak e teh lan hoeh, a nawngha e tawksak e teh a lan dawk doeh.
Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama.
13 Hmaunawngha naw: talaivan taminaw ni na ka hmawt ngaihoeh nakunghai, na kângairu awh hanh.
Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu.
14 Maimouh teh hmaunawngha reira lungkâpataw awh dawkvah, duenae koehoi hringnae koe lah, raka awh toe tie kâpanue awh. Ma e hmaunawngha lungpataw hoeh e tami teh, duenae dawk doeh a hring rah.
Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa.
15 Ma e hmaunawngha lung ka pataw hoeh e tami teh, tami ka thet e lah doeh ao. Tami ka thet e tami buet touh dawk boehai, a yungyoe hringnae awmhoeh tie hah nangmouh ni na panue awh. (aiōnios g166)
Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha. (aiōnios g166)
16 Khrih ni maimouh hane kecu dawk, a hringnae a pasoung e khet navah, a lungpatawnae hah panue awh. Maimouh ni hai hmaunawngha reira hanelah, hringnae pasoung hanlah ao.
Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu.
17 Apipatethai talaivan hnopai a tawn nahlangva vah, a hmaunawngha a roedeng e hah a hmu ei, paawt pawiteh, ahni dawk Cathut lungpatawnae bangtelamaw khuet ao han vaw.
Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu?
18 Canaw: maimouh teh lawk hrawng hoi dueng laipalah, tawksaknae hoi lawkkatang lahoi lungpataw awh sei.
Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi.
19 Hottelah lungpataw awh pawiteh, lawkkatang hoi kâkuet awh toe tie hah na panuek awh vaiteh, mamae lung ni yon na kapen nakunghai, Cathut hmalah lungtangnae ao sak han.
Pamenepo tidzadziwa kuti tili pa choonadi ndipo tidzakhala okhazikika mtima pamaso pa Mulungu,
20 Cathut teh maimae lung hlak a len dawkvah, hnocawngca pueng a panue.
nthawi zonse pamene mtima wathu utitsutsa. Pakuti Mulungu ndi wamkulu kuposa mitima yathu ndipo Iye amadziwa zonse.
21 Ka lungpataw e naw: mae lung ni yon na pen awh hoehpawiteh, Cathut hmalah taranhawinae teh tawn awh toe.
Anzanga okondedwa, ngati mitima yathu sikutitsutsa, tili nako kulimbika mtima pamaso pa Mulungu.
22 Maimouh ni kâpoelawknaw ngâi awh teh, a ngai e patetlah tarawi awh pawiteh, ratoum awh e pueng Cathut koehoi hmu awh han.
Ndipo timalandira chilichonse chimene tichipempha kwa Iye, chifukwa timamvera malamulo ake ndi kuchita zimene zimamukondweretsa.
23 Cathut e kâpoelawk tie hateh Capa Jisuh Khrih min yuem han tie hoi ahni ni na dei pouh e patetlah buet touh hoi buet touh lungkâpataw awh han tie hah doeh.
Ndipo lamulo lake ndi ili: kukhulupirira dzina la Mwana wake, Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga Iye anatilamulira.
24 Kâpoelawknaw ka tarawi e tami teh, Cathut thung ao teh, ahnimouh thung Cathut ao. Maimouh koe na poe e Kathoung Muitha lahoi, Cathut teh maimouh dawk ao tie panue awh.
Iwo amene amamvera malamulo ake amakhala mwa Iye, ndipo Iye amakhala mwa iwo. Ndipo mmenemu ndi momwe timadziwira kuti Iye akukhala mwa ife. Timadziwa mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa.

< 1 Jawhan 3 >