< La Bu 88 >
1 O Yahweh Pakai, eihuhhing'a ka Pathen Elohim, sunleh nangma kakou in, jan leh nakom kahin nailut ji e.
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Tun kakouna neijah peh'in lang katona neisan peh'in.
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 Ajeh chu kahin khohi boina adim in, thinan eikainai chehcheh e. (Sheol )
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol )
4 Athisa bang bep kahitai, mithahat tah khat athahat na bei nungsang bep kahitai.
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 Amahon mithi lah'a eidalha uvin lhan ah mithi lup'in kalum e. Keima hi suhmil in kaum tai, nami kaihoina a kon in eiki lamang tai.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 Nang in kotong noinung pen athim pen ah neison lha e.
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 Nalung han na gihtah chun eidelphan, hichu twi kinong bangin akinong'in eichup tai.
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 Keima hi doumah in neisem in kagol kapai ho neidelmang peh gamtai. Keima hi thang'ah ka-oh in kitoldoh theilouvin kaum e.
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 Kamit lhin kamit achupmin kho muthei louvin kaum e. O Yahweh Pakai niseh'in na panpina kathum in nami lungsetna ngaichan kakhut teni kahin sange.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Nathil kidang bol hohi mithi dinga phachom ding hinam? Mithi hungthodoh a nathangvah theiding hinam?
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 Lhankhuh a kon in amahon nami ngailutna longlou hi ahin phongdoh theina diuvem? Suhmangna mun'a umhon nakitah nahi aphongdoh theina diuvem?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Muthim'in nathilbol kidang hohi aseiphong nadiuvem? Thil suhmil delna gama umhon na chonphat na hochu aseiphong theina diuvem?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 O Yahweh Pakai nangma kakouve, niseh-a nakom a katao jingding ahi.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 O Yahweh Pakai, ibolla kei nei paidoh hitam? Ibol a kei a kon a naki heimang hitam?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 Kakhang don lai a pat a, kanatna hin thina komcha eina lhutsa ahitan, nagim neina masanga hin thabei leh lungkham tah'in kading e.
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 Nalunghan na tijat umtah chun eilonvuh'in, tijat naumna chun eithabei sah e.
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 Hiche hochun sun nilhum in twisoh bangin kavel a eilon khum un ahi. Muthimhi kakinai pipen kagol in apang un ahi.
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 Nang man ka mite le ka ngailut cheng neilahpeh tai, Thimjing hi kaki naipi pen ka loi chu ahi tai.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.