< Jeremiah 33 >
1 Jeremiah chu akihenna songkul’a aumnalaiyin, Pakai thusei ahenga aniveinan ahung lhungin,
Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
2 Pakaiyin hitin aseiye, Leiset semdohpa Pakai, leiset lim hin gongdoh chule phutdohpa, ama min chu Pakai ahi.
“Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
3 Neikouvin nahou ingting, nangman nahetkhah louhel khonung thuguh kisel ho naseipeh ing kate.
‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
4 Pakai, Israel Pathen in hitin aseiye, Gal douna ding pansatna semna dinga, Jerusalem inho jouse leh leng inpiho jouse abon’a kiphelha soh hel ding ahi.
Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
5 Khopi kimvel’a pansa Babylonte kisatpi din nakigongun, phachom louhel ding ahi. Hiche khopia mite hi abonchauva athisa tobang ahiuve. Ajeh chu kalunghan behseh jeh’a, keiman amahohi suhmang dinga kakoi ahitai. Amaho agitlou behseh jeh’uva, keiman kanung ngat ahitai, ati.
Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
6 Amavang, Jerusalem thohna maha chu, keiman kasuh damding, chule amaho chu chamna leh lungmonna chule khantouna lhingset a, kasemphat ding ahi.
“‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
7 Hitia chu, keiman Judah leh Jerusalem hamphatna kasemdoh’a, chule akhopi jouseu kasahphat kit ding ahi.
Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
8 Chule keima douna’a achonsetnauva kon’a, amaho chu kasuh theng ding, chule keima douna athemmonau kangaidam ding ahiuve.
Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
9 Chuteng, leiset’a namtin vaipi angsung’a, hiche khopi hin, keima dinga kipana, loupina leh jabolna ahin phondoh ding ahi. Chule vannoi miten, hiche khopi dinga thilpha kabolpeh chengse amudoh’uva, amaho kicha-a kihot ding ahiuve.
Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
10 Pakaiyin hitin aseiye, “Nanghon hiche gamhi ahomkeova um’a, gancha leh mihem jong chengthei talou ahi,’’ natiuve. Hijongle Jerusalem khopi leh Judah khopi dangho’a, avel a hiche hohi nahinjah kit diu,
“Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
11 Kipa golnop agin, nuigin, jinei ding mou leh moulang lipa thanop agin, chuleh mipite kipa lasah agin hung kijakit ding ahi. Mihon, Pakai thangvahna’a thilto choiya houin ahinjot’u husa najah diu,’’ Thangvah un, thaneipen Pakai chu, Pakai nunnem, alungset longlou chu atonsot geiya ahi,’’ atidiu ahi. Ajeh chu keiman agamsungu hi, masanglai banga khantou machalna kakoi kit ding ahi, ati.
mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
12 Thaneipen Pakaiyin hitin aseiye, Hiche gamsung hi ahomkeo leh, mihem leh ganchaho chenmonasa hita jongle, hiche gamsunga hi avel’a hamhing hung kehdoh kit’a, kelngoi chinghon akelngoiteu vahna leh akicholdohnau mun hung hiding ahi.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
13 Chutengle, thinglhang gam khopi ho’a, Judah gam thinglhang chan ho’a, Neger gamsung’a, Jerusalem khopi kimvel ho’a, chule Judah gamsung khopi jousea, kelngoi chinghon simsenlou kelngoite akivah diu ahi, tin Pakaiyin aseiye.
Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
14 Pakaiyin aseiye, “Keiman Israel leh Judah tedinga, kanatepna banga, amaho dinga thilpha kabolpeh ding nikho chu ahunglhung e,’’ ati.
“‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
15 Hiche nikho chule, keiman leng David khangguiya kon’a achilhah thengsel khat kalhendoh ding, chule amachun, gamsung pumpia kitah leh dihtah’a vai ahomding, thu atanding ahi.
“‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
16 Hiche nikho chule, Judah kihuhdoh ding chule Jerusalem chu lungmonga umding ahiuve. Chule amin chu, “Idihnau chu Pakai ahi’’ atidiu ahi.
Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
17 Ajeh chu Pakaiyin hitin aseiye, David laltouna’a aitih a toujingding, achilhah khat hungdoh ding ahi.
Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
18 Chule aphat jousea, keima angsung’a kilhaina thilto tohdoh ding leh pumgo thilto halvam ding, thempuho lhasam louva umjing ahiuve.
ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
19 Chujouvin Pakai thusei chu Jeremiah heng ahung lhungin,
Yehova anawuza Yeremiya kuti:
20 Pakaiyin hitin aseiye, ‘Aphat cha’a ahungjing nadinga keiman sun le jan toh kitepna kasemdoh hi; Nanghon nasuhkeh uva sun le jan jong kitepna dungjuiya ahung umlouva ahileh,
Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
21 Chutah lebou chun, kalhacha David toh kitepna kasem chu kisukeh ding ahi. Chutengle ama guiya achilhahte, alaltouna’a vaihom ding chapa aneilou ding chule Levi phunga thempuho toh kitepna kasem jong chuti ding ahi.
Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
22 Chutengle vanthamjol’a ahsite leh twikhanglen pang’a neldi jat simjoulou banga, kalhacha David chilhahte kapunsah’a chule keima kinbol’a pang Levite jong kapunsah ding ahiuve.
Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
23 Chuin Pakaiyin Jeremiah henga hitin aseiye,
Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
24 Mihon, “insung ni Judah le Israel chu Pakaiyin, alhendohsa chu apaidoh ahitai,’’ tia aseiyu khu najah louham? Mihon kamite noise tah in aveuvin, Israel chu namkhat dinga simthei ahitapouve, atiuvin ahi.
“Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
25 Pakaiyin hitin aseiye, Keiman kamite kapaidoh kit sangin, keiman sun le jan chule lei le van umje dingdan kasemtohsa hi, khel jing e;
‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
26 Keiman kalhacha Jacob leh David chilhahte aitih’a kapaidoh kit louding; Chule Abraham, Isaac chule Jacob chilhah ho chunga leng change vaihom ding chu, David guiya kasemdoh jing ding ahi. Keiman amaho khoto ingting, chule agamsung u kasemphat’a kahaosah ding ahiuve, ati.
monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”