< Jeremiah 15 >

1 BOEIPA loh kai taengah, “Moses neh Samuel pataeng ka mikhmuh ah pai cakhaw pilnam taengah he ka hinglu a om moenih. Ka mikhmuh lamloh tueih lamtah coe uh saeh.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
2 Tedae nang taengah, “Melam ka coe uh eh?” a ti uh atah amih te thui pah. He tah BOEIPA long ni a thui. Dueknah dongkah ham rhoek te dueknah dongla, cunghang dongkah ham rhoek te cunghang dongla, khokha dongkah ham rhoek te khokha dongla, tamna ham rhoek te tamna la om ni.
Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
3 BOEIPA kah olphong hui tah pali om tih, cunghang neh ngawn ham, ui loh a koeng ham, vaan kah vaa neh diklai rhamsa loh a ngaeh ham neh thup ham te amih ka cawh thil ni.
“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
4 Judah manghai Hezekiah capa Manasseh loh Jerusalem kah a saii kong ah amih te diklai ram boeih ah tonganah neh ngaihuetnah la ka khueh ni.
Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
5 Jerusalem nang soah, unim lungma aka ti vetih, nang hamla unim aka rhaehba ve? Nang kah sadingnah bih ham, unim aka nong ve?
“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
6 Kai he nan phap uh tih a hnuk la na pongpa uh akhaw BOEIPA kah olphong om. Te dongah ka kut he nang soah ka thueng ni. Kohlawt khaw ka ngak coeng dongah nang kan thup ni.
Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
7 Amih te khohmuen vongka ah rha neh ka yah ni. Ka pilnam he a longpuei lamloh ha bal uh pawt cakol la ka milh sak ni.
Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
8 A taengkah nuhmai te tuitunli kah laivin lakah ka tahoeng sak ni. A manu taengah khothun kah aka rhoelrhak tongpang ka khuen pah ni. Khopuei kah lungmitnah te a soah buengrhuet ka cuhu sak ni.
Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
9 Parhih aka cun khaw tahah vetih a hil awt ni. Khothaih pueng ah a khomik te tla rhoe tla vetih yahpoh neh ngam ni. cunghang lamloh a meet te a thunkha kah mikhmuh ah ka paek ni. He tah BOEIPA kah olphong coeng ni,” a ti.
Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
10 Anunae kai aih he. A nu nang loh, kai he khohmuen tom neh tuituknah kah hlang neh olpungkacan kah hlang lam nim nan cun. Ka pu pawt tih kai taengah pu pawt dae a pum la kai n'tap uh.
Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
11 BOEIPA loh, “Nang he kan hlah rhoe kan hlah tang mahpawt nim? A then ham tah yoethae tue vaengah, thunkha neh citcai tue vaengah nang te kan doo tang mahpawt nim?
Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
12 Tlangpuei lamkah thi loh thi neh rhohum a khaem thai a?
“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 Na khorhi tom kah na tholhnah cungkuem dongah mah na khuehtawn neh na thakvoh khaw maeh la ka mop vetih a phu om mahpawh.
Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
14 Ming pawt khohmuen kah na thunkha te kam paan sak ni. Ka thintoek hmai neh nangmih kan hlae vetih na ung uh ni.
Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
15 BOEIPA namah loh na ming. Kai m'poek lamtah kai he n'hip mai. Kai aka hloem rhoek soah kai yueng la phulo nawn. Na thintoek a ueh pawt dongah nim kai nan loh. Nang ham kokhahnah ka phueih he poek.
Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 Na ol a hmuh uh coeng dongah te ni ka caak. Na ol tah na ol la a om dongah kai ham omngaihnah neh ka thinko kohoenah la poeh. Kai taengah caempuei Pathen BOEIPA namah ming ni a khue.
Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 Aka luem tih ka sundaep rhoek kah baecenol dongah ka nuen moenih. Kai he kosi nan hah sak dongah na kut dong bueng ah ni ka ngol.
Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 Balae tih ka thakkhoeihnah om yoeyah a? Ka hmasoe neh aka rhawp loh hoeih ham a aal. Cak uh pawt tih tui hong bangla kai taengah na om khaw na om ve.
Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
19 Te dongah BOEIPA loh he ni a thui. Na mael tih nang taengla ka mael daengah ni ka mikhmuh ah na pai eh. Carhut lakah a phu aka tlo ha thoeng atah kamah ka bangla na om ni. Amih te nang taengla ha mael cakhaw nang te amih taengla na mael mahpawh.
Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 Nang tah pilnam taengah he rhohum vongtung neh a cakrhuet la kang khueh ni. Nang m'vathoh thil cakhaw nang te n'noeng uh mahpawh. Nang khang ham neh nang huul hamla nang taengah ka om. He tah BOEIPA kah olphong ni.
Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
21 Te dongah boethae kah kutrham lamloh nang kang huul vetih hlanghaeng kah kutpha lamloh nang kan tlan ni.
“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

< Jeremiah 15 >