< Johan 4 >
1 Jesuh loh Johan lakah hnukbang muep a khueh tih a nuem te Pharisee rhoek loh a yaak uh tila Jesuh loh a ming.
Yesu atazindikira kuti Afarisi amva zoti Iye ankapeza ndi kubatiza ophunzira ambiri kupambana Yohane,
2 Tedae Jesuh amah long ngawn moenih, a hnukbang rhoek long ni a nuem.
(ngakhale kuti Yesuyo sankabatiza, koma ophunzira ake).
3 Judea te pak a hlah tih Galilee la koep cet.
Iye anachoka ku Yudeya ndi kubwereranso ku Galileya.
4 Te vaengah Samaria te a hil phai ham a kuek.
Ndipo Iye anayenera kudutsa mu Samariya.
5 Te dongah Sychar la a khue Samaria kho puei kah Jakob loh a capa Joseph a paek khohmuen taeng te a pha.
Iye anafika mʼmudzi wa Asamariya wotchedwa Sukari, pafupi ndi malo amene Yakobo anapatsa mwana wake Yosefe.
6 Teah te Jakob tuisih om. Te vaengah Jesuh tah yincaehnah lamloh thakthae tih tuisih taengah ngol.
Chitsime cha Yakobo chinali pamenepo ndipo Yesu atatopa ndi ulendo anakhala pansi pambali pa chitsimecho. Nthawi inali pafupifupi ora lachisanu ndi chimodzi masana.
7 Khonoek parhuk tluk a lo vaengah Samaria nu tah tui than la ha pawk. Anih te Jesuh loh, “Ok ham kai m'pae lah,” a ti nah.
Mayi wa Chisamariya atabwera kudzatunga madzi, Yesu anati kwa iye, “Kodi ungandipatse madzi akumwa.”
8 Te vaengah a hnukbang rhoek tah kho khuiah caak lai hamla cet uh.
(Ophunzira ake nʼkuti atapita mʼmudzi kukagula chakudya).
9 Te dongah amah te Samaria nu loh, “Nang tah Judah hlang la aka om loh balae tih Samaria nu la aka om kai taengah ok ham te nan bih,” a ti nah. Judah rhoek neh Samaria rhoek he a doca uh moenih.
Mayiyo anati kwa Iye, “Inu ndinu Myuda ndipo ine ndine Msamariya. Bwanji mukundipempha madzi akumwa?” (Popeza Ayuda ndi Asamariya sankayanjana).
10 Jesuh loh anih te a doo tih, “Pathen kah kutdoe neh nang taengah aka cal te unim tila na ming koinih amah taengah ok ham kai pae lah,’ tila na bih sui tih tui hing nang m'paek suidae,” a ti nah.
Yesu anamuyankha kuti, “Koma iwe ukanadziwa mphatso ya Mulungu ndi Iye amene akukupempha madzi akumwa, ukanamupempha ndipo akanakupatsa madzi amoyo.”
11 Huta loh anih te, “Saya, tuiduen khaw na khueh pawh, tuito khaw a dung la om. Melam kah tui hing nim, na khueh tih?
Mayiyo anati, “Ambuye, Inu mulibe kanthu kotungira madzi ndipo chitsime ndi chakuya. Kodi madzi amoyowo mungawatenge kuti?
12 A pa Jakob lakah tanglue la na om pawtnim? Tuito he amah loh kaimih m'paek tih he lamkah te amah long khaw, a ca rhoek neh a saelhung long khaw a ok,” a ti nah.
Kodi Inu ndinu wamkulu kuposa kholo lathu Yakobo, amene anatipatsa chitsimechi ndipo iye ankamwanso monga anachita ana ake ndi ziweto zake?”
13 Jesuh loh anih te a doo tih, “He kah tui aka o boeih tah koep hal ni.
Yesu anayankha kuti, “Aliyense amene amamwa madzi awa amamvanso ludzu,
14 Tedae kai loh ka paek ham tui te aka o tah kumhal ah hal tlaih mahpawh. Te phoeiah anih ka paek ham tui te tah dungyan hingnah ham anih ah aka phuet tuisih tui la om ni,” a ti nah. (aiōn , aiōnios )
koma aliyense amene adzamwa madzi amene Ine ndidzamupatsa sadzamvanso ludzu. Ndithudi, madzi amene ndidzamupatsa adzakhala kasupe wamadzi wotumphukira ku moyo wosatha.” (aiōn , aiōnios )
15 Amah te huta loh, “Saya, te tui te kai m'pae lah. Te daengah ni tui ka hal pawt vetih tuithan la ka pawk pawt eh?,” a ti nah.
