< Lampahnah 29 >

1 A hla rhih dongkah hlasae a hnin khat vaengah nangmih ham hmuencim kah tingtunnah om saeh. Nangmih ham tamlung khohnin la a om dongah thohtatnah kah bitat boeih tah saii boeh.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 BOEIPA taengah hmuehmuei botui la saelhung ca vaito pumat, tutal pumat, tu kumkhat ca a hmabuet pumrih neh hmueihhlutnah saii uh.
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Amih kah khocang tah situi neh a thoek vaidam saeh lamtah vaito pumat dongah doh thum, tutal pumat dongah doh nit saeh.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 Tuca pumrhih ham khaw tuca pumat dongah doh at saeh.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Nangmih ham aka dawth la maae ca pumat te boirhaem la om saeh.
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Hlasae kah hmueihhlutnah neh a khocang voel ah, sainoek hmueihhlutnah neh a khocang khaw, a tuisi khaw a laitloeknah bangla BOEIPA taengah hmaihlutnah hmuehmuei botui la om saeh.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 A hla rhih dongkah a hnin rha vaengah nangmih ham a cim tingtunnah om. Te vaengah na hinglu te phaep uh lamtah bitat boeih te saii uh boeh.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 BOEIPA taengah hmueihhlutnah te hmuehmuei botui kuen uh lamtah saelhung vaito ca pumat tutal pumat, tu kum khat ca a hmabuet pumrhih te namamih ham om saeh.
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Situi neh a thoek a khocang vaidam he vaito pumat dongah doh thum, tutal pumat dongah doh nit saeh.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 Tuca pumrhih ham khaw tu pumat dongah doh at, doh at saeh.
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Maae ca pumat te boirhaem la om saeh. Tholh dawthnah boirhaem voel ah sainoek hmueihhlutnah neh a khocang khaw a tuisi khaw om saeh.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 Hla rhih dongkah hnin hlai nga vaengah nangmih ham hmuencim kah tingtunnah om saeh. Thohtatnah bitat boeih tah saii uh boel lamtah BOEIPA ham hnin rhih khuiah khotue te lam uh.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 BOEIPA taengah hmuehmuei botui hmaihlutnah ham hmueihhlutnah a khuen uh vaengkah, saelhung ca vaito pum hlai thum khaw, tutal rhoi khaw, tu kum khat ca hlai li te khaw hmabuet la om saeh.
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Situi neh a thoek a khocang vaidam khaw, vaito pum hlai thum vaengah vaito pumat dongah doh thum, tutal pumnit vaengah tutal pumat dongah doh nit saeh.
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 Tuca hlai li vaengah tuca pumat dongah doh at doh at saeh.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Maae ca pumat te boirhaem la om saeh. Sainoek hmueihhlutnah voel ah a khocang neh a tuisi om saeh.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 A hnin bae dongah saelhung ca vaitotal pum hlai nit, tutal pumnit, tu kum khat ca a hmabuet pum hlai li saeh.
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 A khocang neh a tuisi te laitloeknah bangla amah tarhing ah vaitotal rhoek ham khaw, tutal rhoek ham khaw, tuca rhoek ham khaw om pah saeh.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 Sainoek hmueihhlutnah, a khocang neh a tuisi voel ah maae ca pumat te boirhaem la om saeh.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 A hnin thum dongah vaito pum hlai khat, tutal pumnit, tu kum at ca a hmabuet pum hlai li saeh.
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 A khocang neh a tuisi te laitloeknah bangla amah tarhing ah vaitotal rhoek ham khaw, tutal rhoek ham khaw, tuca rhoek ham khaw om pah saeh.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 Sainoek hmueihhlutnah neh a khocang, a tuisi voel ah maae ca pumat te boirhaem la om saeh.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 A hnin li dongah vaito pumrha, tutal pumnit, tu kum at ca a hmabuet pum hlai li saeh.
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 A khocang neh a tuisi te laitloeknah bangla amah tarhing ah vaitotal rhoek ham khaw, tutal rhoek ham khaw, tuca rhoek ham khaw om pah saeh.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 Sainoek hmueihhlutnah, a khocang neh a tuisi voel ah maae ca pumat te boirhaem la om saeh.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 A hnin nga dongah vaito pumko, tutal pumnit, tu kum at ca a hmabuet pum hlai li saeh.
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 A khocang neh a tuisi te laitloeknah bangla amah tarhing ah vaitotal rhoek ham khaw, tutal rhoek ham khaw, tuca rhoek ham khaw om pah saeh.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 Sainoek hmueihhlutnah, a khocang neh a tuisi voel ah maae ca pumat te boirhaem la om saeh.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 A hnin rhuk dongah vaito pumrhet, tutal pumnit, tu kum at ca a hmabuet pum hlai li saeh.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 A khocang neh a tuisi te laitloeknah bangla amah tarhing ah vaitotal rhoek ham khaw, tutal rhoek ham khaw, tuca rhoek ham khaw om pah saeh.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 Sainoek hmueihhlutnah, a khocang neh a tuisi voel ah maae ca pumat te boirhaem la om saeh.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 A hnin rhih dongah vaito pumrhih, tutal pumnit, tu kum at ca a hmabuet pum hlai li saeh.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 A khocang neh a tuisi te a laitloeknah bangla amah tarhing ah vaitotal rhoek ham khaw, tutal rhoek ham khaw, tuca rhoek ham khaw om pah saeh.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 Sainoek hmueihhlutnah, a khocang neh a tuisi voel ah maae ca pumat te boirhaem la om saeh.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 A hnin rhet dongah tah nangmih ham pahong la om vetih thohtatnah bitat boeih tah saii uh boeh.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Hmueihhlutnah dongah vaitotal pumat, tutal pumat, tu kum khat ca a hmabuet pumrhih te BOEIPA taengah hmaihlutnah hmuehmuei botui la khuen uh.
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 A khocang neh a tuisi te laitloeknah bangla amah tarhing ah vaitotal rhoek ham khaw, tutal rhoek ham khaw, tuca rhoek ham khaw om pah saeh.
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 Sainoek hmueihhlutnah, a khocang neh a tuisi voel ah maae ca pumat te boirhaem la om saeh.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Na olcaeng neh na kothoh lamkah a voel ah, na hmueihhlutnah neh na khocang ham khaw, na tuisi neh na rhoepnah ham khaw nangmih kah khoning vaengah BOEIPA ham saii uh,” a ti nah.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Te dongah BOEIPA loh Moses taengah a cungkuem a uen bangla Moses loh Israel ca rhoek taengah a thui pah.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< Lampahnah 29 >