< Thothuengnah 15 >

1 BOEIPA loh Moses neh Aaron te a voek tih,
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
2 “Israel ca rhoek te voek rhoi lamtah thui pah rhoi. Hlang pakhat te a pumsa dong lamkah pumthim om tih a buk pah vaengah anih te rhalawt coeng.
“Yankhulani ndi Aisraeli ndipo muwawuze kuti, ‘Mwamuna aliyense akakhala ndi nthenda yotulutsa mafinya ku maliseche ake, zotulukazo ndi zonyansa ndithu.
3 Anih kah pumthim te a ti a hnai la om tih a pumsa dongkah aka long pumthim mai khaw, a saa dongah aka kap pumthim mai khaw a ti a hnai la om.
Lamulo lokhudza kudziyipitsira ndi zotuluka ku maliseche a munthu nali: Malisechewo akamatulukabe mafinya, kaya aleka, munthuyo adzakhala wodetsedwa:
4 A hnai loh a hnai thil thingkong khat khat dongah aka yalh khaw aka poeih uh la om vetih anih loh a hnai thil hnopai khat khat dongkah aka ngol khaw aka poeih uh la om.
“‘Bedi lililonse limene munthu wotulutsa mafinyayo agonapo, ndiponso chinthu chilichonse chimene akhalepo chidzakhala chodetsedwa.
5 Anih kah thingkong aka ben boeih long tah a himbai te suk saeh lamtah tui neh sil uh saeh. Anih te khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
Aliyense wokhudza bedi la munthuyo achape zovala zake ndi kusamba. Komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
6 A pum aka hnai loh a ngol thil hnopai dongah aka ngol long khaw a himbai te suk saeh lamtah tui hlu saeh. Anih te khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
Aliyense wokhala pa chinthu chimene munthu wotulutsa mafinyayo anakhalapo, achape zovala zake ndi kusamba. Komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
7 Aka hnai kah a pumsa aka ben long khaw a himbai suk saeh lamtah tui hlu saeh. Anih te khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
“‘Aliyense wokhudza thupi la munthu amene akutulutsa mafinyayo achape zovala zake ndi kusamba. Komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
8 A cuem te a hnai loh a phuh atah a himbai suk saeh lamtah tui hlu saeh. Anih te khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
“‘Munthu wotulutsa mafinya akalavulira malovu munthu wina amene ndi woyeretsedwa, munthu ameneyo achape zovala zake ndi kusamba. Komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
9 A pum aka hnai loh a ngol thil ngoldoelh boeih khaw aka poeih uh la om saeh.
“‘Chilichonse chimene munthuyo akhalira akakwera pa kavalo chidzakhala chodetsedwa.
10 Anih dangkah aka om boeih te aka ben boeih khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh. Tekah hno aka phuei long tah a himbai te suk saeh lamtah tui hlu saeh. Anih te khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
Ndipo aliyense wokhudza chimene anakhalira munthuyo adzakhala wodetsedwanso mpaka madzulo. Aliyense wonyamula chinthucho achape zovala zake ndi kusamba. Komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
11 A pum dongah aka hnai hlang aka taek boeih khaw a kut te tui neh a lae pawt atah a himbai suk saeh lamtah tui hlu saeh. Anih te khaw kholaeh duela aka poeih uh la om saeh.
“‘Munthu wotulutsa mafinyayo akakhudza munthu aliyense asanasambe mʼmanja, wokhudzidwayo achape zovala zake ndi kusamba. Komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
12 Lai am khaw a pum buk loh a ben atah rhek dae saeh. Tedae thing baelyak boeih te tah tui neh lae saeh.
“‘Mʼphika wadothi umene munthu wotulutsa mafinyayo wakhudza awuphwanye, ndipo chiwiya chilichonse chamtengo achitsuke ndi madzi.
13 A pumthim aka buk te a caihcil van atah a ciimnah ham hnin rhih due tae saeh. Te phoeiah a himbai te suk saeh lamtah a pumsa te tui hing neh sil saeh lamtah caihcil saeh.
“‘Munthu wotulutsa mafinyayo akaona kuti wachira, awerenge masiku asanu ndi awiri akuyeretsedwa kwake kenaka achape zovala zake ndi kusamba pa kasupe, ndipo adzayeretsedwa.
14 A hnin rhet dongah vahu phiknit mai khaw, vahui ca phiknit mai khaw amah ham lo saeh. Te phoeiah tingtunnah dap thohka kah BOEIPA mikhmuh la khuen saeh lamtah khosoih taengah pae saeh.
Pa tsiku la chisanu ndi chitatu atenge njiwa ziwiri kapena mawunda a nkhunda awiri ndi kubwera nazo pamaso pa Yehova pa khomo pa tenti ya msonkhano ndipo azipereke kwa wansembe.
15 Te vaengah pakhat te boirhaem la, pakhat te hmueihhlutnah la khosoih loh nawn pah saeh. Te phoeiah anih kah pumthim kongah te khosoih loh BOEIPA mikhmuh ah dawth pah saeh.
Wansembe apereke zimenezo: imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza. Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera machimo a munthu wotulutsa mafinya uja pamaso pa Yehova.
16 Hlang te a yangtui a yae atah a pumsa tom te tui neh sil saeh. Anih te khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
“‘Mwamuna akataya pansi mbewu yake yaumuna, asambe thupi lake lonse. Komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
17 Himbai khat khat mai khaw, maehpho khat khat mai khaw yangtui aka om atah tui neh sil saeh. Anih te khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
Chovala chilichonse kapena chikopa chilichonse pomwe pagwera mbewu yaumunayo achichape, komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo.