Mayiyo anati kwa Iye, “Ambuye, patseni madzi amenewo kuti ndisadzamvenso ludzu ndi kumabwerabe kuno kudzatunga madzi.”
16 Amah te, “Cet, na va te khue lamtah hela ha lo,” a ti nah.
Iye anamuwuza kuti, “Pita kayitane mwamuna wako ndipo ubwere naye.”
17 Huta loh a doo tih, “Va ka khueh moenih,” a ti nah. Jesuh loh anih te, “Va ka khueh pawh balh na ti.
Iye anayankha kuti, “Ine ndilibe mwamuna.” Yesu anati kwa iye, “Wakhoza ponena kuti ulibe mwamuna.
18 Va panga na khueh coeng dae tahae kah na khueh te na va la a om moenih, oltak te thui saw,” a ti nah.
Zoona nʼzakuti iwe wakhala pa banja ndi amuna asanu, ndipo mwamuna amene uli naye tsopano si wako. Zimene wanenazi ndi zoona.”
19 Huta loh Jesuh te, “Boeipa, nang tah tonghma ni tila kan hmat coeng.
Mayiyo anati, “Ambuye, ine ndazindikira kuti Inu ndinu mneneri.
20 A pa rhoek loh hekah tlang ah bawk uh. Tedae nangmih long tah Jerusalem kah aka om hmuen ah te a bawk ham a kuek na ti uh,” a ti nah.
Makolo athu ankapembedza mʼphiri ili koma inu Ayuda mumati malo amene tiyenera kupembedzera ali ku Yerusalemu.”
21 Jesuh loh anih te, “Huta aw, kai he n'tangnah lah. Tekah a tue ha pawk vaengah hekah tlang pawt ah khaw, Jerusalem pawt ah khaw pa te na bawk uh bitni.
Yesu anati, “Mayi inu khulupirira Ine. Nthawi ikubwera pamene inu simudzapembedza Atate mʼphiri ili kapena mu Yerusalemu.
22 Nangmih loh na bawk uh te na ming uh pawh. Kaimih tah ka bawk uh te ka minguh. Khangnah khaw Judah rhoek lamkah ni a om.
Inu Asamariya mumapembedza chimene simukuchidziwa. Ife timapembedza chimene tikuchidziwa, pakuti chipulumutso nʼchochokera kwa Ayuda.
23 Tedae a tue ha pai tih om coeng. Bawkkung taktak rhoek long tah pa te Mueihla neh oltak dongah a bawk uh ni. Amah aka bawk rhoek van te ni pa loh a toem.
Koma nthawi ikubwera ndipo yafika kale tsopano pamene opembedza woona adzapembedza Atate mu mzimu ndi mʼchoonadi, pakuti opembedza otere ndiwo amene Atate akuwafuna.
24 Pathen tah Mueihla ni. Te dongah amah aka bawk loh mueihla neh oltak ah bawk ham a kuek,” a ti nah.
Mulungu ndi Mzimu, ndipo omupembedza Iye ayenera kumupembedza mu mzimu ndi mʼchoonadi.”
25 Amah te huta loh, “Khrih la a khue Messiah te ha pawk tila ka ming. Te te ha pawk vaengah soeprhaep boeih te kaimih taengah ha puen ni,” a ti nah.
Mayiyo anati, “Ine ndikudziwa kuti Mesiya (wotchedwa Khristu) akubwera. Akabwera, Iye adzafotokoza zonse kwa ife.”
26 Jesuh loh anih te, “Te tah nang taengah aka cal kamah ni,” a ti nah.
Ndipo Yesu anamuwuza kuti, “Amene ndikukuyankhulane, ndine amene.”
27 Te vaengah te a hnukbang rhoek te ha pawk uh tih huta taengah a cal te a ngaihmang uh. Tedae, “Balae na toem tih balae tih anih te na voek?” ti na uh pawh.
Pa nthawi yomweyo ophunzira ake anabwerera ndipo anadabwa kupeza Iye akuyankhula ndi mayi. Koma palibe amene anamufunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” kapena, “Nʼchifukwa chiyani mukuyankhula naye?”
28 Te dongah huta loh a amrhaeng te a toeng tih kho khuila cet.
Kenaka mayiyo anasiya mtsuko wamadzi, nabwerera ku mzinda ndipo anati kwa anthu,
29 Te phoeiah a hlang rhoek te, “Halo uh lah, ka saii boeih aka thui hlang te so uh lah. Anih tah Khrih la om pawtnim?” a ti nah.
“Tiyeni mukaone munthu amene wandiwuza ine zilizonse zimene ndinazichita. Kodi ameneyu sangakhale Khristu?”
30 Te dongah khopuei lamloh cet uh tih amah te a paan uh.
Iwo anatuluka mʼmudziwo ndi kupita kumene kunali Iye.
31 Te rhuet ah amah te hnukbang rhoek loh a dawt uh tih, “Rhabbi, ca laeh saw,” a ti nauh.
Pa nthawi imeneyi ndi kuti ophunzira ake akumukakamiza kuti, “Rabi idyani.”
32 Tedae amih te, “Kai loh caak ham caak ka khueh te na ming uh moenih,” a ti nah.
Koma Iye anawawuza kuti, “Ine ndili ndi chakudya choti ndidye chimene inu simukuchidziwa.”
33 Te dongah hnukbang rhoek loh amamih te, “Khat khat loh a caak koi khuen pah pawtnim,” a ti uh.
Ndipo ophunzira ake anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi alipo wina amene anamubweretsera Iye chakudya?”
34 Jesuh loh amih te, “Kai aka tueih kah kongaih saii ham neh amah kah bibi coeng ham te kai kah cakok la om.
Yesu anati, “Chakudya changa ndikuchita chifuniro cha Iye amene anandituma Ine ndi kumaliza ntchito yake.
35 Nangmih loh, 'Cangah pha ham hlali om pueng tila na ti uh moenih a? Nangmih taengah ka thui, na mik te dai uh lamtah dan uh, hmuenlung te cangaeng neh cangah ham om coeng ke.
Kodi inu simunena kuti, ‘Kwatsala miyezi inayi ndipo kenaka kukolola?’ Ine ndikukuwuzani kuti, tsekulani maso anu ndipo muyangʼane mʼminda! Mbewu zacha kale kuti zikololedwe.
36 Aka at loh thapang a dang tih dungyan hingnah dongah cangthaih a coi coeng. Te daengah ni aka tuh neh aka at loh thikat la a omngaih eh. (aiōnios )
Ngakhale tsopano amene akukolola akulandira malipiro ake, ndipo akututa mbewu ku moyo wosatha kuti wofesa ndi wokolola asangalale pamodzi. (aiōnios )
37 Hekah ol tah oltak pai ni. Aka tuh khaw a tloe, aka at khaw a tloe la om pai.
Nʼchifukwa chake mawu akuti, ‘Wina amafesa ndipo wina amakolola’ ndi woona.
38 Kai loh cangat la nangmih kan tueih te na thakthae moenih, a tloe rhoek tah thakthaeuh. Te dongah amih kah thakthaenah khuiah na kun uh coeng,” a ti nah.
Ine ndinakutumani kukakolola zimene simunagwirire ntchito. Ena anagwira ntchito yolemetsa ndipo inu mwatuta phindu la ntchito yawo.”
39 Huta loh, “Ka saii boeih te kamah taengah a thui coeng, “tila ol a phong. Te dongah kho khui lamkah Samaria rhoek loh Jesuh te muep a tangnah uh.
Asamariya ambiri ochokera mʼmudziwo anakhulupirira Iye chifukwa cha umboni wa mayiyo wakuti, “Iye anandiwuza ine zonse ndinazichita.”
40 Te dongah Samaria rhoek loh amah taengla a pawk uh vaengah amah te amih taengah rhaeh sak ham a bih uh dongah hnin nit pahoi rhaeh.
Choncho Asamariya atabwera kwa Iye, anamuwumiriza Iye kuti akhale nawo, ndipo Iye anakhala nawo masiku awiri.
41 Te vaengah a ol aka tangnah khaw taoe yet.
Ndipo chifukwa cha mawu ake, ena ambiri anakhulupirira.