18 Huta tongpa a yalh hmaih vaengkah yangtui te khaw tui neh sil rhoi saeh. Amih rhoi khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
Mwamuna akagona ndi mkazi wake nataya mbewu yake yaumuna, onse awiriwo asambe. Komabe adzakhala odetsedwa mpaka madzulo.
19 Huta khaw a pumsa pumthim om tih thii a buk vaengah pumom bangla hnin rhih om saeh. Te vaengah anih aka ben boeih tah kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
“‘Mkazi akakhala wosamba ndipo ikakhala kuti ndi nthawi yake yeniyeni yosamba, adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri. Aliyense amene adzamukhudza adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
20 Pumom vaengkah a yalh thil hnopai boeih khaw aka poeih uh la om tih a ngol thil hnopai boeih te a poeih uh.
“‘Chilichonse chimene mkaziyo agonera pa nthawi yake yosamba chidzakhala chodetsedwa, ndipo chilichonse chimene adzakhalira chidzakhalanso chodetsedwa.
21 Anih kah thingkong aka ben boeih loh a himbai te suk saeh lamtah tui hlu saeh. Anih khaw kholaeh due aka poeih uh la om saeh.
Aliyense wokhudza bedi lake achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
22 A ngol thil hnopai khat khat aka ben boeih long khaw a himbai te suk saeh lamtah tui hlu saeh. Anih khaw kholaeh due poeih uh la om saeh.
Aliyense wokhudza chimene wakhalapo achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
23 A thingkong khaw, anih loh a ngol thil hnopai mai khaw aka ben tah kholaeh due poeih uh la om saeh.
Kaya ndi bedi kapena chinthu china chilichonse chimene anakhalapo, ngati munthu wina akhudza chinthucho, munthuyo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
24 Hlang loh a yalh a yalh puei tih pum a om atah hnin rhih khuiah poeih uh la om saeh. Te vaengah a yalh thil thingkong boeih khaw aka poeih uh la om saeh.
“‘Mwamuna aliyense akagona naye ndipo magazi osamba kwake ndi kumukhudza, munthuyo adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri, ndipo bedi limene wagonapo lidzakhalanso lodetsedwa.
25 Huta he khohnin a sen pumthim la a thii buk tih a pumom tue pawt ah khaw, pumom tue a poeng phoeiah khaw pumthim la a ti a hnai neh hnin takuem a buk atah pumom tue bangla anih te rhalawt la om.
“‘Mkazi akataya magazi masiku ambiri, wosakhala pa nthawi yake yosamba, kapena akamasambabe kupitirira nthawi yake yosamba, mkaziyo adzakhala wodetsedwa nthawi yonse imene akutaya magazi, monga momwe amakhalira pa masiku ake osamba.
26 Pumthim a om tue khuiah a yalh thil thingkong boeih khaw pumom vaengkah thingkong vanbangla om. A ngol thil hnopai boeih khaw pumom tue vaengkah a tihnai vanbangla anih te rhalawt la om ni.
Bedi lililonse limene mkaziyo adzagonapo pa masiku onse pamene ali wotaya magazi, ndiponso chilichonse chimene wakhalira chidzakhala chodetsedwa monga mmene chimakhalira chodetsedwa pa nthawi yake yosamba.
27 Tekah hnopai aka ben boeih khaw a poeih coeng dongah a himbai te suk saeh lamtah tui hlu saeh. Anit khaw kholaeh due poeih uh la om saeh.
Aliyense amene adzakhudza zinthu zimenezo adzakhala wodetsedwa ndipo ayenera kuchapa zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
28 Tedae a pumthim te a caihcil phoeiah hnin rhih hil tae saeh lamtah caihcil saeh.
“‘Nthawi yosamba ikatha, mkaziyo awerenge masiku asanu ndi awiri, ndipo masikuwo akatha adzakhala woyeretsedwa.
29 A rhet hnin dongah vahu phiknit mai khaw vahui ca phiknit mai khaw amah ham lo saeh lamtah tingtunnah dap thohka kah khosoih taengla khuen saeh.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mkaziyo atenge njiwa ziwiri kapena mawunda awiri, ndipo abwere nazo kwa wansembe pa khomo la Tenti ya Msonkhano.
30 Te vaengah pakhat te boirhaem la, pakhat te hmueihhlutnah la khosoih loh nawn saeh. Te phoeiah anih kah a ti a hnai pumthim kongah khosoih loh BOEIPA mikhmuh ah dawth pah saeh.
Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza. Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera mkaziyo pamaso pa Yehova chifukwa cha matenda ake wosamba aja.
31 Israel ca rhoek loh a tihnai khui lamkah cue uh saeh. Te daengah ni amih khui kah ka dungtlungim te a poeih vaengkah amamih kah a tihnai dongah a duek uh pawt eh.
“‘Choncho muwayeretsa ana a Israeli nʼkudetsedwa kwawo kuti angafe pochita tchimo lowadetsa limene polichita limadetsa malo anga wokhalamo amene ali pakati pawo.’”
32 He tah a pum lamloh a hnai neh yangtui aka coe loh a poeih ham,
Amenewa ndi malamulo a munthu amene akutuluka mafinya kumaliseche kwake, komanso a munthu aliyense amene wadetsedwa ndi mbewu yaumuna,
33 a pumom vaengkah hainakthak neh pumthim aka buk ham khaw, tongpa ham neh huta ham khaw, rhalawt taengah aka yalh hlang ham olkhueng ni,” a ti nah.
mkazi wodwala chifukwa cha msambo komanso a mwamuna kapena mkazi amene akutulutsa mafinya kumaliseche kwake ndi mwamuna wogona ndi mkazi amene akusamba.

< Thothuengnah 15 >