42 Te phoeiah huta te, “Na olcal dongah ka tangnah uh pawt dae kaimih loh ka yaak uh daengah ni he tah Diklai kah khangkung la om tangtang tila ka ming uh,” a ti nauh.
Iwo anati kwa mayiyo, “Ife sitikukhulupirira chifukwa cha mawu ako okha, koma tsopano ife tadzimvera tokha, ndipo tikudziwa kuti munthu uyu ndithu ndi Mpulumutsi wa dziko lapansi.”
43 Hnin nit phoeiah te lamloh Galilee la cet.
Patatha masiku awiri Iye anachoka napita ku Galileya.
44 Tonghma loh amah tolrhum ah hinyahnah a dang pawt te khaw Jesuh amah loh a phong coeng.
(Tsopano Yesu mwini ananena kale kuti mneneri salandira ulemu mʼdziko lake).
45 Khotue vaengkah Jerusalem ah a saii boeih te a hmuh uh. Amih khaw khotue te a paan uh. Te dongah Galilee la ha pawk vaengah tah Galilee rhoek loh amah a doe uh.
Iye atafika ku Galileya, Agalileya anamulandira. Iwo anali ataona zonse zimene anazichita mu Yerusalemu pa phwando la Paska, pakuti iwonso anali komweko.
46 Te dongah Galilee kah Kana la koep pawk. Te ah ni tui khaw misurtui la a saii. Te vaengah Kapernaum ah capa aka tlo rhalboei pakhat te ana om.
Iye anakafikanso ku Kana wa ku Galileya, kumene anasanduliza madzi kukhala vinyo. Ndipo kumeneko kunali nduna ina ya mfumu imene mwana wake wamwamuna anali chigonere akudwala ku Kaperenawo.
47 Judea lamloh Galilee la Jesuh a pawk te anih loh a yaak vaengah a taeng la cet tih, “Duek hamla aka om a capa te hoeih sak ham ha suntla dae,” tila a bih.
Munthu uyu atamva kuti Yesu wafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya, anapita kwa Iye, namupempha kuti apite akachiritse mwana wakeyo, amene anali pafupi kufa.
48 Te dongah Jesuh loh anih te, “Miknoek neh khobae rhambae na hmuh uh pawt atah na tangnah uh tlaih pawh,” a ti nah.
Yesu anawawuza iwo kuti, “Anthu inu pokhapokha mutaona zizindikiro zodabwitsa, simudzakhulupirira.”
49 Rhalboei loh amah taengah, “Boeipa, ka capa te a duek hlan ah ha suntla dae,” a ti nah.
Nduna ya mfumuyo inati, “Ambuye tiyeni mwana wanga asanafe.”
50 Jesuh loh anih te, “Cet laeh, na capa te hing coeng,” a ti nah. Jesuh loh anih taengah a thui olka te a tangnah dongah tekah hlang khaw cet.
Yesu anayankha kuti, “Pita. Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Munthuyo anakhulupirira mawu a Yesu ndipo ananyamuka.
51 A suntlak neh anih te a sal rhoek loh oepsoeh la a doe uh tih a capa a hing pah te a thui pauh.
Iye ali pa njira, antchito ake anakumana naye, namuwuza kuti mwana wanu uja wachira.
52 Te dongah a then la a om nah a tue te amih taengah a cae. Te vaengah, “Hlaem khonoek parhih vaengah a satloh loh a hlah,” a ti nauh.
Iye atafunsa kuti ndi nthawi yanji imene mwana wake anapeza bwino, iwo anati kwa iye, “Malungo anamusiya iye dzulo pa ora lachisanu ndi chiwiri.”
53 Te dongah Jesuh loh anih te, “Na capa te hing coeng,” a ti nah vaeng kah a tue te te vaeng ah ni tila ana pa loh a ming dongah amah neh a im pum loh a tangnah uh.
Ndipo bamboyo anazindikira kuti iyi inali nthawi yomweyo imene Yesu anati kwa iye, “Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Choncho iye ndi onse a pa banja lake anakhulupirira.
54 He he Judea lamkah loh Galilee la ha pawk vaengah Jesuh loh koep a saii a miknoek pabae ni.
Ichi ndiye chinali chizindikiro chodabwitsa chachiwiri chimene Yesu anachita atafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya.